< Hosea 1 >
1 The word of Jehovah, which came to Hoses, the son of Beeri, in the days of Uzziah, Jotham, Ahaz, and Hezekiah, kings of Judah, and in the days of Jeroboam, the son of Joash, king of Israel.
Awa ndi mawu amene Yehova anayankhula kwa Hoseya mwana wa Beeri pa nthawi ya ulamuliro wa Uziya, Yotamu, Ahazi ndi Hezekiya, mafumu a ku Yuda ndiponso pa nthawi ya ulamuliro wa Yeroboamu mwana wa Yowasi mfumu ya ku Israeli.
2 The beginning of the word of Jehovah by Hosea. Jehovah said to Hosea: Go, and take thee a wife of lewdness, and children of lewdness; for the land hath committed great lewdness; it is false to Jehovah.
Yehova atayamba kuyankhula kudzera mwa Hoseya, Yehova anati kwa Hoseyayo, “Pita kakwatire mkazi wachiwerewere ndipo ubereke naye ana mʼchiwerewere chake pakuti anthu a mʼdziko muno achimwa pochita chigololo choyipitsitsa, posiya Yehova.”
3 So he went, and took Gomer, the daughter of Diblaim; and she conceived and bore him a son.
Motero Hoseya anakwatira Gomeri mwana wamkazi wa Dibulaimu, ndipo mkaziyo anakhala woyembekezera nabala mwana wamwamuna.
4 And Jehovah said to him, Call his name Jezreel; for yet a little while, and I will avenge the blood of Jezreel upon the house of Jehu, and will bring the kingdom of the house of Israel to an end.
Tsono Yehova anati kwa Hoseya, “Umutche dzina loti Yezireeli, pakuti ndili pafupi kulanga banja la Yehu chifukwa cha anthu amene anawapha ku Yezireeli ndipo ndidzathetsa ufumu wa Israeli.
5 Yea, in that day will I break the bow of Israel in the valley of Jezreel.
Tsiku limenelo ndidzathyola uta wa Israeli mʼchigwa cha Yezireeli.”
6 And she conceived again, and bore a daughter. And God said to him, Call her name Unpitied; for I will no more have pity upon the house of Israel, but will surely take them away.
Gomeri anakhala woyembekezeranso ndipo anabereka mwana wamkazi. Ndipo Yehova anati kwa Hoseya, “Umutche dzina loti ‘Sakondedwa’ pakuti sindidzaonetsanso chikondi changa pa nyumba ya Israeli, kuti ndingawakhululukire konse.
7 But upon the house of Judah will I have pity, and will save them by Jehovah their God; I will not save them by bow, nor by sword, nor by battle, nor by horses, nor by horsemen.
Komatu ndidzaonetsa chikondi pa nyumba ya Yuda; ndipo ndidzawapulumutsa, osati ndi uta, lupanga kapena nkhondo, kapena akavalo ndi okwerapo ake, koma ine Yehova Mulungu wawo ndidzawapulumutsa.”
8 Then she weaned her daughter Unpitied, and conceived, and bore a son.
Sakondedwa ataleka kuyamwa, Gomeri anabereka mwana wina wamwamuna.
9 And God said, Call his name Not-my-people. For ye are not my people, and I will not be your God.
Pamenepo Yehova anati, “Umutche dzina loti Sianthuanga,” pakuti inu si ndinu anthu anga ndipo Ine si ndine Mulungu wanu.
10 Yet the number of the children of Israel shall be as the sand of the sea, which cannot be measured, or numbered; and in the place where it was said to them, Ye are not my people, there shall it be said to them, Ye are the sons of the living God.
“Komabe Aisraeli adzachuluka ngati mchenga wa mʼmbali mwa nyanja umene sangathe kuwuyeza kapena kuwuwerenga. Pamalo omwe ananena kuti, ‘Sindinu anthu anga,’ pomweponso adzawatchula kuti ‘Ana a Mulungu wamoyo.’
11 Then shall the sons of Judah and the sons of Israel be gathered together, and shall appoint to themselves one head, and shall come up out of the land. For great shall be the day of Jezreel.
Anthu a ku Yuda ndi anthu a ku Israeli adzasonkhananso pamodzi ndipo adzasankha mtsogoleri mmodzi ndi kutuluka mʼdzikomo, pakuti tsiku la Yezireeli lidzakhala lalikulu kwambiri.”