< Jeremiah 44 >
1 The word which came to Jeremiah concerning all the Jews that dwelt in the land of Egypt, that dwelt at Migdol, and at Tahpanhes, and at Noph, and in the land of Pathros, saying:
Uthenga umene Yeremiya analandira wonena za Ayuda onse amene ankakhala ku Igupto, ku mizinda ya Migidoli, Tapanesi ndi Mefisi, ndiponso ku Patirosi ndi uwu:
2 Thus saith Jehovah of hosts, the God of Israel: Ye have seen all the evil which I have brought upon Jerusalem, and upon all the cities of Judah; and behold, this day they are a desolation, and no man dwelleth therein;
“Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israeli akuti: Inu mwaona mavuto aakulu amene ndinawabweretsa pa Yerusalemu ndi mizinda yonse ya Yuda. Lero mizinda yonseyo yasanduka mabwinja, yopanda munthu wokhalamo.
3 because of their wickedness, which they have committed, to provoke me to anger, in that they went to burn incense and to serve strange gods, whom they knew not, neither they, ye, nor your fathers;
Zimenezi zinachitika chifukwa cha zoyipa zomwe anachita. Iwo anaputa mkwiyo wanga pofukiza lubani ndi potumikira milungu ina imene iwo kapena inu ngakhalenso makolo anu sanayidziwe.
4 and I sent to you all my servants, the prophets, rising early and sending them, saying: O do not this abominable thing, which I hate!
Kawirikawiri Ine ndakhala ndikutuma atumiki anga, aneneri, amene anati, ‘Musachite chinthu chonyansachi chimene Ine ndimadana nacho!’
5 But they hearkened not, nor inclined their ear to turn from their wickedness, to burn no incense to strange gods.
Koma iwo sanamvere kapena kulabadira; sanatembenuke kusiya zoyipa zawo kapena kuleka kufukiza lubani kwa milungu ina.
6 Therefore hath my fury been poured forth, and mine anger, and hath burned in the cities of Judah, and in the streets of Jerusalem; and they are become a desolation and a waste at this day.
Nʼchifukwa chake mkwiyo wanga unayaka ngati moto kutentha mizinda ya ku Yuda ndi misewu ya mu Yerusalemu ndi kuyisandutsa bwinja mpaka lero.
7 And now thus saith Jehovah, the God of hosts, the God of Israel: Wherefore do ye commit this great evil against your own souls, that ye may cut off from you man and woman, child and suckling, out of Judah, so as to leave yourselves no remnant?
“Ndiye tsopano Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israeli, akunena kuti, ‘Chifukwa chiyani mukufuna kudziwononga chotere? Kodi mukufuna kuti amuna, akazi, ana ndi makanda onse aphedwe ndi kuti mu Yuda musatsale ndi munthu mmodzi yemwe?
8 Why do ye provoke me to wrath with the works of your hands, burning incense to strange gods in the land of Egypt, whither ye are gone to dwell, so that ye may cut yourselves off, and that ye may be a curse and a reproach among all the nations of the earth?
Chifukwa chiyani mukuputa mkwiyo wanga popembedza mafano pofukiza lubani kwa milungu ina mʼdziko lino la Igupto mʼmene mukukhalamo. Kodi mukuchita zimenezi kuti mudziwononge nokha ndi kuti mudzisandutse chinthu choseketsa ndi chonyozeka pakati pa mitundu yonse ya dziko lapansi?
9 Have ye forgotten the wickedness of your fathers, and the wickedness of the kings of Judah, and the wickedness of their wives, and your own wickedness, and the wickedness of your wives, which they have committed in the land of Judah, and in the streets of Jerusalem?
Kodi mwayiwala zoyipa zimene anachita makolo anu, mafumu a ku Yuda ndi akazi awo, ndiponso zoyipa zimene munachita inuyo ndi akazi anu mʼdziko la Yuda ndi mʼmisewu ya mu Yerusalemu?
10 They have not been humbled even to this day, neither have they feared, nor walked in my law, nor in my statutes, which I set before you, and before your fathers.
Koma mpaka lero simunalape. Simunandilemekeze kapena kumvera malamulo anga amene ndinayikira inuyo ndi makolo anu.
11 Therefore thus saith Jehovah of hosts, the God of Israel: Behold, I set my face against you for evil, even to cut off all Judah.
“Nʼchifukwa chake Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israeli akunena kuti, ‘Ine ndatsimikiza zobweretsa mavuto pa inu ndi kuwatheratu anthu a ku Yuda.
