< Jeremiah 38 >

1 And Shephatiah, the son of Mattan, and Gedaliah, the son of Pashur, and Jucal, the son of Shelemiah, and Pashur, the son of Malchiah, heard the words which Jeremiah spoke to all the people, saying,
Sefatiya mwana wa Matani, Gedaliya mwana wa Pasi-Huri, Yukali mwana wa Selemiya, ndi Pasi-Huri mwana wa Malikiya anamva zimene Yeremiya ankawuza anthu onse kuti,
2 “Thus saith Jehovah: He that remaineth in this city shall die by the sword, by famine, and by pestilence; but he that goeth forth to the Chaldaeans shall live, and he shall retain his life as a prey, and shall live.
“Yehova akuti, ‘Aliyense amene akhale mu mzinda muno adzafa ndi nkhondo njala kapena mliri. Koma aliyense amene atatuluke kukadzipereka kwa Ababuloni adzapulumutsa moyo wake; iyeyo adzakhala ndi moyo.
3 Thus saith Jehovah: This city shall surely be given into the hand of the army of the king of Babylon, and he shall take it.”
Mzinda uno udzaperekedwa ndithu kwa gulu lankhondo la mfumu ya ku Babuloni, amene adzawulande.’”
4 Then said the princes to the king, “We beseech thee, let this man be put to death! for thus he weakeneth the hands of the men of war that remain in this city, and the hands of all the people, in speaking such words to them; for this man seeketh not the welfare of this people, but their hurt.”
Tsono akuluakuluwo anawuza mfumu kuti, “Munthu uyu ayenera kuphedwa. Iye akutayitsa mtima asilikali pamodzi ndi anthu onse amene atsala mu mzinda muno, chifukwa cha zimene akuwawuza. Munthu ameneyu sakufunira zabwino anthuwa koma chiwonongeko chawo.”
5 Then Zedekiah the king said, “Behold, he is in your hand; for the king is not one that can do anything in opposition to you.”
Mfumu Zedekiya anayankha kuti, “Munthuyu ali mʼmanja mwanu. Ine sindingakuletseni chimene mukufuna kumuchitira.”
6 Then took they Jeremiah, and cast him into the dungeon of Malchiah, the son of Hammelech, which was in the court of the prison; and they let down Jeremiah with cords. And in the dungeon there was no water, but only mire; and Jeremiah sunk in the mire.
Choncho iwo anatenga Yeremiya nakamuponya mʼchitsime cha Malikiya, mwana wa mfumu, chimene chinali mʼbwalo la alonda. Iwo anamutsitsira mʼdzenjemo ndi chingwe. Munalibe madzi koma matope okhaokha, ndipo Yeremiya anamira mʼmatopewo.
7 And Ebedmelech, the Ethiopian, a eunuch, who was then in the king's house, heard that they had put Jeremiah into the dungeon; and the king was sitting in the gate of Benjamin.
Koma Ebedi-Meleki, Mkusi, mmodzi mwa anthu ofulidwa ogwira ntchito mʼnyumba ya mfumu, anamva kuti Yeremiya anamuponya mʼchitsime. Nthawi imeneyo nʼkuti mfumu ili ku chipata cha Benjamini.
8 Then Ebedmelech went forth out of the king's house, and spake to the king, saying,
Ebedi-Meleki anatuluka ku nyumba ya mfumu kukayiwuza kuti,
9 “My lord the king! these men have done evil in all that they have done to Jeremiah the prophet whom they have cast into the dungeon; for he was already almost dead in his place for hunger; for there is no more bread in the city.”
“Mbuye wanga mfumu, zimene anthu awa amuchitira mneneri Yeremiya ndi zoyipa kwambiri. Iwo amuponya mʼchitsime, ndipo adzafa ndi njala chifukwa buledi watha mu mzinda muno.”
10 Then the king commanded Ebedmelech, the Ethiopian, saying, “Take along with thee thirty men from hence, and take up Jeremiah the prophet out of the dungeon, before he die.”
Tsono mfumu inalamula Ebedi-Meleki, Mkusi, kuti, “Tenga anthu makumi atatu, ndipo mukamutulutse mʼchitsimemo mneneri Yeremiya asanafe.”
11 And Ebedmelech took the men with him, and went into the king's house under the store-room, and took from thence torn rags and worn-out rags, and let them down by cords into the dungeon to Jeremiah.
Pamenepo Ebedi-Meleki anatenga anthuwo, napita nawo ku nyumba ya mfumu ya pansi pa chipinda chosungiramo chuma. Kumeneko anakatengako sanza ndipo anatsitsira sanzazo ndi chingwe mʼchitsime mʼmene munali Yeremiya.
12 And Ebedmelech, the Ethiopian, said to Jeremiah, put now these torn and worn-out rags under thy knuckles under the cords. And Jeremiah did so.
Ebedi-Meleki, Mkusi, anawuza Yeremiya kuti, “Ika sanzazo mkwapa mwako kuti zingwe zingakupweteke.” Yeremiya anachitadi zimenezi,
13 And they drew up Jeremiah with cords, and took him up out of the dungeon; and Jeremiah remained in the court of the prison.
ndipo anamukoka ndi zingwe ndi kumutulutsa mʼchitsimecho. Ndipo Yeremiya anakhalabe ku bwalo la alonda.
14 And King Zedekiah sent, and took Jeremiah the prophet to him into the third entrance, which is in the house of Jehovah; and the king said to Jeremiah, “I will ask thee a question; hide nothing from me!”
Tsiku lina Mfumu Zedekiya anayitana mneneri Yeremiya ndipo anabwera naye ku chipata chachitatu cha Nyumba ya Yehova. Mfumu inawuza Yeremiya kuti, “Ndikufuna kukufunsa kanthu kena, ndipo usandibisire chilichonse.”
