< Amos 2 >

1 Thus saith Jehovah: For three transgressions of Moab, And for four, will I not turn away his punishment; For he burned the bones of the king of Edom into lime!
Yehova akuti, “Chifukwa anthu a ku Mowabu akunka nachimwirachimwira, Ine sindileka kuwalanga. Popeza anatentha mafupa a mfumu ya ku Edomu, mpaka kuwasandutsa phulusa,
2 But I will send a fire on Moab, Which shall devour the palaces of Kirioth; And Moab shall die amid tumults, Amid the war-shout, and the sound of the trumpet.
Ine ndidzatumiza moto pa Mowabu, umene udzanyeketsa nyumba zaufumu za ku Keriyoti. Mowabu adzafera pakati pa nkhondo yoopsa, mʼkati mwa mfuwu wa nkhondo ndi kuliza malipenga.
3 I will destroy the judge from the midst of him, And slay all the princes with him, saith Jehovah.
Ndidzawononga wolamulira wake ndi kupha akuluakulu onse amene ali pamodzi ndi iye,” akutero Yehova.
4 Thus saith Jehovah: For three transgressions of Judah, And for four, will I not turn away their punishment; For they have despised the law of Jehovah, And have not kept his statutes, And their idols have caused them to err, After which their fathers walked.
Yehova akuti, “Chifukwa anthu a ku Yuda akunka nachimwirachimwira, Ine sindileka kuwalanga. Popeza iwo akana lamulo la Yehova ndipo sanasunge malangizo ake, popeza asocheretsedwa ndi milungu yabodza, milungu imene makolo awo ankayitsatira,
5 But I will send a fire upon Judah, Which shall devour the palaces of Jerusalem.
Ine ndidzatumiza moto pa Yuda, umene udzanyeketsa nyumba zaufumu za ku Yerusalemu.”
6 Thus saith Jehovah: For three transgressions of Israel, And for four, will I not turn away their punishment. For they sell the righteous for silver, And the needy for a pair of shoes;
Yehova akuti, “Chifukwa anthu a ku Israeli akunka nachimwirachimwira, Ine sindileka kuwalanga. Iwo amagulitsa anthu olungama ndi siliva, ndi osauka ndi nsapato.
7 They pant for the dust of the earth on the head of the poor, And pervert the cause of the afflicted. The son and the father go in to the same damsel, To dishonor my holy name.
Amapondereza anthu osauka ngati akuponda fumbi, ndipo sawaweruza mwachilungamo anthu oponderezedwa. Abambo ndi mwana wawo amagonana ndi mtsikana mmodzi yemweyo, ndipo potero amanyozetsa dzina langa loyera.
8 They lay themselves down upon pledged garments Near every altar; And drink wine, procured by fines, In the house of their gods.
Anthuwo amakagonana mʼmbali mwa guwa lililonse la nsembe pa zovala zimene anatenga ngati chikole. Mʼnyumba ya mulungu wawo amamweramo vinyo amene analipiritsa anthu pa milandu.
9 Yet I destroyed the Amorites before them, Who were tall as the cedars, And strong as the oaks. I destroyed their fruit above, And their roots beneath.
“Ine ndinawononga Aamori pamaso pawo, ngakhale iwo anali anthu ataliatali ngati mikungudza ndiponso amphamvu ngati mitengo ya thundu. Ndinawononga zipatso zawo ndiponso mizu yawo.
10 I brought you up from the land of Egypt, And led you in the desert forty years, That ye might possess the land of the Amorite.
“Ine ndinakutulutsani ku Igupto, ndipo ndinakutsogolerani mʼchipululu kwa zaka makumi anayi, kudzakupatsani dziko la Aamori.
11 Of your sons also I raised up prophets, And of your young men Nazarites; Is it not even so, O ye sons of Israel? saith Jehovah.
Ine ndinawutsanso ena mwa ana ako kuti akhale aneneri, ndi ena mwa anyamata ako kuti akhale anaziri. Kodi si choncho, inu Aisraeli?” akutero Yehova.
12 But ye gave the Nazarites wine to drink, And commanded the prophets, Saying, Prophesy not!
“Koma inu munawamwetsa vinyo anaziri aja, ndipo munalamula aneneri kuti asanenere.
13 Behold, I will press you down, As a wagon presseth down that is full of sheaves.
“Tsono Ine ndidzakupsinjani monga imapsinjikira ngolo imene yadzaza ndi tirigu.
14 And flight shall fail the swift, And the strong shall not exert his strength, And the mighty shall not save his life,
Munthu waliwiro sadzatha kuthawa, munthu wamphamvu sadzakhalanso ndi nyonga, wankhondo sadzapulumutsa moyo wake.
15 And he that handleth the bow shall not stand, And the swift of foot shall not save himself, And the horseman shall not escape with his life.
Munthu wa uta sadzalimbika, msilikali wothamanga kwambiri sadzapulumuka, ndipo wokwera pa akavalo sadzapulumutsa moyo wake.
16 He that is strong in heart among the mighty Shall, in that day, flee away naked, saith Jehovah.
Ngakhale asilikali olimba mtima kwambiri adzathawa ali maliseche pa tsikulo,” akutero Yehova.

< Amos 2 >