12 And I will take the remnant of Judah, that have set their faces to go into the land of Egypt to sojourn there, and they shall all be consumed; in the land of Egypt shall they fall; by the sword and by famine shall they be consumed, from the least to the greatest; by the sword and by famine shall they die; and they shall become an execration, and an astonishment, and a curse, and a reproach.
Ndidzatenga anthu otsala a ku Yuda amene atsimikiza zopita ku Igupto ndi kukakhala kumeneko. Onse adzathera ku Igupto. Adzaphedwa ndi lupanga kapena kufa ndi njala. Kuyambira wamngʼono mpaka wamkulu, adzaphedwa ndi lupanga kapena kufa ndi njala. Adzasanduka chinthu chotembereredwa ndi chochititsa mantha, chinthu choseketsa ndi chonyozeka.
13 For I will punish them that dwell in the land of Egypt, as I have punished Jerusalem, by the sword, by famine, and by pestilence.
Ndidzalanga Ayuda okhala ku Igupto ndi lupanga, njala ndi mliri, ngati mmene ndinalangira anthu a ku Yerusalemu.
14 And none shall escape or remain of the remnant of Judah which are gone into the land of Egypt, to sojourn there, and to return into the land of Judah, to which they have a desire to return, to dwell there; for none shall return but a few fugitives that escape.
Motero mwa anthu amene anapita ku Igupto palibe ndi mmodzi yemwe adzapulumuke, kapena kukhala ndi moyo, kapena kubwerera ku Yuda. Palibe amene adzabwerere kupatula othawa nkhondo.’”
15 Then all the men who knew that their wives had burned incense to strange gods, and all the women that stood by, a great multitude, even all the people that dwelt in the land of Egypt, and in Pathros, answered Jeremiah, saying:
Tsono amuna onse amene anadziwa kuti akazi awo ankafukiza lubani kwa milungu ina, ndiponso akazi onse amene anali pamenepo, gulu lalikulu la anthu, pamodzi ndi anthu onse amene amakhala ku Patirosi mʼdziko la Igupto, anati kwa Yeremiya,
16 “As for the word which thou hast spoken to us in the name of Jehovah, we will not hearken to thee,
“Ife sitimvera uthenga umene watiwuza mʼdzina la Yehova!
17 But whatever hath gone forth from our mouth, that will we do, to burn incense to the queen of heaven, and to pour out drink-offerings to her, as we have done, we and our fathers, our kings and our princes, in the cities of Judah, and in the streets of Jerusalem; for then we had plenty of bread, and were prosperous, and saw no calamity.
Koma tidzachitadi chilichonse chimene tinanena kuti tidzachita: Tidzafukiza lubani kwa mfumukazi yakumwamba ndipo tidzayipatsa nsembe yachakumwa ngati mmene tinkachitira ifeyo ndi makolo athu, mafumu athu ndi akuluakulu mʼmizinda ya ku Yuda ndi mʼmisewu ya mu Yerusalemu. Nthawi imeneyo ife tinali ndi chakudya chochuluka ndipo tinali pabwino, sitimapeza mavuto.
18 But from the time we left off to burn incense to the queen of heaven, and to pour out drink-offerings to her, we have been in want of all things, and have been consumed by the sword and by famine.
Koma kuchokera nthawi imene tinasiya kufukiza lubani ndi kupereka chopereka cha chakumwa kwa mfumukazi yakumwamba, ifeyo takhala tikusowa zinthu ndipo takhala tikuphedwa ndi lupanga ndi kufa ndi njala.”
19 And when we [[said the women]] burned incense to the queen of heaven, and poured out drink-offerings to her, did we without the knowledge of our men make cakes to worship her, and pour out drink-offerings to her?”
Akazi anawonjezera kunena kuti, “Pamene tinkafukiza lubani kwa mfumukazi yakumwamba ndi kuyipatsa chopereka cha chakumwa, kodi suja amuna athu ankavomereza mmene timayipangira mfumukazi yakumwambayo makeke abwino olembapo chinthunzi chake ndi kuyipatsa chopereka cha chakumwa?”
20 Then spake Jeremiah to all the people, to the men, and to the women, and to all the people who had given him that answer, saying:
Yeremiya atamva kuyankha kumeneku anawawuza kuti,
21 “The incense which ye burned in the cities of Judah, and in the streets of Jerusalem, ye and your fathers, your kings and your princes, and the people of the land, did not Jehovah remember it, and came it not into his mind?
“Kodi mukuganiza kuti Yehova nʼkuyiwala kuti inuyo ndi makolo anu, mafumu anu ndi akuluakulu anu, ndiponso anthu onse, munkafukiza lubani kwa mafano a mʼmizinda ya ku Yuda ndi mʼmisewu ya mu Yerusalemu?
