< Ezekiel 15 >

1 And the word of Jehovah came to me, saying:
Yehova anayankhulanso nane kuti,
2 Son of man, what is the wood of the vine more than any wood, —a branch, that is among the trees of the forest?
“Iwe mwana wa munthu, kodi mtengo wamphesa umapambana bwanji mtengo wina uliwonse? Nthambi zake zimapambana bwanji nthambi ina iliyonse.
3 Shall wood be taken from it to be wrought into any work? Or will men take a pin of it to hang a vessel upon?
Mtengo umene uja nʼkupangira chiyani? Kodi anthu angathe kupangira chikhomo chokolekapo zinthu zawo?
4 Behold, it is cast into the fire for fuel; the fire devoureth both the ends of it, and the middle of it is burned. Is it then fit for any work?
Taonani, ndi nkhuni chabe zosonkhera moto. Ukaponyedwa pa moto monga nkhuni ndi kuyaka mbali zonse ndi kusanduka makala, kodi ungagwiritsidwe ntchito ina iliyonse?
5 Behold, when it was whole, nothing could be made of it; how much less can anything be made of it when the fire hath devoured it and it is burned!
Ngati pamene unali wosapsa sukanatheka kuwugwiritsa ntchito, nanga bwanji utapserera ndi moto, adzawugwiritsa ntchito bwanji?
6 Therefore thus saith the Lord Jehovah: As the wood of the vine among the trees of the forest, which I have given to the fire for fuel, so will I give to it the inhabitants of Jerusalem.
“Nʼchifukwa chake Ambuye Yehova akuti, ‘Mtengo wamphesa ndidzawuponya mʼmoto monga ndimachitira ndi mitengo ina ya ku nkhalango. Momwemonso ndidzachita ndi anthu a ku Yerusalemu.
7 And I will set my face against them; they shall go out from one fire, and another fire shall devour them; and ye shall know that I am Jehovah, when I set my face against them.
Ndidzawalanga pamenepo ngakhale iwo atuluka pa moto, motowo udzawatenthabe. Ndipo pamene ndidzatsutsana nawo, mudzadziwa kuti Ine ndine Yehova.
8 And I will make the land desolate, because they have grievously trespassed, saith the Lord Jehovah.
Ine ndidzasandutsa dziko kukhala chipululu chifukwa anthu akhala osakhulupirika, akutero Ambuye Yehova.’”

< Ezekiel 15 >