< Psalms 96 >

1 Sing to YHWH a new song. Sing to YHWH, all the earth.
Imbirani Yehova nyimbo yatsopano; Imbirani Yehova dziko lonse lapansi.
2 Sing to YHWH. Bless his name. Proclaim his salvation from day to day.
Imbirani Yehova, tamandani dzina lake; lalikirani chipulumutso chake tsiku ndi tsiku.
3 Declare his glory among the nations, his marvelous works among all the peoples.
Lengezani ulemerero wake pakati pa mayiko, ntchito zake zodabwitsa pakati pa mitundu yonse ya anthu.
4 For great is YHWH, and greatly to be praised. He is to be feared above all gods.
Pakuti wamkulu ndi Yehova ndipo ndi woyenera kwambiri kumutamanda; ayenera kuopedwa kupambana milungu yonse.
5 For all the gods of the peoples are idols, but YHWH made the heavens.
Pakuti milungu yonse ya anthu a mitundu ina ndi mafano, koma Yehova analenga mayiko akumwamba.
6 Honor and majesty are before him. Strength and beauty are in his sanctuary.
Ulemu ndi ufumu zili pamaso pake, mphamvu ndi ulemerero zili mʼmalo ake opatulika.
7 Ascribe to YHWH, you families of nations, ascribe to YHWH glory and strength.
Perekani kwa Yehova, inu mabanja a anthu a mitundu ina, perekani kwa Yehova ulemerero ndi mphamvu.
8 Ascribe to YHWH the glory due to his name. Bring an offering, and come into his courts.
Perekani kwa Yehova ulemerero woyenera dzina lake; bweretsani chopereka ndipo mulowe mʼmabwalo ake.
9 Worship YHWH in holy array. Tremble before him, all the earth.
Lambirani Yehova mu ulemerero wa chiyero chake; njenjemerani pamaso pake, dziko lonse lapansi.
10 Say among the nations, "YHWH reigns." The world is also established. It can't be moved. He will judge the peoples with equity.
Nenani pakati pa mitundu ya anthu, “Yehova akulamulira.” Dziko lonse lakhazikika molimba, silingasunthidwe; Iye adzaweruza mitundu ya anthu molungama.
11 Let the heavens be glad, and let the earth rejoice. Let the sea roar, and its fullness.
Mayiko akumwamba asangalale, dziko lapansi likondwere; nyanja ikokome, ndi zonse zili mʼmenemo;
12 Let the field and all that is in it exult. Then all the trees of the woods shall sing for joy
minda ikondwere pamodzi ndi chilichonse chili mʼmenemo. Pamenepo mitengo yonse ya mʼnkhalango idzayimba ndi chimwemwe;
13 before YHWH; for he comes, for he comes to judge the earth. He will judge the world with righteousness, the peoples with his truth.
idzayimba pamaso pa Yehova, pakuti Iye akubwera kudzaweruza dziko lapansi; adzaweruza dziko lonse mwachilungamo ndi mitundu ya anthu onse mʼchoonadi.

< Psalms 96 >