15 And Jeremiah said to Zedekiah, “When I have told thee, wilt thou not surely put me to death? and if I give thee counsel, thou wilt not hearken to me.”
Yeremiya anati kwa Zedekiya, “Ndikakuyankhani, kodi simundipha? Ngakhaletu ine nditakulangizani, inu simudzandimvera.”
16 Then King Zedekiah swore to Jeremiah in secret, saying, “As Jehovah liveth, who made for us this soul, I will not put thee to death, neither will I give thee into the hand of these men that seek thy life.”
Koma Mfumu Zedekiya mwachinsinsi inalumbira kwa Yeremiya kuti, “Pali Yehova wamoyo, amene amatipatsa moyo, sindidzakupha ngakhalenso kukupereka kwa amene akufuna kukuphawa.”
17 Then said Jeremiah to Zedekiah, “Thus saith Jehovah of hosts, the God of Israel: If thou wilt go forth to the chieftains of the king of Babylon, then shalt thou live; and this city shall not be burned with fire; and thou shalt live, thou and thine house.
Pamenepo Yeremiya anati kwa Zedekiya, “Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israeli akuti, ‘Ngati mutuluka kukadzipereka kwa ankhondo a mfumu ya ku Babuloni, mudzakhala ndi moyo ndipo mzinda uno sadzawutentha, inu pamodzi ndi banja lanu mudzakhala ndi moyo.
18 But if thou wilt not go forth to the chieftains of the king of Babylon, then shall this city be given into the hand of the Chaldaeans, and they shall burn it with fire, and thou shalt not escape out of their hand.”
Koma ngati simutuluka kukadzipereka kwa ankhondo a mfumu ya ku Babuloni, mzinda uno udzaperekedwa kwa Ababuloni ndipo adzawutentha; inuyo simudzapulumuka mʼdzanja mwawo.’”
19 And Zedekiah the king said to Jeremiah, “I am afraid of the Jews who have gone over to the Chaldaeans, lest I should be delivered into their hand, and they should mock me.”
Mfumu Zedekiya inati kwa Yeremiya, “Ine ndikuopa Ayuda amene anathawira kale kwa Ababuloni, pakuti mwina Ababuloniwo adzandipereka kwa Ayudawo ndipo iwowo adzandizunza.”
20 And Jeremiah said, “Thou shalt not be delivered up to them. Obey, I beseech thee, the voice of Jehovah in what I speak to thee; so shall it be well with thee, and thou shalt live.
Yeremiya anayankha kuti, “Ngati mumvera Yehova ndi kuchita zimene ndakuwuzani, ndiye kuti zinthu zidzakuyenderani bwino. Inu simudzaphedwa.
21 But if thou refuse to go forth, this is what Jehovah hath revealed to me.
Koma mukakana kudzipereka, chimene Yehova wandiwululira ndi ichi:
22 Behold, all the women that are left in the house of the king of Judah shall be brought forth to the chieftains of the king of Babylon, and shall say, 'Thy friends have set thee on, and have prevailed against thee; thy feet are sunk in the mire; they go backward.'
Akazi onse amene atsala mʼnyumba ya mfumu ya Yuda adzaperekedwa kwa akuluakulu a mfumu ya ku Babuloni. Akazi amenewo adzakuwuzani kuti, “‘Abwenzi ako okhulupirika aja anakusokeretsa, ndipo anakugonjetsa. Poti tsopano miyendo yako yazama mʼmatope; abwenzi ako aja akusiya.’
23 And all thy wives and thy children shall they bring out to the Chaldaeans, and thou shalt not escape out of their hand, but by the hand of the king of Babylon shalt thou be taken; and thou shalt cause this city to be burned with fire.”
“Akazi pamodzi ndi ana anu adzaperekedwa kwa Ababuloni. Inuyo simudzapulumuka mʼmanja mwawo koma mfumu ya ku Babuloni idzakugwirani; mzinda uno adzawutentha.”
24 Then said Zedekiah to Jeremiah, “Let no man know of these words, and thou shalt not die.
Pamenepo Zedekiya anati kwa Yeremiya, “Usawuze munthu wina aliyense zimene takambiranazi, ukatero udzaphedwa.
25 But if the princes shall hear that I have talked with thee, and shall come to thee, and say to thee, 'Tell us, we pray thee, what thou hast said to the king; hide it not from us, and we will not put thee to death; and what the king hath said to thee';
Akuluakulu akamva kuti ndinayankhula nawe ndipo akabwera kwa iwe nʼkudzakufunsa kuti, ‘Tiwuze zimene unanena kwa mfumu ndi zimene mfumu inanena kwa iwe; usatibisire, ukatero tidzakupha,’
26 then shalt thou say to them, 'I presented my supplication before the king, that he would not cause me to return to the house of Jonathan to die there.'”
udzawawuze kuti, ‘Ine ndimapempha mfumu kuti isandibwezerenso ku nyumba ya Yonatani kuti ndikafere kumeneko.’”
27 Then came all the princes to Jeremiah, and asked him; and he told them according to all those words which the king had commanded. And they said no more to him, for the matter was not known.
Akuluakulu onse anabweradi kwa Yeremiya kudzamufunsa. Iye anawayankha monga momwe mfumu inamulamula. Choncho palibe amene ananenanso kanthu, pakuti palibe amene anamva zomwe anakambirana ndi mfumu.
28 And Jeremiah remained in the court of the prison to the day when Jerusalem was taken.
Ndipo Yeremiya anakhalabe mʼbwalo la alonda mpaka tsiku limene mzinda wa Yerusalemu unalandidwa.

< Jeremiah 38 >