< Jeremiah 11 >

1 The word which came to Jeremiah from Jehovah, saying:
Yehova anayankhula ndi Yeremiya kuti,
2 Hear ye the words of this covenant, And speak ye to the men of Judah, And the inhabitants of Jerusalem.
“Imvani mawu a pangano ili, ndipo uwawuze anthu a ku Yuda ndi a ku Yerusalemu.
3 And say thou to them, Thus saith Jehovah, the God of Israel: Cursed is the man who will not obey the words of this covenant,
Awuze kuti Yehova, Mulungu wa Israeli akuti ‘adzakhala wotembereredwa munthu amene samvera mawu a pangano ili.
4 Which I commanded your fathers, When I brought them forth from the land of Egypt, From the iron furnace, saying, “Obey ye my voice, And do all which I command you; So shall ye be my people, And I will be your God;
Awa anali mawu amene ndinalamulira makolo anu nditawatulutsa mu Igupto, kuchoka mʼngʼanjo yamoto.’ Ine ndinati, ‘Mverani Ine ndi kuchita chilichonse chimene ndakulamulirani. Mukatero mudzakhala anthu anga ndi Ine ndidzakhala Mulungu wanu.
5 So that I may perform the oath, Which I made to your fathers, To give them a land flowing with milk and honey, as it is this day.” Then answered I, and said, So may it be, O Jehovah!
Tsono Ine ndidzakwaniritsa lumbiro lomwe ndinalumbira kwa makolo anu kuti ndidzawapatsa dziko loyenda mkaka ndi uchi,’ dziko lomwe inu lero mukukhalamo.” Tsono Ine ndinayankha kuti, “Ameni, Yehova.”
6 Then said Jehovah to me, Proclaim all these words in the cities of Judah, And the streets of Jerusalem, saying: Hear ye the words of this covenant, and do them!
Yehova anandiwuza kuti, “Lengeza mawu onsewa mʼmizinda yonse ya ku Yuda ndi mʼmisewu ya mu Yerusalemu: ‘Mverani mawu a pangano ili ndi kuzitsatira.
7 For I have earnestly admonished your fathers, From the time when I brought them up from the land of Egypt to this day, Rising early and admonishing them, saying, “Obey ye my voice!”
Kuyambira nthawi imene ndinatulutsa makolo anu ku Igupto mpaka lero, ndakhala ndi kuwachenjeza kawirikawiri kuti, ‘Mverani Ine.’
8 Yet they obeyed not, nor inclined their ear, But walked every one in the obstinacy of his evil heart; Therefore have I brought upon them all the words of this covenant, Which I commanded them to obey, And they obeyed not.
Koma sanamvere kapena kulabadirako. Aliyense anawumirira kuchita zoyipa za mʼmitima yawo. Ngakhale ndinawalamulira kuti asunge pangano langa koma iwo sanasunge. Choncho ndinawalanga monga ndinaneneramo.’”
9 Jehovah also said to me: A conspiracy hath been found among the men of Judah, And the inhabitants of Jerusalem.
Kenaka Yehova anandiwuza kuti, “Anthu a ku Yuda ndi ku Yerusalemu andiwukira.
10 They turn back to the iniquities of their forefathers, Who refused to hearken to my words; They go after strange gods and serve them; The house of Israel and the house of Judah have broken the covenant Which I made with their fathers.
Abwereranso ku machimo a makolo awo, amene anakana kumvera mawu anga. Akutsata milungu ina ndi kumayitumikira. Aisraeli ndi Ayuda aphwanya pangano limene ndinachita ndi makolo awo.
11 Therefore thus saith Jehovah: Behold I bring upon them a calamity, From which they shall not be able to escape; And though they cry to me, I will not hear them.
Choncho Yehova akuti, ‘Ndidzawagwetsera mavuto amene sadzatha kuwalewa. Ngakhale adzandilirire, sindidzawamvera.
12 Then may the cities of Judah and the inhabitants of Jerusalem go, And cry to the gods to whom they burn incense; But they shall not save them at all in the time of their calamity.
Anthu a mʼmizinda ya Yuda ndi anthu a ku Yerusalemu adzapita ndi kukalirira milungu imene ankayifukizira lubani, koma milunguyo sidzawathandiza ndi pangʼono pomwe mavuto akadzafika.