22 And Jehovah could no longer bear the evil of your doings, and the abominations which ye committed; therefore is your land a desolation, and an astonishment, and a curse, without an inhabitant at this day.
Ndiye Yehova sakanathanso kupirira ndi machitidwe anu ndi zonyansa zimene munkachita. Nʼchifukwa chake dziko lanu linasanduka chipululu, chinthu choopsa ndi chotembereredwa. Dziko lopandamo anthu monga zilili lero lino.
23 Because ye have burned incense, and because ye have sinned against Jehovah, and have not obeyed the voice of Jehovah, nor walked in his law, nor in his statutes, nor in his ordinances, therefore is this evil come upon you, at this day.”
Mavuto awa akugwerani chifukwa munkafukiza lubani ndipo munkachimwira Yehova pokana kumvera mawu ake ndi kutsatira malamulo ndi malangizo ake.”
24 And Jeremiah said to all the people and to all the women, Hear the word of Jehovah, all Judah, that are in the land of Egypt!
Kenaka Yeremiya anawuza anthu onse, makamaka akazi kuti, “Imvani mawu a Yehova, anthu onse a ku Yuda amene muli mu Igupto.
25 Thus saith Jehovah of hosts, the God of Israel: Ye and your wives speak with your mouths, and fulfill with your hands; ye say, “We will keep our vows, which we have vowed, to burn incense to the queen of heaven, and to pour out drink-offerings to her”; ye will surely accomplish your vows; ye will surely perform your vows.
Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israeli akuti: Inu ndi akazi anu munalonjeza ndi pakamwa panu, ndipo malonjezowo mwakwaniritsa. Inu munanena kuti, ‘Tidzachita zimene tinalonjeza, kufukizira lubani mfumukazi yakumwamba ndi kuyipatsa chopereka cha zakumwa.’ Tsopano chitanitu zimene munalonjezazo! Kwaniritsani malumbiro anu. “Yambani, chitani zimene munalonjeza! Kwaniritsani malumbiro anu!
26 Therefore hear ye the word of Jehovah, all ye of Judah, that dwell in the land of Egypt! Behold, I swear by my great name, saith Jehovah, that my name shall no more be named in the mouth of any man of Judah in all the land of Egypt, saying, “As the Lord Jehovah liveth!”
Koma imvani mawu a Yehova, inu Ayuda nonse amene mukukhala mu Igupto: Yehova akuti, ‘Ine ndikulumbira mʼdzina langa lopambana kuti palibe wochokera ku Yuda amene akukhala mu Igupto amene adzatchule dzina langa polumbira kuti, ‘Pali Ambuye Yehova wamoyo.’
27 Behold, I will watch over them for evil, and not for good; and all the men of Judah who are in the land of Egypt shall be consumed by the sword and by famine, until there be an end of them.
Pakuti ndionetsetsa kuti ndiwachitire choyipa, osati chabwino. Anthu a ku Yuda amene akukhala ku Igupto adzaphedwa pa nkhondo. Ena adzafa ndi njala mpaka onse atatheratu.
28 And they that escape the sword shall return out of the land of Egypt into the land of Judah, few in number; and all the remnant of Judah, that are gone into the land of Egypt to sojourn there, shall know whose words shall stand, mine or theirs.
Amene adzapulumuke ku lupanga ndi kubwerera ku dziko la Yuda kuchokera ku Igupto adzakhala ochepa kwambiri. Choncho otsala onse a ku Yuda amene anapita kukakhala ku Igupto adzadziwa kuti mawu woona ndi ati, anga kapena awo.
29 And this shall be a sign to you, saith Jehovah, that I will punish you in this place, that ye may know that my words shall surely stand against you for evil.
“Ine Yehova ndikukupatsani chizindikiro chakuti ndidzakulangani ku malo ano. Motero mudzadziwa kuti mawu anga akuti ndidzakulangani ndi woona.
30 Thus saith Jehovah: Behold, I will give Pharaoh Hophra, the king of Egypt, into the hand of his enemies, and into the hand of them that seek his life, as I gave Zedekiah, the king of Judah, into the hand of Nebuchadnezzar, the king of Babylon, his enemy, that sought his life.”
Yehova akuti, ‘Ine ndidzamupereka Farao Hofira mfumu ya Igupto kwa adani ake amene akufuna kumupha, monga momwe ndinaperekera Zedekiya mfumu ya Yuda kwa Nebukadinezara mfumu ya ku Babuloni, mdani wake amene ankafuna kumupha.’”