< Jeremiah 13 >

1 Thus saith Jehovah to me: Go and get thee a linen girdle, and put it on thy loins, and put it not into water!
Yehova anandiwuza kuti, “Pita kagule lamba wansalu yosalala ndipo ukavale mʼchiwuno mwako, koma usakamuviyike mʼmadzi.”
2 So I got a girdle according to the word of Jehovah, and put it on my loins.
Choncho ndinakagula lambayo, monga momwe anandiwuzira Yehova, ndipo ndinamanga mʼchiwuno mwanga.
3 Then the word of Jehovah came to me the second time, saying,
Kenaka Yehova anandiyankhulanso kachiwiri kuti,
4 Take the girdle which thou hast gotten, which is upon thy loins, and arise, go to the Euphrates, and hide it there in a hole of the rock.
“Tenga lamba amene unagula ndi kuvala mʼchiwuno mwako uja. Tsono pita ku mtsinje wa Yufurate ndipo ukamubise lambayo mʼmingʼalu ya mʼmatanthwe.”
5 So I went and hid it near the Euphrates, as Jehovah commanded me.
Ndipo ndinapitadi ndi kukabisa lambayo ku Yufurate, monga anenera Yehova.
6 And after many days Jehovah said to me. Arise, go to the Euphrates, and take thence the girdle which I commanded thee to hide there.
Patapita masiku ambiri Yehova anandiwuzanso kuti, “Pitanso ku Yufurate ndipo ukatenge lamba amene ndinakuwuza kuti ukamubise kumeneko.”
7 Then I went to the Euphrates, and digged, and took the girdle from the place where I had hidden it; and, behold, the girdle was marred, so that it was good for nothing.
Choncho ndinapita ku Yufurate kukafukula lambayo ndi kumuchotsa pamalo pamene ndinamubisa, koma nthawi imeneyi nʼkuti lambayo atawonongeka kotheratu ndipo analibenso ntchito.
8 Then the word of Jehovah came to me, saying: —
Pamenepo Yehova anandiwuza kuti,
9 Thus saith Jehovah: After this manner will I mar the pride of Judah, And the great pride of Jerusalem.
“Izi ndi zimene ine ndikunena: ‘Umu ndi mmene ndidzawonongere zimene akunyadira kwambiri a ku Yuda ndi a ku Yerusalemu.
10 This evil people, Who refuse to hearken to my words, Who walk after the obstinacy of their heart, And walk after strange gods, To serve them and to worship them, Shall be like this girdle, Which is good for nothing.
Anthuwa ndi oyipa. Iwo akana kumvera mawu anga. Mʼmalo mwake amawumirira kutsata milungu ina, kuyitumikira ndi kuyipembedza. Anthu amenewa adzakhala ngati lamba wopanda ntchitoyu.
11 For as a girdle cleaveth to the loins of a man, So have I caused to cleave to me the whole house of Israel, And the whole house of Judah, saith Jehovah, That they might be to me a people, And a name, and a praise, and a glory; But they hearkened not to me.
Monga momwe lamba amakanirira mʼchiwuno cha munthu, momwemonso ndinakonza kuti nyumba yonse ya Israeli ndi nyumba yonse ya Yuda indikangamire Ine kuti akhale anthu anga, kuti azitamanda dzina langa ndi kulemekeza Ine. Koma iwo sanamvere,’ akutero Yehova.
12 Then shalt thou speak to them in this manner. Thus saith Jehovah, the God of Israel: Every flagon shall be filled with wine. And they will say to thee, “Do we not know that every flagon shall be filled with wine?”
“Awuze anthuwo kuti, ‘Yehova Mulungu wa Israeli akuti: Mtsuko uliwonse adzawudzaza ndi vinyo.’ Ndipo ngati iwo anena kwa iwe kuti, ‘Kodi ngati ife sitikudziwa kuti mtsuko uliwonse udzadzazidwa ndi vinyo?’
13 Then shalt thou say to them, Thus saith Jehovah: Behold, I will fill all the inhabitants of this land, And the kings that sit upon David's throne, And the priests, and the prophets, And all the inhabitants of Jerusalem, with drunkenness.
Tsono iwe uwawuze kuti, Yehova akuti ‘Ine ndidzaledzeretsa anthu onse okhala mʼdziko muno, kuyambira mafumu amene amakhala pa mpando waufumu wa Davide, ansembe, aneneri, pamodzi ndi anthu onse amene akukhala mu Yerusalemu.
14 And I will dash them one against another, Even fathers and children together, saith Jehovah; I will not pity, nor spare, Nor show mercy, so as not to destroy them.
