< Job 16 >
1 But Job answered and said:
Pamenepo Yobu anayankha kuti,
2 Of such things as these I have heard enough! Miserable comforters are ye all!
“Ndinamvapo zambiri monga zimenezi; nonsenu ndinu anthu osatha kutonthoza mtima mnzanu.
3 Will there ever be an end to words of wind? What stirreth thee up, that thou answerest?
Kodi mawu anu ochulukawo adzatha? Kodi chikukuvutani nʼchiyani kuti muzingoyankhula mawu otsutsawa?
4 I also might speak like you, If ye were now in my place; I might string together words against you, And shake my head at you.
Inenso ndikanatha kuyankhula monga inu, inuyo mukanakhala monga ndilili inemu; Ine ndikanatha kuyankhula mawu omveka bwino kutsutsana nanu ndi kukupukusirani mutu wanga.
5 I would strengthen you with my mouth, And the consolation of my lips should sustain you.
Ndipo mawu a pakamwa panga akanakulimbikitsani; chitonthozo chochokera pa milomo yanga chikanachepetsa ululu wanu.
6 If I speak, my grief is not assuaged; And if I forbear, it doth not leave me.
“Koma ine ndikati ndiyankhule ululu wanga sukuchepa; ndipo ndikati ndikhale chete, ululu wanga sukuchokabe.
7 For now He hath quite exhausted me; Thou hast desolated all my house!
Ndithudi, Inu Mulungu mwanditha mphamvu; mwawononga banja langa lonse.
8 Thou hast seized hold of me, and this is a witness against me; My leanness riseth up and testifieth against me to my face.
Inu mwandimanga ndipo kundimangako kwakhala umboni; kuwonda kwanga kwandiwukira ndipo kukuchita umboni wonditsutsa.
9 His anger teareth my flesh, and pursueth me; He gnasheth upon me with his teeth; My adversary sharpeneth his eyes upon me.
Mulungu amabwera kwa ine mwankhanza ndipo amadana nane, amachita kulumira mano; mdani wanga amandituzulira maso.
10 They gape for me with their mouths; In scorn they smite me on the cheek; With one consent they assemble against me.
Anthu amatsekula pakamwa pawo kundikuwiza; amandimenya pa tsaya mwachipongwe ndipo amagwirizana polimbana nane.
11 God hath given me a prey to the unrighteous, And delivered me into the hands of the wicked.
Mulungu wandipereka kwa anthu ochita zoyipa ndipo wandiponyera mʼmanja mwa anthu oyipa mtima.
12 I was at ease, but he hath crushed me; He hath seized me by the neck, and dashed me in pieces; He hath set me up for his mark.
Ine ndinali pamtendere, koma Mulungu ananditswanya; anandigwira pa khosi ndi kundiphwanya. Iye anandisandutsa choponyera chandamale chake;
13 His archers encompass me around; He pierceth my reins, and doth not spare; He poureth out my gall upon the ground.
anthu ake oponya mauta andizungulira. Mopanda kundimvera chisoni, Iye akulasa impsyo zanga ndipo akutayira pansi ndulu yanga.
14 He breaketh me with breach upon breach; He rusheth upon me like a warrior.
Akundivulaza kawirikawiri, akuthamangira pa ine monga munthu wankhondo.
15 I have sewed sackcloth upon my skin, And thrust my horn into the dust.
“Ndasokerera chiguduli pa thupi langa ndipo ndayika mphamvu zanga pa fumbi.
16 My face is red with weeping, And upon my eyelids is deathlike darkness.
Maso anga afiira ndi kulira, ndipo zikope zanga zatupa;
17 Yet is there no injustice in my bands. And my prayer hath been pure.
komatu manja anga sanachite zachiwawa ndipo pemphero langa ndi lolungama.
18 O earth! cover not thou my blood, And let there be no hiding-place for my cry!
“Iwe dziko lapansi, usakwirire magazi anga; kulira kwanga kofuna thandizo kusalekeke!
19 Yet even now, behold, my witness is in heaven, And he who knoweth me is on high.
Ngakhale tsopano mboni yanga ili kumwamba; wonditchinjiriza pa mlandu wanga ali komweko.
20 My friends have me in derision, But my eye poureth out tears unto God.
Wondipembedzera ndi bwenzi langa, pamene maso anga akukhuthula misozi kwa Mulungu;
21 O that one might contend for a man with God, As a man contendeth with his neighbor!
iye, mʼmalo mwanga, amamudandaulira Mulungu monga munthu amadandaulira bwenzi lake.
22 For when a few years shall have passed, I shall go the way whence I shall not return.
“Pakuti sipapita zaka zambiri ndisanayende mʼnjira imene sindidzabwerera.”