< Jeremiah 42 >

1 And all the captains of the forces, and Johanan, the son of Kareah, and Jezaniah, the son of Hoshaiah, and all the people, from the least even to the greatest, came near,
Atsogoleri onse a ankhondo pamodzi ndi Yohanani mwana wa Kareya ndi Azariya mwana wa Hosayia, ndiponso anthu onse, ana ndi akuluakulu omwe, anapita
2 and said to Jeremiah the prophet: “Let, we beseech thee, our supplication be accepted before thee, and pray for us to Jehovah, thy God, for all this remnant; (for we are left a few out of many, as thine eyes do behold us; )
kwa mneneri Yeremiya ndipo anamuwuza kuti, “Chonde imvani dandawulo lathu ndipo mutipempherere anthu otsalafe kwa Yehova Mulungu wanu. Pakuti monga tsopano mukuona, ngakhale kuti kale tinalipo ambiri, koma tsopano ochepa okha ndiye amene atsala.
3 that Jehovah, thy God, may show us the way wherein we shall walk, and the thing which we shall do.”
Mupemphere kuti Yehova Mulungu wanu atiwuze kumene tiyenera kupita ndi chimene tiyenera kuchita.”
4 And Jeremiah the prophet said to them: “I have heard; behold, I will pray to Jehovah your God, according to your words, and all which Jehovah shall answer you I will declare to you; I will keep back nothing from you.”
Mneneri Yeremiya anawayankha kuti, “Ndamva zimene mwanenazi. Ndithu ndidzapemphera kwa Yehova Mulungu wanu monga momwe mwandipemphera. Ndidzakuwuzani chilichonse chimene Yehova anene ndipo sindidzakubisirani kanthu kalikonse.”
5 Then they said to Jeremiah: “May Jehovah be our witness, a faithful and true witness! According to all for which Jehovah our God shall send thee to us, so will we do.
Ndipo iwo anawuza Yeremiya kuti, “Yehova akhale mboni yoona ndi yokhulupirika yodzatitsutsa ife ngati sitichita mogwirizana ndi chilichonse chimene Yehova Mulungu adzakutumani kuti mutiwuze.
6 Whether it be good, or whether it be evil, we will obey the voice of Jehovah our God, to whom we send thee, that it may be well with us when we shall have obeyed the voice of Jehovah our God.”
Kaya ndi zotikomera kapena zosatikomera, ife tidzamvera Yehova Mulungu wathu, amene takutumaniko. Tidzamvera Yehova Mulungu wathu kuti zinthu zidzatiyendere bwino.”
7 And it came to pass after ten days, that the word of Jehovah came to Jeremiah.
Patapita masiku khumi, Yehova anayankhula ndi Yeremiya.
8 And he called Johanan, the son of Kareah, and all the captains of the forces which were with him, and all the people, from the least even to the greatest,
Choncho Yeremiya anayitana Yohanani mwana wa Kareya pamodzi ndi atsogoleri onse a ankhondo amene anali naye ndiponso anthu onse, ana ndi akulu omwe.
9 and said to them: “Thus saith Jehovah, the God of Israel, to whom ye sent me to present your supplication before him:
Yehova, Mulungu wa Israeli amene munanditumako kuti ndikapereke madandawulo mʼdzina lanu akuti,
10 If ye will still abide in this land, then will I build you, and not pull you down, and I will plant you, and not pluck you up; for I repent me of the evil which I have done to you.
“Ngati mukhala mʼdziko muno, ndiye kuti ndidzakukhazikitsani, osakuchotsani. Inde ndidzakudzalani osakuchotsani pakuti ndi kumva chisoni kwambiri chifukwa cha mavuto amene ndabweretsa pa inu.
11 Be not afraid of the king of Babylon, of whom ye are afraid; be not afraid of him, saith Jehovah; for I will be with you to save you, and to deliver you from his hand.
Musayiope mfumu ya ku Babuloni, imene mukuyiopa tsopano. Musachite nayo mantha, akutero Yehova, pakuti Ine ndili nanu ndipo ndidzakupulumutsani ndi kukulanditsani mʼmanja mwake.
