< Isaiah 46 >

1 Bel sinketh down; Nebo falleth; Their images are laid upon beasts and cattle; Those that ye once bore are packed upon them; A burden to the weary beast!
Beli wagwada pansi, Nebo wawerama; nyama zonyamula katundu za nyamula milungu yawo. Mafano awo asanduka katundu wolemera pa msana pa ngʼombe. Asandukadi ngati katundu pa msana pa nyama zotopa.
2 They sink down; they fall together; They cannot rescue the burden; They themselves go into captivity.
Nyamazo zikuwerama ndi kufuna kugwa ndi milunguyo; sizikutha kupulumutsa katunduyo, izo zomwe zikupita ku ukapolo.
3 Hearken to me, O house of Jacob, And all the remnant of the house of Israel; Ye that have been borne by me from your birth, That have been carried by me from your earliest breath!
Mverani Ine, Inu nyumba ya Yakobo, inu nonse otsala a mʼnyumba ya Israeli, Ine ndakhala ndi kukusamalirani kuyambira mʼmimba ya amayi anu, ndakhala ndikukunyamulani chibadwire chanu.
4 Even to your old age I am the same; Even to hoar hairs I will carry you; I have done it, and I will still bear you; I will carry, and will deliver you.
Mpaka pamene mudzakalambe ndi kumera imvi ndidzakusamalirani ndithu. Ndinakulengani ndipo ndidzakunyamulani, ndidzakusamalirani ndi kukulanditsani.
5 To whom will ye liken me, and compare me? Yea, to whom will ye compare me, that we may be like?
“Kodi inu mudzandifanizira ndi yani, kapena mufananitsa ndi yani? Kodi mudzandiyerekeza kapena kundifanizitsa ndi yani?
6 They lavish gold out of the bag, And weigh silver in the balance; They hire a goldsmith, and he maketh it a god; They fall down, yea, they worship it.
Anthu ena amakhuthula golide mʼzikwama zawo ndipo amayeza siliva pa masikelo; amalemba ntchito mʼmisiri wosula kuti awapangire mulungu, kenaka iwo amagwada pansi ndikupembedza kamulunguko.
7 They lift him upon the shoulder, and carry him; They set him in his place, and there he standeth; From his place he moveth not; Yea, one may cry to him, yet doth he not answer, Nor save him out of his distress.
Amanyamula nʼkumayenda nayo milunguyo pa mapewa awo; amayikhazika pa malo pake ndipo imakhala pomwepo. Singathe kusuntha pamalo pakepo. Ngakhale wina apemphere kwa milunguyo singathe kuyankha; kapena kumupulumutsa ku mavuto ake.
8 Remember these things, and show yourselves men; Lay them to heart, ye apostates!
“Kumbukirani zimenezi ndipo muchite manyazi, Muzilingalire mu mtima, inu anthu owukira.
9 Remember the former things in ancient times! For I am God, and there is none else; I am God, and there is none like me.
Kumbukirani zinthu zakale zinthu zamakedzana; chifukwa Ine ndine Mulungu ndipo palibe wina ofanana nane.
10 Declaring the end from the beginning; From ancient times the things that were not yet done; Saying, My purpose shall stand, And I will do all my pleasure;
Ndinaneneratu zakumathero kuchokera pachiyambi pomwe. Kuyambira nthawi yamakedzana ndinaloseratu zoti zidzachitike. Ndikanena zimene ndifuna kuchita ndipo zimachitikadi. Chilichonse chimene ndafuna ndimachichita.
11 Calling from the East the eagle, The man that executeth my purpose from a far country; I have spoken it, I will also bring it to pass; I have purposed it, I will also do it.
Ndikuyitana chiwombankhanga kuchokera kummawa. Ndikuyitana kuchokera ku dziko lakutali munthu amene adzakwaniritsa cholinga changa. Zimene ndanena ndidzazikwaniritsadi; zimene ndafuna ndidzazichitadi.
12 Hearken to me, ye stubborn-hearted, That are far from deliverance!
Ndimvereni, inu anthu owuma mtima, inu amene muli kutali ndi chipulumutso.
13 I have brought near my deliverance; it is not far off; My salvation shall not tarry; I will give to Zion salvation, To Israel, my glory.
Ndikubweretsa pafupi tsiku la chipulumutso changa; sichili kutali. Tsikulo layandikira ndipo sindidzachedwa kukupulumutsani ndi kupereka ulemerero wanga kwa Israeli.

< Isaiah 46 >