< Isaiah 35 >
1 The wilderness and the parched land shall be glad, And the desert rejoice and blossom as the rose;
Chipululu ndi dziko lopanda madzi zidzasangalala; dziko lowuma lidzakondwa ndi kuchita maluwa.
2 It shall blossom abundantly, and exult with joy and singing; The glory of Lebanon shall be given to it; The beauty of Carmel and Sharon; They shall behold the glory of Jehovah, The majesty of our God;
Dzikolo lidzakhala ndi maluwa ochuluka lidzasangalala kwambiri ndi kufuwula mwachimwemwe. Lidzakhala ndi ulemerero monga wa ku mapiri a ku Lebanoni, maonekedwe ake wokongola adzakhala ngati a ku Karimeli ndi a ku Saroni. Aliyense adzaona ulemerero wa Yehova, ukulu wa Mulungu wathu.
3 Strengthen ye the weak hands, And confirm the tottering knees!
Limbitsani manja ofowoka, limbitsani mawondo agwedegwede;
4 Say ye to the faint-hearted, “Be ye strong; fear ye not; Behold your God! Vengeance cometh, the retribution of God; He will come and save you!”
nenani kwa a mitima yamantha kuti; “Limbani mtima, musachite mantha; Mulungu wanu akubwera, akubwera kudzalipsira; ndi kudzabwezera chilango adani anu; akubwera kudzakupulumutsani.”
5 Then shall the eyes of the blind be opened, And the ears of the deaf be unstopped.
Pamenepo maso a anthu osaona adzapenyanso ndipo makutu a anthu osamva adzatsekuka.
6 Then shall the lame leap like the hart, And the tongue of the dumb shall sing; For in the wilderness shall waters break forth, And streams in the desert.
Anthu olumala adzalumpha ngati mbawala, ndipo osayankhula adzayimba mokondwera. Akasupe adzatumphuka mʼchipululu ndipo mitsinje idzayenda mʼdziko lowuma,
7 The glowing sands shall become a pool, And the thirsty ground springs of water; In the habitation of jackals, where they lie, Shall be a place for reeds and rushes.
mchenga wotentha udzasanduka dziwe, nthaka yowuma idzasanduka ya akasupe. Pamene panali mbuto ya ankhandwe padzamera udzu ndi bango.
8 And a path shall be there, and a highway, And it shall be called the holy way; No unclean person shall pass over it; it shall be for them alone; He that therein goeth in this way, though a fool, shall not err therein.
Ndipo kumeneko kudzakhala msewu waukulu; ndipo udzatchedwa Msewu Wopatulika. Anthu odetsedwa sadzayendamo mʼmenemo; zitsiru sizidzasochera mʼmenemo.
9 No lion shall be there, Nor shall any ravenous beast go up thereon; It shall not be found there; But the redeemed shall walk there.
Kumeneko sikudzakhala mkango, ngakhale nyama yolusa sidzafikako; sidzapezeka konse kumeneko. Koma okhawo amene Yehova anawapulumutsa adzayenda mu msewu umenewu.
10 Yea, the ransomed of Jehovah shall return; They shall come to Zion with songs: Everlasting joy shall be upon their heads; They shall obtain joy and gladness, And sorrow and sighing shall flee away.
Iwo amene Yehova anawawombola adzabwerera. Adzalowa mu mzinda wa Ziyoni akuyimba; kumeneko adzakondwa mpaka muyaya. Adzakutidwa ndi chisangalalo ndi chimwemwe, ndipo chisoni ndi kudandaula zidzatheratu.