12 And I will show mercies to you, that he may have compassion upon you, and cause you to return to your own land.
Ndidzakuchitirani chifundo, ndipo mfumuyonso idzakuchitirani chifundo ndi kukulolani kuti mukhale mʼdziko mwanumwanu.
13 But if ye say, 'We will not dwell in this land,' so as not to hearken to the voice of Jehovah your God,
“Koma mwina simudzamvera Yehova Mulungu wanu nʼkumanena kuti, ‘Ayi ife sitidzakhala mʼdziko muno,
14 saying, 'No! but we will go into the land of Egypt, where we shall see no war, nor hear the sound of the trumpet, nor be hungry for bread, and there will we dwell, —
ndipo ngati mukunena kuti, ‘Ayi, koma tidzapita ku Igupto kumene sitidzaonako nkhondo kapena kumva kulira kwa lipenga kapenanso kusowa chakudya.’
15 now, therefore, hear the word of Jehovah, ye remnant of Judah! Thus saith Jehovah of hosts, the God of Israel: If ye set your faces to enter into Egypt, and go to sojourn there,
Tsono, inu otsala a ku Yuda, imvani mawu a Yehova. Iye akuti, ngati mutsimikiza zopita ku Igupto, nʼkupitadi kukakhala kumeneko,
16 then it shall come to pass that the sword, which ye feared, shall overtake you there in the land of Egypt, and the famine, of which ye were afraid, shall follow close after you into Egypt, and there shall ye die.
ndiye nkhondo imene mukuyiopayo idzakugonjetsani ku Igupto komweko. Njala imene mukuyiopayo idzakupezani ku Igupto komweko ndipo mudzafera kumeneko.
17 So shall it be with all the men that set their faces to go into Egypt to sojourn there. They shall die by the sword, and by famine, and by pestilence, and not one of them shall remain, or escape from the evil which I bring upon them.
Kunena zoona, onse amene atsimikiza zopita ku Igupto kuti akakhale kumeneko adzafa ndi nkhondo njala ndi mliri. Palibe ndi mmodzi yemwe amene adzapulumuke kapena kuthawa mavuto amene ndidzawagwetsera.’
18 For thus saith Jehovah of hosts, the God of Israel: As my anger and my wrath have been poured forth upon the inhabitants of Jerusalem, so shall my wrath be poured forth upon you, when ye shall enter into Egypt; and ye shall be an execration, and an astonishment, and a curse, and a reproach; and ye shall see this place no more.
Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israeli akuti, ‘Momwe ndinawakwiyira mwaukali anthu okhala mu Yerusalemu, koteronso ndidzakukwiyirani mukapita ku Igupto. Mudzasanduka chinthu chotembereredwa ndi chochititsa mantha, choseketsa ndi chonyozeka. Malo ano simudzawaonanso.’
19 This is the word of Jehovah to you, ye remnant of Judah! Go ye not into Egypt; ye shall surely know that I have warned you this day.
“Inu otsala a ku Yuda, Yehova wakuwuzani kuti, ‘Musapite ku Igupto.’ Dziwani chinthu ichi: Ine lero ndikukuchenjezani
20 Ye err to your own ruin; for ye sent me to Jehovah your God, saying, 'Pray for us to Jehovah our God, and according to all that Jehovah our God shall say, so declare to us, and we will do it';
kuti munalakwitsa kwambiri. Inu munandituma kwa Yehova Mulungu wanu nʼkumati ‘Mukatipempherere kwa Yehova Mulungu wathu, nʼkudzatiwuza chimene afuna kuti tichite, ndipo ife tidzachita.’
21 and now I have this day declared it to you, but ye have not hearkened to the voice of Jehovah your God, nor to anything for which he sent me to you.
Ine lero ndakuwuzani, koma inu simukumverabe zonse zimene Yehova Mulungu anandituma kuti ndikuwuzeni.
22 Now, therefore, ye shall know assuredly, that by the sword, by famine, and by pestilence ye shall die, in the place whither ye have chosen to go and to sojourn.”
Tsono dziwani ichi: mudzafadi ndi nkhondo, njala ndi mliri kumalo kumene mukufuna mukakhaleko.”

< Jeremiah 42 >