< 2 John 1 >

1 The elder to the elect Cyria, and to her children, whom I love in truth, and not I only, but also all that know the truth, —
Ndine mkulu wampingo, kulembera: Mayi wosankhidwa ndi Mulungu ndi kwa ana ake amene ndimawakonda mʼchoonadi. Ndipo sindine ndekha amene ndimawakonda, komanso onse odziwa choonadi.
2 for the sake of the truth which abideth in us, and will be with us for ever. (aiōn g165)
Timakukondani chifukwa cha choonadi chimene chimakhala mwa ife ndipo chidzakhala mwa ife mpaka muyaya. (aiōn g165)
3 Grace, mercy, peace shall be with you from God the Father, and from Jesus Christ, the Son of the Father, in truth and love.
Chisomo, chifundo ndi mtendere zochokera kwa Mulungu Atate ndi kwa Yesu Khristu, Mwana wa Atate, zikhale ndi ife mʼchoonadi ndi mʼchikondi.
4 I rejoiced greatly, that I found some of thy children walking in truth, as we received commandment from the Father.
Ndinakondwera kwambiri nditapeza ana anu ena akuyenda mʼchoonadi, monga Atate anatilamulira.
5 And now I beseech thee, Cyria, not as writing to thee a new commandment, but that which we have had from the beginning, that we love one another.
Ndipo tsopano, amayi wokondedwa, sindikukulemberani lamulo latsopano koma lomwe lija takhala nalo kuyambira pachiyambi. Ine ndikukupemphani kuti tidzikondana wina ndi mnzake.
6 And this is love, that we walk according to his commandments. This is the commandment, as ye have heard from the beginning, that ye should walk in it.
Ndipo chikondi ndiye kuyenda momvera malamulo ake. Lamulo lake ndi lakuti mukhale moyo wachikondi monga munamva kuyambira pachiyambi.
7 For many deceivers went out into the world, who do not acknowledge Jesus Christ coming in the flesh; this is the deceiver and the antichrist.
Ndikunena zimenezi chifukwa anthu ambiri onyenga, amene savomereza kuti Yesu Khristu anabwera monga munthu, akuyenda mʼdziko lapansi. Munthu aliyense otere ndi wonyenga ndiponso wokana Khristu.
8 Look to yourselves, that ye lose not the things which ye wrought, but receive a full reward.
Chenjerani kuti mungataye chimene mwagwirira ntchito, koma chitani khama kuti mukalandire mphotho yanu yonse.
9 Whoever goeth beyond, and abideth not in the teaching of Christ, hath not God. He that abideth in the teaching, he hath both the Son and the Father.
Aliyense amene sasunga chiphunzitso cha Khristu, alibe Mulungu. Koma amene amasunga chiphunzitsochi, ameneyo alinso ndi Atate ndi Mwana.
10 If any one cometh to you, and bringeth not this teaching, receive him not into your house, and do not bid him good speed.
Ngati wina aliyense abwera kwa inu osaphunzitsa zimenezi, musamulandire mʼnyumba mwanu kapena kumupatsa moni.
11 For he that biddeth him good speed taketh part in his evil deeds.
Aliyense wolandira munthu wotere ndiye kuti akuvomerezana nazo ntchito zake zoyipa.
12 Having many things to write to you, I would not write with paper and ink; but I hope to come to you, and to speak face to face, that our joy may be full.
Ndili nazo zambiri zoti ndikulembereni, koma sindikufuna kuzilemba mʼkalata. Mʼmalo mwake, ndikuyembekeza kufika kwanuko kuti tidzakambirane nanu pamaso ndi pamaso, potero chimwemwe chathu chidzakhala chathunthu.
13 The children of thy elect sister salute thee.
Ana a mlongo wanu wosankhidwa ndi Mulungu akupereka moni.

< 2 John 1 >