< Hosea 12 >
1 Ephraim feedeth on wind, and followeth after the east wind; Every day he multiplieth falsehood and violence; They make a league with Assyria, And oil is carried into Egypt.
Efereimu amadya mpweya; tsiku lonse amasaka mphepo ya kummawa ndipo amachulukitsa mabodza ndi chiwawa. Amachita mgwirizano ndi Asiriya ndipo amatumiza mphatso za mafuta a olivi ku Igupto.
2 Therefore Jehovah hath a controversy with Judah. And he will punish Jacob for his ways, And requite him according to his doings.
Yehova akuyimba mlandu Yuda; Iye adzalanga Yakobo molingana ndi makhalidwe ake, adzamulanga molingana ndi ntchito zake.
3 In the womb he took his brother by the heel, And in his strength he contended with God;
Akali mʼmimba mwa amayi ake, Yakobo anagwira chidendene cha mʼbale wake; iye atakula analimbana ndi Mulungu.
4 Yea, he contended with the angel, and prevailed; He wept, and made supplication to him. At Bethel he found him, And there he spake with us.
Yakobo analimbana ndi mngelo ndipo anapambana; analira napempha kuti amukomere mtima. Mulungu anakumana naye ku Beteli ndipo anayankhula naye kumeneko,
5 And Jehovah, the God of hosts, Jehovah is his name.
Yehova Mulungu Wamphamvuzonse, Yehova ndiye dzina lake lotchuka!
6 Therefore turn thou to thy God; Observe mercy and justice, And hope in thy God always!
Koma inu muyenera kubwerera kwa Mulungu wanu; pitirizani chikondi ndi chiweruzo cholungama, ndipo muzidikira Mulungu wanu nthawi zonse.
7 He is a Canaanite; in his hands are the balances of deceit; He loveth to oppress.
Munthu wamalonda amagwiritsa ntchito masikelo achinyengo; iyeyo amakonda kubera anthu.
8 Yet Ephraim saith, Lo, I have become rich; I have found myself substance; In all my earnings can be found no transgression in which there is guilt.
Efereimu amadzitama ponena kuti, “Ndine wolemera kwambiri; ndili ndi chuma chambiri. Palibe amene angandiloze chala chifukwa cha kulemera kwanga.”
9 Yet I, Jehovah, have been thy God from the land of Egypt; I will again cause thee to dwell in tents, as in the days of the solemn feast.
“Ine ndine Yehova Mulungu wako amene ndinakutulutsa mu Igupto. Ndidzakukhazikaninso mʼmatenti, monga munkachitira masiku aja pa nthawi ya zikondwerero zanu.
10 I have also spoken to the prophets, And I have given many visions, And by the prophets I have used similitudes.
Ndinayankhula ndi aneneri, ndinawaonetsa masomphenya ambiri, ndipo ndinawawuza mafanizo kudzera mwa iwo.”
11 Behold, Gilead is full of iniquity; Surely they have become corrupt; In Gilgal they sacrifice oxen, And their altars are like the heaps in the furrows of the field.
Kodi Giliyadi ndi woyipa? Anthu ake ndi achabechabe! Kodi amapereka nsembe za ngʼombe zazimuna ku Giligala? Maguwa awo ansembe adzakhala ngati milu ya miyala mʼmunda molimidwa.
12 Jacob fled into the country of Syria, And Israel served for a wife, And for a wife he kept sheep.
Yakobo anathawira ku dziko la Aramu, Israeli anagwira ntchito kuti apeze mkazi, ndipo anaweta nkhosa kuti akwatire mkaziyo.
13 By a prophet Jehovah brought up Israel out of Egypt, And by a prophet was he preserved.
Yehova anagwiritsa ntchito mneneri kuti atulutse Israeli mu Igupto; kudzera mwa mneneriyo Iye anawasamalira.
14 Ephraim hath provoked his Lord most bitterly; Therefore will he leave his blood upon him, And recompense to him his reproach.
Koma Efereimu wamukwiyitsa kwambiri. Nʼchifukwa chake Yehova adzawalanga ndi imfa. Adzawalanga chifukwa anamuchititsa manyazi kwambiri.