< Job 14 >

1 Man, that is born of woman, Is of few days, and full of trouble.
“Munthu wobadwa mwa amayi amakhala masiku owerengeka ndipo ndi odzaza ndi mavuto okhaokha.
2 He cometh forth as a flower, and is cut down; He fleeth also as a shadow, and continueth not.
Amaphuka ngati duwa ndipo kenaka amafota; amathawa ngati mthunzi ndipo sakhalitsa.
3 And dost thou fix thine eyes upon such a one? And dost thou bring me into judgment with thee?
Kodi munthu wotereyo nʼkumuyangʼanitsitsa? Kodi mungamubweretse pamaso panu kuti mumuzenge mlandu?
4 Who can produce a clean thing from an unclean? Not one.
Ndani angatulutse chabwino mʼchoyipa? Palibe ndi mmodzi yemwe!
5 Seeing that his days are determined, And the number of his months, with thee, And that thou hast appointed him bounds which he cannot pass,
Masiku a munthu ndi odziwikiratu; munakhazikitsa chiwerengero cha miyezi yake ndipo munamulembera malire amene sangathe kuwalumpha.
6 O turn thine eyes from him, and let him rest, That he may enjoy, as a hireling, his day!
Choncho Inu mumufulatire ndipo mumuleke apumule kufikira atakondwera nawo moyo ngati munthu waganyu.
7 For there is hope for a tree, If it be cut down, that it will sprout again, And that its tender branches will not fail;
“Mtengo uli nacho chiyembekezo: ngati wadulidwa, udzaphukiranso ndipo nthambi zake sizidzaleka kuphukira.
8 Though its root may have grown old in the earth, And though its trunk be dead upon the ground,
Mizu yake ingathe kukalamba mʼnthaka ndipo chitsa chake nʼkuwola pa dothi,
9 Through the scent of water it will bud, And put forth boughs, like a young plant.
koma pamene chinyontho chafika udzaphukira ndipo udzaphuka nthambi ngati mtengo wanthete.
10 But man dieth, and he is gone! Man expireth, and where is he?
Koma munthu amafa nayikidwa mʼmanda, amapuma mpweya wotsiriza ndipo kutha kwake nʼkomweko.
11 The waters fail from the lake; And the stream wasteth and drieth up;
Monga madzi amaphwera mʼnyanja kapena monga mtsinje umaphwera nuwuma,
12 So man lieth down, and riseth not; Till the heavens be no more, he shall not awake, Nor be roused from his sleep.
momwemonso munthu amagona ndipo sadzukanso; mpaka zamlengalenga zidzathe, anthu sadzauka kapena kudzutsidwa ku tulo tawo.
13 O that thou wouldst hide me in the under-world! That thou wouldst conceal me till thy wrath be past! That thou wouldst appoint me a time, and then remember me! (Sheol h7585)
“Aa, Inu mukanangondibisa mʼmanda ndi kundiphimba kuti ndisaoneke mpaka mkwiyo wanu utapita! Achikhala munandiyikira nthawi, kuti pambuyo pake mundikumbukirenso. (Sheol h7585)
14 If a man die, can he live again? All the days of my war-service would I wait, Till my change should come.
Munthu akafa, kodi adzakhalanso ndi moyo? Masiku anga onse a moyo wovutikawu ndidzadikira mpaka itafika nthawi yomasulidwa.
15 Thou wilt call, and I will answer thee; Thou wilt have compassion upon the work of thy hands!
Inu mudzandiyitane ndipo ndidzakuyankhani; inu mudzafunitsitsa kuona cholengedwa chimene munachipanga ndi manja anu.
16 But now thou numberest my steps; Thou watchest over my sins.
Ndithudi pamenepo mudzayangʼana mayendedwe anga koma simudzalondola tchimo langa.
17 My transgression is sealed up in a bag; Yea, thou addest unto my iniquity.
Zolakwa zanga zidzakulungidwa mʼthumba; inu mudzaphimba tchimo langa.
18 As the mountain falling cometh to nought, And the rock is removed from its place;
“Koma monga phiri limakokolokera ndi kuswekasweka ndipo monga thanthwe limasunthira kuchoka pa malo ake,
19 As the waters wear away the stones, And the floods wash away the dust of the earth, So thou destroyest the hope of man.
monganso madzi oyenda amaperesera miyala ndipo madzi othamanga amakokololera nthaka, momwemonso Inu mumawononga chiyembekezo cha munthu.
20 Thou prevailest against him continually, and he perisheth; Thou changest his countenance, and sendest him away.
Inu mumamugonjetsa kamodzinʼkamodzi ndipo munthuyo nʼkutheratu; Inu mumasintha maonekedwe a nkhope yake ndipo mumamutaya kutali.
21 His sons come to honor, but he knoweth it not; Or they are brought low, but he perceiveth it not.
Ana ake akamalemekezedwa, iyeyo sazidziwa zimenezo; akamachititsidwa manyazi iye saziona zimenezo.
22 But his flesh shall have pain for itself alone; For itself alone shall his soul mourn.
Iye amangomva zowawa za mʼthupi lake ndipo amangodzilirira yekha mwini wakeyo.”

< Job 14 >