< Job 13 >

1 Lo! all this mine eye hath seen; Mine ear hath heard and understood it.
“Ndaziona ndi maso anga zonsezi, ndazimva ndi makutu anga ndipo ndazimvetsa.
2 What ye know, I know also; I am not inferior to you.
Zimene inu mukudziwa, inenso ndimazidziwa; ineyo sindine munthu wamba kwa inu.
3 But O that I might speak with the Almighty! O that I might reason with God!
Koma ine ndikulakalaka nditayankhula ndi Wamphamvuzonse ndi kukamba mlandu wanga ndi Mulungu.
4 For ye are forgers of lies; Physicians of no value, all of you!
Koma inu mukundipaka mabodza; nonsenu ndinu asingʼanga opanda phindu!
5 O that ye would altogether hold your peace! This, truly, would be wisdom in you.
Achikhala munangokhala chete nonsenu! Apo mukanachita zanzeru.
6 Hear, I pray you, my arguments; Attend to the pleadings of my lips!
Tsopano imvani kudzikanira kwanga; imvani kudandaula kwa pakamwa panga.
7 Will ye speak falsehood for God? Will ye utter deceit for him?
Kodi inu mudzayankhula moyipa kuyankhulira Mulungu? Kodi mudzayankhulira Iyeyo mwachinyengo?
8 Will ye be partial to his person? Will ye contend earnestly for God?
Kodi mudzaonetsa kuti Iyeyo ngokondera? Kodi inu mudzamuteteza Mulungu pa mlandu wake?
9 Will it be well for you, if he search you thoroughly? Can ye deceive him, as one may deceive a man?
Mulungu atayangʼanitsitsa, inu nʼkukupezani wosalakwa? Kodi inu mungamunamize Iye monga momwe munganamizire munthu?
10 Surely he will rebuke you, If ye secretly have respect to persons.
Ndithudi, Iye angathe kukudzudzulani ngati muchita zokondera mseri.
11 Doth not his majesty make you afraid, And his dread fall upon you?
Kodi ulemerero wake sungakuopseni? Kodi kuopsa kwake sikungakuchititseni mantha?
12 Your maxims are words of dust; Your fortresses are fortresses of clay.
Mawu anu anzeru ali ngati miyambi yopanda tanthauzo; mawu anu odzitchinjirizira ali ngati mpanda wadothi.
13 Hold your peace, and let me speak: And then come upon me what will!
“Khalani chete ndipo ndilekeni ndiyankhule; tsono zimene zindichitikire zichitike.
14 Why do I take my flesh in my teeth, And put my life in my hand?
Chifukwa chiyani ndikuyika moyo wanga pa chiswe ndi kutengera mʼmanja moyo wangawu?
15 Lo! he slayeth me, and I have no hope! Yet will I justify my ways before him.
Ngakhale Iye andiphe, komabe ndidzamukhulupirira; ndithu, ndidzafotokoza mlandu wanga pamaso pake.
16 This also shall be my deliverance; For no unrighteous man will come before him.
Zoonadi, ichi ndiye chidzakhala chipulumutso changa pakuti palibe munthu wosapembedza amene angafike pamaso pake!
17 Hear attentively my words, And give ear to my declaration!
Mvetserani mosamala mawu anga; makutu anu amve zimene ndikunena.
18 Behold, I have now set in order my cause; I know that I am innocent.
Pakuti tsopano ndawukonzekera mlandu wanga, ndikudziwa ndipo adzandipeza wolungama.
19 Who is he that can contend with me? For then would I hold my peace, and die!
Kodi alipo wina amene angatsutsane nane? ngati zili choncho, ndidzakhala chete ndi kufa.
20 Only do not unto me two things, Then will I not hide myself from thy presence;
“Inu Mulungu, ndipatseni zinthu ziwiri izi, ndipo pamenepo ine sindidzakubisalirani:
21 Let not thy hand be heavy upon me, And let not thy terrors make me afraid:
Muchotse dzanja lanu pa ine, ndipo muleke kundichititsa mantha ndi kuopsa kwanuko.
22 Then call upon me, and I will answer; Or I will speak, and answer thou me.
Tsono muyitane ndipo ndidzayankha, kapena mulole kuti ine ndiyankhule ndipo Inu muyankhe.
23 How many are my iniquities and sins? Make me to know my faults and transgressions.
Kodi zolakwa zanga ndi zingati ndipo machimo anga ndi angati? Wonetseni kulakwa kwanga ndi machimo anga.
24 Wherefore dost thou hide thy face, And account me as thine enemy?
Chifukwa chiyani mukundifulatira ndi kundiyesa ine mdani wanu?
25 Wilt thou put in fear the driven leaf? Wilt thou pursue the dry stubble?
Kodi mudzazunza tsamba lowuluka ndi mphepo? Kodi mudzathamangitsa mungu wowuma?
26 For thou writest bitter things against me, And makest me inherit the sins of my youth.
Pakuti Inu mwalemba zinthu zowawa zonditsutsa nazo ndipo mukundipaka machimo a pa ubwana wanga.
27 Yea, thou puttest my feet in the stocks, And waterest all my paths; Thou hemmest in the soles of my feet.
Inu mwamanga miyendo yanga ndi maunyolo. Mumayangʼanitsitsa mayendedwe anga onse poyika zizindikiro pamene mapazi anga apondapo.
28 And I, like an abandoned thing, shall waste away; Like a garment which is moth-eaten.
“Motero munthu amatha ngati chinthu chofumbwa, ngati chovala chodyedwa ndi njenjete.

< Job 13 >