< Job 15 >

1 Then answered Eliphaz the Temanite, and said:
Pamenepo Elifazi wa ku Temani anayankha kuti,
2 Should a wise man answer with arguments of wind, Or fill his bosom with the east wind?
“Kodi munthu wanzeru angayankhe ndi mawu achabechabe otere, kapena angakhutitse mimba yake ndi mphepo yotentha yochokera kummawa?
3 Should he argue with speech that helpeth him not, And with words which do not profit him?
Kodi angathe kutsutsa ndi mawu opanda pake, kapena kuyankhula mawu opanda phindu?
4 Behold, thou makest the fear of God a vain thing, And discouragest prayer before him.
Koma iwe ukuchepetsa zoopa Mulungu ndipo ukutchinga zodzikhuthulira kwa Mulungu.
5 Yea, thy own mouth proclaimeth thy iniquity, Though thou choosest the tongue of the crafty.
Tchimo lako ndiye likuyankhulitsa pakamwa pakopo; ndipo watengera mayankhulidwe a atambwali.
6 Thy own mouth condemneth thee, and not I; Thy own lips testify against thee.
Pakamwa pakopo ndiye pakukutsutsa osati pakamwa panga; milomo yakoyo ikukutsutsa.
7 Art thou the first man that was born? Wast thou formed before the hills?
“Kodi ndiwe munthu woyamba kubadwa? Kodi unalengedwa mapiri asanalengedwe?
8 Hast thou listened in the council of God, And drawn all wisdom to thyself?
Kodi unali mʼgulu la alangizi a Mulungu? Kodi ukudziyesa wanzeru ndiwe wekha?
9 What dost thou know, that we know not also? What dost thou understand, that is a secret to us?
Kodi iwe umadziwa chiyani chimene ife sitichidziwa? Kodi iwe uli ndi chidziwitso chanji chimene ife tilibe?
10 With us are the aged and hoary-headed; Much older than thy father.
Anthu a imvi ndi okalamba ali mbali yathu, anthu amvulazakale kupambana abambo ako.
11 Dost thou despise the consolations of God, And words so full of kindness to thee?
Kodi mawu otonthoza mtima ochokera kwa Mulungu sakukukwanira, mawu oyankhula mofatsawa kwa iwe?
12 Why hath thy passion taken possession of thee? And why this winking of thine eyes?
Chifukwa chiyani ukupsa mtima, ndipo chifukwa chiyani ukutuzula maso ako,
13 For against God hast thou turned thy spirit, And uttered such words from thy mouth.
moti ukupsera mtima Mulungu ndi kuyankhula mawu otero pakamwa pako?
14 What is man, that he should be pure, And he that is born of woman, that he should be innocent?
“Kodi munthu nʼchiyani kuti nʼkukhala woyera mtima kapena wobadwa mwa amayi nʼchiyani kuti nʼkukhala wolungama mtima?
15 Behold, He putteth no trust in his ministering spirits, And the heavens are not pure in his sight;
Ngati Mulungu sakhulupirira ngakhale angelo ake, ngakhale zakumwamba sizoyera pamaso pake,
16 Much less, abominable and polluted man, Who drinketh iniquity as water.
nanga kuli bwanji munthu amene ndi wonyansa ndi wa njira zokhotakhota, amene kuchita zoyipa kuli ngati kumwa madzi.
17 Hear me, and I will show thee, And that which I have seen will I declare;
“Mvetsera kwa ine ndipo ndidzakufotokozera; ndilole ndikuwuze zimene ndaziona,
18 Which the wise men have told, And not kept concealed, as received from their fathers;
zimene anandiphunzitsa anthu anzeru, sanandibisire kalikonse kamene anamva kuchokera kwa makolo awo.
19 To whom alone the land was given, And among whom not a stranger wandered.
(Ndi kwa iwowa kumene dziko lino linaperekedwa pamene panalibe mlendo wokhala pakati pawo).
20 “All his days the wicked man is in pain; Yea, all the years, that are laid up for the oppressor.
Munthu woyipa amavutika ndi masautso masiku onse a moyo wake, munthu wankhanza adzavutika zaka zake zonse.
21 A fearful sound is in his ears; In peace the destroyer cometh upon him.
Amamva mawu owopsa mʼmakutu mwake, pamene zonse zikuoneka ngati zili bwino, anthu achifwamba amamuthira nkhondo.
22 He hath no hope that he shall escape from darkness; He is set apart for the sword.
Iye sakhulupirira kuti angathe kupulumuka ku mdima wa imfa; iyeyo ndi woyenera kuphedwa.
23 He wandereth about, seeking bread; He knoweth that a day of darkness is at hand.
Amangoyendayenda pali ponse kunka nafuna chakudya; amadziwa kuti tsiku la mdima lili pafupi.
24 Distress and anguish fill him with dread; They prevail against him like a king ready for the battle.
Masautso ndi nthumanzi zimamuchititsa mantha kwambiri; zimamugonjetsa iye monga imachitira mfumu yokonzekera kukathira nkhondo,
25 Because he stretched forth his hand against God, And bade defiance to the Almighty,
chifukwa iye amatambasula dzanja lake kuyambana ndi Mulungu ndipo amadzitama yekha polimbana ndi Wamphamvuzonse.
26 And ran against him with outstretched neck, With the thick bosses of his bucklers;
Amapita mwa mwano kukalimbana naye atanyamula chishango chochindikala ndi cholimba.
27 Because he covered his face with fatness, And gathered fat upon his loins,
“Ngakhale nkhope yake ndi yonenepa ndipo mʼchiwuno mwake muli mnofu wambiri,
28 And dwelt in desolated cities, In houses which no man inhabiteth, That are ready to become heaps.
munthuyo adzakhala mʼmizinda yowonongeka ndi mʼnyumba zosayenera kukhalamo anthu, nyumba zimene zikugwa ndi kuwonongeka.
29 He shall not be rich; his substance shall not endure, And his possessions shall not be extended upon the earth.
Iye sadzalemeranso ndipo chuma chake sichidzakhalitsa, ngakhale minda yake sidzabala zipatso pa dziko lapansi.
30 He shall not escape from darkness, And the flame shall dry up his branches; Yea, by the breath of His mouth shall he be taken away.
Iyeyo sadzapulumuka mu mdimamo; lawi lamoto lidzawumitsa nthambi zake, ndipo mpweya wochokera mʼkamwa mwa Mulungu udzamusesa.
31 “Let not man trust in vanity! he will be deceived; For vanity shall be his recompense.
Asadzinyenge yekha podalira zinthu zachabechabe, pakuti pa mapeto pake sadzaphulapo kanthu.
32 He shall come to his end before his time, And his branch shall not be green.
Iye adzalandira malipiro ake nthawi yake isanakwane, ndipo nthambi zake sizidzaphukanso.
33 He shall shake off his unripe fruit like the vine, And shed his blossoms like the olive-tree.
Iye adzakhala ngati mtengo wamphesa wopululidwa zipatso zake zisanapse, adzakhala ngati mtengo wa olivi umene wayoyola maluwa ake.
34 The house of the unrighteous shall be famished, And fire shall consume the tents of bribery.
Pakuti anthu osapembedza Mulungu adzakhala osabala ndipo moto udzapsereza nyumba za onse okonda ziphuphu.
35 They conceive mischief, and bring forth misery, And their breast deviseth deceit.”
Iwo amalingalira zaupandu ndipo amachita zoyipa; mtima wawo umakonzekera zachinyengo.”

< Job 15 >