< Zephaniah 1 >

1 The word of YHWH which came to Zephaniah, the son of Cushi, the son of Gedaliah, the son of Amariah, the son of Hezekiah, in the days of Josiah, the son of Amon, king of Judah.
Yehova anayankhula ndi Zefaniya mwana wa Kusi, mwana wa Gedaliya, mwana wa Amariya, mwana wa Hezekiya pa nthawi ya Yosiya, mwana wa Amoni, mfumu ya Yuda.
2 I will utterly sweep away everything off of the surface of the earth, says YHWH.
“Ndidzawononga kotheratu zinthu zonse pa dziko lapansi,” akutero Yehova.
3 I will sweep away people and animals. I will sweep away the birds of the sky, and the fish of the sea, and the idols that cause the wicked to stumble. I will remove humankind from the surface of the earth, says YHWH.
“Ndidzawononga anthu pamodzi ndi nyama zomwe; ndidzawononga mbalame zamlengalenga ndi nsomba za mʼnyanja. Ndidzawononga anthu oyipa, ndipo ndidzafafaniza mtundu wa anthu pa dziko lonse lapansi,” akutero Yehova.
4 I will stretch out my hand against Judah, and against all the inhabitants of Jerusalem. I will cut off the remnant of Baal from this place, the name of the idolatrous priests along with the priests,
Ndidzatambasula dzanja langa pa Yuda ndi onse okhala mu Yerusalemu. Ndidzawononga pamalo pano otsalira opembedza Baala, mayina a anthu osapembedza pamodzi ndi ansembe a mafano:
5 those who worship the host of heaven on the housetops, those who worship and swear by YHWH and also swear by Milcom,
amene amagwada pa madenga a nyumba zawo kupembedza zolengedwa zamumlengalenga, amene amagwada ndi kulumbira mʼdzina la Yehova, komanso mʼdzina la Moleki,
6 those who have turned back from following YHWH, and those who haven't sought YHWH nor inquired after him.
amene abwerera mʼmbuyo osatsata Yehova, osafunafuna kapena kupempha nzeru kwa Yehova.
7 Be silent at the presence of YHWH, for the day of YHWH is at hand. For YHWH has prepared a sacrifice. He has consecrated his guests.
Khalani chete pamaso pa Ambuye Yehova, chifukwa tsiku la Yehova layandikira. Yehova wakonzekera kupereka nsembe; wapatula iwo amene wawayitana.
8 It will happen in the day of YHWH's sacrifice that I will punish the princes, the king's sons, and all those who are clothed with foreign attire.
Pa tsiku la nsembe ya Yehova ndidzalanga akalonga ndi ana aamuna a mfumu ndi onse amene amavala zovala zachilendo.
9 In that day, I will punish all those who leap over the threshold, who fill their master's house with violence and deceit.
Pa tsiku limenelo ndidzalanga onse amene safuna kuponda pa chiwundo, amene amadzaza nyumba ya ambuye awo ndi chiwawa ndi chinyengo.
10 On that day, says YHWH, there will be the noise of a cry from the Fish Gate, a wailing from the Second Quarter, and a loud crash from the hills.
“Pa tsiku limenelo,” akutero Yehova, “Kufuwula kwakukulu kudzamveka pa Chipata cha Nsomba, kulira kwa chisoni kuchokera mʼChigawo Chatsopano, ndi phokoso la kugumuka kochokera ku mapiri.
11 Wail, you inhabitants of the market district, for all the merchants will be destroyed, and all those who weigh out silver will be removed.
Lirani mwachisoni, inu amene mumakhala kumene kuli msika; a malonda anu onse adzapululidwa, ndiponso onse amene ali ndi siliva adzawonongedwa.
12 It will happen at that time that I will search Jerusalem with lamps, and I will punish the people who are complacent, who say in their heart, "YHWH will not do good, nor will he do harm."
Pa nthawi imeneyo ndidzafufuzafufuza mu Yerusalemu ndi nyale ndi kulanga onse amene sakulabadira, amene ali ngati vinyo wosakhutchumulidwa, amene amaganiza kuti, ‘Yehova sadzachita chilichonse, chabwino kaya choyipa.’
13 Their wealth will be looted and their houses a desolation. Yes, they will build houses, but won't inhabit them. They will plant vineyards, but won't drink their wine.
Chuma chawo chidzafunkhidwa, nyumba zawo zidzagwetsedwa. Adzamanga nyumba, koma osakhalamo; adzadzala minda ya mpesa koma sadzamwako vinyo wake.”
14 The great day of YHWH is near. Near and approaching very rapidly. The cry on the day of YHWH is bitter. In it the warrior shouts his battle cry.
Tsiku lalikulu la Yehova layandikira, layandikira ndipo lifika msanga. Tamverani! Kulira kwa pa tsiku la Yehova kudzakhala kowawa, ngakhale munthu wolimba mtima adzalira kwambiri.
15 That day is a day of wrath, a day of distress and anguish, a day of devastation and ruin, a day of clouds and thick darkness,
Tsiku limenelo lidzakhala la ukali, tsiku losautsa ndi lomvetsa chisoni, tsiku la mavuto ndi la chiwonongeko, tsiku la mdima ndi lachisoni, tsiku la mitambo ndi la mdima wandiweyani.
16 a day of the trumpet and battle cry against the fortified cities, and against the high corner towers.
Tsiku loliza lipenga ndi la mfuwu wankhondo, tsiku la kugwa kwa mizinda yotetezedwa ndi nsanja za pa ngodya.
17 I will bring distress on the people, that they will walk like blind men, because they have sinned against YHWH, and their blood will be poured out like dust, and their flesh like dung.
Ndidzabweretsa msautso pa anthu ndipo adzayenda ngati anthu osaona, chifukwa achimwira Yehova, magazi awo adzamwazika ngati fumbi ndi mnofu wawo ngati ndowe.
18 Neither their silver nor their gold will be able to deliver them in the day of YHWH's wrath, but the whole land will be devoured by the fire of his jealousy; for he will bring terrifying destruction on all the inhabitants of the land.
Ngakhale siliva wawo kapena golide wawo sadzatha kuwapulumutsa pa tsiku la ukali wa Yehova. Dziko lonse lapansi lidzanyeka mʼmoto wa nsanje yake chifukwa adzakantha modzidzimutsa onse okhala pa dziko lapansi.

< Zephaniah 1 >