< Isaiah 27 >

1 In that day will Jehovah punish with his sword, His hard, and great, and strong sword, The leviathan, that fleet serpent, Even the leviathan, that winding serpent; Yea, he will slay the monster, that is in the sea.
Tsiku limenelo, Yehova ndi lupanga lake lakuthwa, lalikulu ndi lamphamvu, adzalanga Leviyatani chinjoka chothawa chija, Leviyatani chinjoka chodzikulunga; adzapha chirombo choopsa cha mʼnyanja.
2 In that day, sing ye thus concerning the vineyard:
Tsiku limenelo Yehova adzati, “Tidzayimba nyimbo ya munda wamphesa wobereka bwino:
3 “I, Jehovah, am its guardian; I will water it every moment; That no one may assault it, I will watch it day and night.
Ine, Yehova, ndimawuyangʼanira; ndimawuthirira nthawi zonse. Ndimawulondera usana ndi usiku kuti wina angawononge.
4 There is no fury in me; But let me find the thorns and thistles in battle. I will go against them, And burn them up together,
Ine sindinakwiye. Ngati mkandankhuku ndi minga zikanaoneka ndikanalimbana nazo! Ndikachita nazo nkhondo; ndikanazitentha zonse ndi moto.
5 Unless they take hold of my protection, And with me make peace, And make peace with me.”
Koma ngati apo ayi, abweretu kwa Ine adani angawo kuti ndidzawateteze; apangane nane za mtendere, ndithu, apangane nane za mtendere.”
6 In coming days shall Jacob take root, And Israel flourish and bud forth, And fill the world with fruit.
Masiku akubwerawo Yakobo adzazika mizu, Israeli adzaphukira ndi kuchita maluwa, ndipo adzadzaza dziko lonse lapansi ndi zipatso.
7 Did he smite Israel, as he smote those that smote him? Was he slain as those that slew him?
Kodi Yehova anakantha Israeli ngati momwe anakanthira anthu amene anazunza Israeli? Kapena kodi Yehova anapha Israeli ngati mmene anthu ena anaphera Israeli?
8 In measure, by sending her away, didst thou punish her, Taking her away in the rough tempest, in the day of the east wind.
Yehova mwawalanga powapirikitsa ndi kuwatumiza ku ukapolo, mwawachotsa ndi mpweya wanu woopsa, monga zimachitikira pa tsiku la mkuntho wochokera kummawa.
9 By this, therefore, is the iniquity of Jacob expiated, And this is wholly the fruit of the removal of his sin, That He has made the stones of the altar like limestones broken in pieces, And that the images of Astarte and the sun-pillars no more stand.
Yehova adzakhululuka kulakwa kwa Yakobo. Iwo adzaonetsa kuti alapadi pamene adzaphwanya miyala yonse ya guwa lachikunja, ngati mmene anthu amaphwanyira miyala yanjereza mpaka kukhala ngati fumbi lokhalokha. Sipadzapezekanso mafano a Asera kapena maguwa ofukiza lubani.
10 For the fortified city is desolate, A habitation forsaken, deserted like a wilderness; There doth the calf feed, and there doth he lie down, And consume her branches.
Mzinda wamalinga uja wasanduka bwinja, wasanduka malo osiyidwa, ndi kutayidwa ngati chipululu; kumeneko amadyetselako ana angʼombe kumeneko zimapumulako ziweto ndi kumwetula nthambi za mitengo kotheratu.
11 When her boughs are withered, they are broken off; Women come, and burn them; For it was a people of no understanding; Therefore he that made him had not mercy on him, And he that formed him showed him no favor.
Pamene nthambi za mitengoyo zauma, zimathyoka ndipo amayi amabwera nazitola ndi kuzisandutsa nkhuni. Pakuti awa ndi anthu opanda nzeru; kotero Mulungu amene anawapanga sadzachitira chisoni, ndipo Mlengi wawo sawakomera mtima.
12 But it shall come to pass in that day, That Jehovah shall gather fruit From the stream of the Euphrates to the river of Egypt, And ye shall be gathered, one by one, ye children of Israel!
Tsiku limenelo Yehova adzasonkhanitsa pamodzi anthu ake mmodzimmodzi kumalo opunthira tirigu, kuchokera ku mtsinje wa Yufurate mpaka ku mtsinje wa ku Igupto.
13 In that day shall a great trumpet be sounded, And they shall come who are lost in the land of Assyria, And are outcasts in the land of Egypt, And shall worship Jehovah upon the holy mountain in Jerusalem.
Ndipo tsiku limenelo lipenga lalikulu lidzalira. Amene akuzunzika ku Asiriya iwo amene ali ku ukapolo ku Igupto adzabwera ndi kudzalambira Yehova pa phiri lopatulika mu Yerusalemu.

< Isaiah 27 >