Ndidzawagundanitsa mitu kuti aphwanyane okhaokha ngati mitsuko, makolo ndi ana awo, akutero Yehova. Sindidzawamvera chisoni kapena kuwachitira chifundo kapena kukhudzidwa nawo kuti ndileke kuwawononga.’”
15 Hear ye, and attend! be not lifted up! For Jehovah speaketh.
Imvani inu Aisraeli ndipo tcherani khutu, musadzitukumule, pakuti ndi Yehova amene akuyankhula.
16 Give glory to Jehovah, your God, Before he bring darkness, And your feet stumble upon the dark mountains, And, while ye look for light, He turn it into deathlike shade, And make it gross darkness.
Lemekezani Yehova Mulungu wanu asanagwetse mdima, mapazi anu asanayambe kupunthwa mʼchisisira chamʼmapiri. Asanasandutse kuwala mukuyembekezerako kukhala mdima wandiweyani.
17 But if ye will not hear, I will mourn in secret places for your pride, I will weep continually, And my eyes shall run down with tears, Because the flock of Jehovah is carried away captive.
Koma ngati simumvera, ndidzalira kwambiri chifukwa cha kunyada kwanu. Mʼmaso mwanga mwadzaza ndi misozi yowawa chifukwa nkhosa za Yehova zatengedwa ukapolo.
18 Say to the king and to the queen, Sit ye down upon the ground, For your beautiful crown shall fall from your heads.
Uza mfumu pamodzi ndi amayi ake kuti, “Tsikani pa mipando yaufumuyo, pakuti zipewa zanu zaufumu zokongolazo zagwa pansi.”
19 The cities of the South are shut up, and none openeth them; Judah is carried away captive, all of it, Every man of it is carried away captive.
Mizinda ya ku Negevi yatsekedwa ndipo palibe wina woti nʼkuyitsekula. Yuda yense watengedwa kupita ku ukapolo, watengedwa yense ukapolo.
20 Lift up your eyes, and behold them that come from the North! Where is the flock that was given thee, thy beautiful flock?
Tukula maso ako kuti uwone amene akubwera kuchokera kumpoto. Kodi nkhosa zimene anakusungitsa zili kuti, nkhosa zanu zokongola zija?
21 What wilt thou say when he shall punish thee? For thou thyself hast taught them to be lords over thee. Shall not sorrows seize thee, as a woman in travail?
Kodi udzanena chiyani pamene [Yehova] adzakuyikira anthu amene unkanena kuti ndi abale ako akukugonjetsa ndi kukulamulira? Kodi sudzamva zowawa ngati za mayi pa nthawi yake yochira?
22 And if thou say in thine heart, “Wherefore are these things coming upon me?” For the greatness of thy iniquity are thy skirts uncovered, And thy heels made bare.
Ndipo ngati udzadzifunsa kuti, “Kodi zimenezi zandichitikira chifukwa chiyani?” Ndi chifukwa cha machimo anu ambiri kuti zovala zanu zingʼambike ndiponso kuti akuchitireni nkhanza.
23 Can the Ethiopian change his skin, Or the leopard his spots? Then may ye also do good, Who have been accustomed to do evil.
Kodi wa dziko la Kusi nʼkusintha khungu lake, kapena kambuku kusintha mawanga ake? Inunso amene munazolowera kuchita zoyipa simungathe kusintha.
24 Therefore will I scatter you like stubble, Which passeth away before the wind of the desert.
“Ine ndidzakumwazani ngati mankhusu amene amawuluka ndi mphepo ya ku chipululu.
25 This is thy lot, The portion measured out for thee by me, saith Jehovah, Because thou hast forgotten me, and trusted in falsehood.
Limeneli ndiye gawo lanu, chilango chimene ndakukonzerani chifukwa chondiyiwala Ine ndi kutumikira milungu yabodza, akutero Yehova.
26 Therefore will I lift up thy skirts over thy head, So that thy shame shall be seen.
Ine ndidzakwinya zovala zanu mpaka ku maso kuti umaliseche wanu uwonekere.
27 Thine adulteries, thy neighings, The lewdness of thy whoredom on the hills, in the fields, All thy abominations, have I seen. Woe to thee, O Jerusalem! How long ere thou wilt become pure!
Ndaona zonyansa zanu: zigololo zanu, kutchetcherera kwanu ndi ziwerewere zanu, zochitika pa mapiri ndi mʼminda. Tsoka iwe Yerusalemu! Udzakhala wosayeretsedwa pa zachipembedzo mpaka liti?”

< Jeremiah 13 >