< Amos 7 >

1 The Lord Jehovah showed me this vision: Behold, he formed locusts In the beginning of the shooting up of the latter growth; Behold, it was the latter growth after the king's mowing.
Zimene Ambuye Yehova anandionetsa ndi izi: Yehova ankasonkhanitsa gulu la dzombe nthawi imene gawo la zokolola za mfumu linali litakololedwa kale ndipo mbewu zachiwiri zinali zitangoyamba kumera kumene.
2 And when they had devoured the grass of the land, Then said I, O Lord Jehovah, forgive, I beseech thee! How shall Jacob stand? For he is small!
Dzombelo litadya zomera zonse za mʼdzikomo, Ine ndinafuwula kuti, “Ambuye Yehova, khululukani! Kodi Yakobo adzapulumuka bwanji? Iye ndi wofowoka kwambiri!”
3 Jehovah repented of this; It shall not be, said Jehovah.
Kotero Yehova anakhululuka. Yehovayo anati, “Izi sizidzachitika.”
4 The Lord Jehovah also showed me this vision: Behold, the Lord Jehovah commanded the fire to execute judgment; And it devoured the great deep, And it devoured the fields.
Zimene Ambuye Yehova anandionetsa ndi izi: Ambuye Yehova ankayitana malawi a moto kuti alange anthu. Motowo unawumitsa nyanja yakuya ndi kupsereza dziko.
5 Then said I, O Lord Jehovah, desist, I beseech thee! How shall Jacob stand? For he is small!
Tsono ine ndinafuwula kuti, “Ambuye Yehova, chonde ndikukupemphani, lekani! Kodi Yakobo adzapulumuka bwanji? Iye ndi wofowoka kwambiri!”
6 Jehovah repented of this; This also shall not be, said the Lord Jehovah.
Kotero Yehova anakhululuka. Ambuye Yehova anati, “Izinso sizidzachitika.”
7 He also showed me this vision: Behold, the Lord stood upon a wall, built with a plumb-line, And in his hand was a plumb-line;
Zimene Iye anandionetsa ndi izi: Ambuye anayima pambali pa khoma lomangamanga, mʼmanja mwake muli chingwe chowongolera khoma.
8 And Jehovah said to me, What seest thou, Amos? And I said, A plumb-line. And the Lord said, Behold I will set a plumb-line in the midst of my people Israel; I will not spare them any more.
Ndipo Ambuye anandifunsa kuti, “Amosi, nʼchiyani ukuonachi?” Ine ndinayankha kuti, “Chingwe chowongolera khoma.” Ndipo Yehova anati, “Taona, Ine ndikuyika chingwe chowongolerachi pakati pa anthu anga, Aisraeli; sindidzawalekereranso.
9 The high places of Isaac shall be desolate, And the sanctuaries of Israel shall be laid waste, And I will rise against the house of Jeroboam with the sword.
“Malo achipembedzo a Isake adzawonongedwa ndipo malo opatulika a Israeli adzasanduka bwinja; ndidzagwetsa nyumba ya Yeroboamu ndi lupanga langa.”
10 Then sent Amaziah, the priest of Bethel, To Jeroboam, the king of Israel, and said: Amos conspireth against thee in the midst of the house of Israel; The land is not able to bear all his words.
Pamenepo Amaziya wansembe wa ku Beteli anatumiza uthenga kwa Yeroboamu mfumu ya Israeli kuti, “Amosi akukuutsirani chiwembu pakati pa Aisraeli. Dziko silingalekerere zonena zake zonsezo.
11 For thus hath Amos said: Jeroboam shall die by the sword, And Israel shall surely be led captive from their own land.
Pakuti zimene Amosi akunena ndi izi: “‘Yeroboamu adzaphedwa ndi lupanga, ndipo Israeli adzapita ndithu ku ukapolo, kutali ndi dziko lake.’”
12 And Amaziah said to Amos, Go, thou seer! flee into the land of Judah! There eat thy bread, and there prophesy!
Ndipo Amaziya anawuza Amosi kuti, “Choka, mlosi iwe! Bwerera ku dziko la Yuda. Uzikalosera kumeneko ndipo anthu a kumeneko azikakudyetsa.
13 But prophesy no more at Bethel, For it is the king's sanctuary, And it is the king's abode.
Usanenerenso ku Beteli, chifukwa kumeneko ndi malo opatulika a mfumu ndiponso ndi malo a nyumba yachipembedzo yaufumu.”
14 Then answered Amos, and said to Amaziah: I was no prophet, nor the son of a prophet; I was a shepherd, and a gatherer of sycamore fruit.
Amosi anayankha Amaziya kuti, “Ine sindine mneneri kapena mwana wa mneneri; koma ndine woweta ziweto, ndiponso mlimi wa nkhuyu.
15 And Jehovah took me from the flock; And Jehovah said to me, Go, prophesy to my people Israel!
Koma Yehova ananditenga ndikuweta nkhosa ndipo anati, ‘Pita ukanenere kwa anthu anga Aisraeli.’
16 Now, therefore, hear the word of Jehovah: Thou sayest, Prophesy not against Israel, And speak no word against the house of Isaac!
Tsono imva mawu a Yehova. Iwe ukunena kuti, “‘Usanenere zotsutsa Israeli, ndipo siya kulalikira motsutsa nyumba ya Isake.’”
17 Therefore thus saith Jehovah: “Thy wife shall be put to shame in the city, And thy sons and daughters shall fall by the sword; Thy land shall be divided by the line, And thou shalt die in a polluted land, And Israel shall surely be led captive from his own land.”
“Tsono zimene akunena Yehova ndi izi: “‘Mkazi wako adzasanduka wachiwerewere mu mzindamu, ndipo ana ako aamuna ndi aakazi adzaphedwa ndi lupanga. Munda wako udzayezedwa ndi chingwe ndi kugawidwa, ndipo iwe mwini udzafera mʼdziko la anthu osapembedza Mulungu. Ndipo Israeli adzatengedwa ndithu kupita ku ukapolo, kutali ndi dziko lake.’”

< Amos 7 >