< Amos 9 >

1 I saw the Lord standing by the altar; and he said: Smite the capital, so that the thresholds shall tremble! Break them in pieces upon the heads of all of them! And their residue will I slay with the sword. He that fleeth of them shall not flee from danger, And he that escapeth of them shall not escape into safety.
Ine ndinaona Ambuye atayima pambali pa guwa lansembe, ndipo anati: “Kantha mitu ya nsanamira kuti ziwundo za nyumba zigwedezeke. Muzigwetsere pa mitu ya anthu onse, onse amene atsalira ndidzawapha ndi lupanga. Palibe ndi mmodzi yemwe amene adzathawe, palibe amene adzapulumuke.
2 Though they dig down to the under-world, Thence shall my hand take them; Though they climb up to heaven, Thence will I bring them down. (Sheol h7585)
Ngakhale atakumba pansi mpaka ku malo a anthu akufa, dzanja langa lidzawatulutsa kumeneko. Ngakhale atakwera kumwamba Ine ndidzawatsakamutsa kumeneko. (Sheol h7585)
3 Though they hide themselves on the top of Carmel, There will I search for them, and take them away; Though they hide themselves from mine eyes in the bottom of the sea, There will I command the serpent, and he shall bite them.
Ngakhale atakabisala pamwamba pa phiri la Karimeli, Ine ndidzawasaka kumeneko ndi kuwagwira. Ngakhale atakabisala pansi pa nyanja yayikulu, ndidzalamula njoka kuti iwalume kumeneko.
4 Though they go into captivity before their enemies, There will I command the sword, and it shall slay them; I will set mine eyes upon them for evil, and not for good.
Ngakhale adani awo awakusire ku ukapolo, ndidzalamula lupanga kuti liwaphe kumeneko. Ndidzawayangʼanitsitsa kuti zoyipa ziwagwere; osati zabwino.”
5 For the Lord Jehovah of hosts Is he, that toucheth the earth, and it shall melt, And all that dwell therein shall mourn; All of it shall rise in waves like a river, And shall be overflowed, as by the river of Egypt;
Ambuye Yehova Wamphamvuzonse amene amakhudza dziko lapansi ndipo dzikolo limasungunuka, onse amene amakhala mʼmenemo amalira. Dziko lonse lidzadzaza ngati mtsinje wa Nailo, kenaka nʼkuphwera ngati mtsinje wa ku Igupto.
6 He that buildeth his upper rooms in the heavens, And foundeth his arch upon the earth, —That calleth the waters of the sea, And poureth them out upon the face of the earth, —Jehovah is his name.
Iye amene amamanga malo ake okhalamo kumwamba, ndi kuyika maziko ake pa dziko lapansi, Iye amene amayitana madzi a ku nyanja ndikuwakhuthulira pa dziko lapansi, dzina lake ndiye Yehova.
7 Are ye not as the Ethiopians to me, O children of Israel? saith Jehovah. Did I not bring Israel from the land of Egypt, And the Philistines from Caphtor, and the Syrians from Kir?
“Kodi kwa Ine, inu Aisraeli, simuli chimodzimodzi ndi Akusi?” Akutero Yehova. “Kodi sindine amene ndinatulutsa Israeli ku Igupto, Afilisti ku Kafitori ndi Aaramu ku Kiri?
8 Behold, the eyes of the Lord Jehovah are upon the sinful kingdom, And I will destroy it from the face of the earth; Yet will I not utterly destroy the house of Jacob, saith Jehovah.
“Taonani, maso a Ambuye Yehova ali pa ufumu wochimwawu. Ndidzawufafaniza pa dziko lapansi. Komabe sindidzawononga kotheratu nyumba ya Yakobo,” akutero Yehova.
9 For, behold, I will command, And I will sift the house of Israel among all the nations, As one sifteth corn with a sieve, And not a grain shall fall upon the ground.
“Pakuti ndidzalamula, ndipo ndidzagwedeza nyumba ya Israeli pakati pa mitundu yonse ya anthu monga momwe amasefera ufa mʼsefa, koma palibe nʼkamwala kamodzi komwe kamene kadzagwe pansi.
10 But all the sinners of my people shall die by the sword, Who say, Evil shall not approach, nor fall upon us.
Anthu onse ochimwa pakati pa anthu anga adzaphedwa ndi lupanga, onse amene amanena kuti, ‘Tsoka silidzatigwera ife kapena kutiwononga.’
11 In that day I will raise up the fallen tabernacle of David, And I will close up the breaches thereof, And raise up its ruins, And I will build it, as in the days of old.
“Tsiku limenelo ndidzabwezeretsa nyumba ya Davide imene inagwa. Ndidzakonzanso malo amene anagumuka, ndi kuyimanganso monga inalili poyamba,
12 That they may possess the remnant of Edom, And all the nations, which shall be called by my name. Thus saith Jehovah, who doeth this.
kuti adzatengenso otsala a Edomu ndi mitundu yonse imene imatchedwa ndi dzina langa,” akutero Yehova amene adzachita zinthu izi.
13 Behold the days come, saith Jehovah, That the plougher shall draw near to the reaper, And the treader of grapes to the sower of the seed; And the mountains shall drop new wine, And all the hills shall melt.
Yehova akunena kuti “Nthawi ikubwera pamene mlimi wotipula adzapyola wokolola ndipo woponda mphesa adzapyola wodzala mbewu. Mapiri adzachucha vinyo watsopano ndi kuyenderera pa zitunda zonse.
14 I will bring back the captives of my people Israel, And they shall build the desolate cities, and shall inhabit them; And they shall plant vineyards, and drink their wine; They shall also make gardens, and eat their fruit.
Ndidzawabwezeranso pabwino anthu anga Aisraeli; mizinda imene inali mabwinja idzamangidwanso ndipo azidzakhalamo. Adzalima minda ya mpesa ndipo adzamwa vinyo wake; adzalima minda ndipo adzadya zipatso zake.
15 I will plant them in their land, And they shall no more be rooted up from the land which I have given them, Saith Jehovah, thy God.
Ndidzakhazika Aisraeli mʼdziko mwawo, ndipo sadzachotsedwamonso mʼdziko limene Ine ndawapatsa,” akutero Yehova Mulungu wako.

< Amos 9 >