13 For according to the number of thy cities are thy gods, O Judah! According to the number of the streets of Jerusalem have ye set up altars to a thing of shame, Altars for burning incense to Baal.
Iwe Yuda, uli ndi milungu yochuluka ngati chiwerengero cha mizinda yako; chiwerengero cha maguwa ansembe amene umafukizirapo lubani kwa Baala chili ngati misewu ya mu Yerusalemu.’
14 Therefore pray not thou for this people, Nor lift up a cry or a prayer for them; For I will not hear when they cry to me On account of their calamity.
“Tsono iwe Yeremiya usawapempherere anthu amenewa ngakhale kuwadandaulira kapena kuwapepesera, chifukwa sindidzawamvera akadzandiyitana pa nthawi ya mavuto awo.
15 What hath my beloved to do in my house, While many pollute it with wickedness? The holy flesh shall pass away from thee, For when thou doest evil, thou rejoicest.
“Kodi anthu anga okondedwa akudzachita chiyani mʼNyumba yanga? Kodi suja iwowa amachita zoyipa zambiri? Kodi mungathe kupulumuka, tsoka osakugwerani chifukwa cha nsembe zanuzo?”
16 Jehovah hath called thee an olive-tree, Green, fair, and of goodly fruit; With the noise of a great crackling doth he kindle a fire upon it, And the branches of it shall be broken.
Kale Yehova ankakutchani mtengo wa olivi wa masamba obiriwira, wokhala ndi zipatso zokongola. Koma tsopano adzawutentha ndi mkuntho wamkokomo ndipo nthambi zake zidzapserera.
17 For Jehovah of hosts, who planted thee, Hath pronounced evil against thee, On account of the wickedness of the house of Israel and of Judah, which they have committed In provoking me to anger by burning incense to Baal.
Yehova Wamphamvuzonse, amene anakudzalani, walamula kuti mavuto akugwereni. Inu a banja la Yuda ndi a banja la Israeli munachitira Yehova zoyipa ndi kumukwiyitsa pamene munkapereka nsembe zanu kwa Baala.
18 Jehovah made it known to me, and I knew it; Thou didst show me their machinations!
Yehova anandiwululira ndipo ndinadziwa. Iye anatsekula maso anga kuti ndione chiwembu chawocho.
19 For I was like a tame lamb, that is led to the slaughter, And knew not that they had formed plots against me, [[saying, ]] “Let us destroy the tree with its fruit, Let us cut him off from the land of the living, That his name may no more be remembered!”
Ndinali ngati mwana wankhosa wofatsa amene akupita naye kukamupha; sindinkadziwa kuti chiwembu chimene ankakonzekeracho chinkaloza ine. Iwo amati: “Tiyeni timuphe munthu ameneyu kuti dzina lake lisadzakumbukiridwenso.”
20 But, O Jehovah of hosts, the righteous judge, Who triest the reins and the heart, I shall see thy vengeance on them, For to thee have I revealed my cause!
Koma, Inu Yehova Wamphamvuzonse, Inu amene mumaweruza molungama ndi kuyesa mitima ndi maganizo, lolani kuti ine ndione kuti mwawalipsira, pakuti mlandu wanga ndawupereka mʼmanja mwanu.
21 Therefore thus saith Jehovah against the men of Anathoth, Who seek thy life, and say, “Prophesy not in the name of Jehovah, Lest thou die by our hand!”
“Nʼchifukwa chake Yehova akunena za anthu a ku Anatoti amene akufuna kuwononga moyo wako namanena kuti, ‘Usanenere mʼdzina la Yehova, ukatero ife tidzakupha ndi manja athu,’
22 Therefore thus saith Jehovah of hosts: Behold, I will punish them; Their young men shall die by the sword; Their sons and their daughters shall die by famine,
koma Yehova Wamphamvuzonse akuti, ‘Ine ndidzawalanga. Achinyamata awo adzaphedwa ndi lupanga, ana awo aamuna ndi aakazi adzafa ndi njala.
23 There shall be none of them left; For I will bring evil upon the men of Anathoth, At the time of their punishment.
Sipadzakhala otsala ndi mmodzi yemwe, chifukwa ndidzalanga anthu a ku Anatoti chikadzafika chaka chawo cha chilango.’”

< Jeremiah 11 >