< Psalms 83 >

1 [A song. A Psalm by Asaph.] God, do not be silent. Do not be deaf, and do not be inactive, God.
Nyimbo. Salimo la Asafu. Inu Mulungu musakhale chete; musangoti phee, Mulungu musangoti duu.
2 For, look, your enemies make an uproar. Those who hate you are hostile.
Onani adani anu akuchita chiwawa, amene amadana nanu autsa mitu yawo.
3 They devise crafty plans against your people, and conspire together against your treasured ones.
Mochenjera iwo akukambirana za chiwembu kutsutsana ndi anthu anu; Iwo akukonzekera kutsutsana ndi omwe mumawakonda.
4 They say, "Come, and let us annihilate them as a nation; let the name of Israel may be remembered no more."
Iwo akunena kuti, “Bwerani” akutero, “Tiyeni tiwononge mtundu wonsewu kuti dzina la Israeli lisakumbukikenso.”
5 For they plot a unified strategy; they make a covenant against you;
Ndi mtima umodzi akukonzekera chiwembu; Iwo achita mgwirizano kutsutsana nanu:
6 the tents of Edom and the Ishmaelites, Moab, and the Hagrites,
Matenti a Edomu ndi Aismaeli, Mowabu ndi Ahagiri,
7 Gebal, Ammon, and Amalek, Philistia with the inhabitants of Tyre.
Agebala, Aamoni ndi Aamaleki, Afilisti, pamodzi ndi anthu a ku Turo.
8 Assyria too is joined with them; they lend support to the descendants of Lot. (Selah)
Ngakhalenso Aasiriya aphatikizana nawo kupereka mphamvu kwa ana a Loti. (Sela)
9 Do to them as you did to Midian, as to Sisera, as to Jabin at the Kishon River,
Muwachitire zomwe munachitira Amidiyani, monga munachitira Sisera ndi Yabini ku mtsinje wa Kisoni.
10 who were destroyed at Endor, who became manure for the ground.
Amene anawonongedwa ku Endori ndi kukhala ngati zinyalala.
11 Make their nobles like Oreb and Zeeb, all their princes like Zebah and Zalmunna,
Anthu awo otchuka muwachite zomwe munachita Orebu ndi Zeebu ana a mafumu muwachite zomwe munachita Zeba ndi Zalimuna,
12 who said, "Let us take possession for ourselves the pastures of God."
amene anati, “Tiyeni tilande dziko la msipu la Mulungu.”
13 My God, make them like tumbleweed; like dead weeds blown by the wind.
Muwasandutse fumbi lowuluka, Inu Mulungu wanga, ngati mankhusu owuluka ndi mphepo.
14 Like a fire that consumes a forest, and like the flames that consume the mountains,
Monga moto umatentha nkhalango, kapena malawi a moto kuyatsa phiri,
15 so pursue them with your gale winds, and terrify them with your storm.
kotero muwathamangitse ndi mphepo yamkuntho, ndi kuwachititsa mantha ndi namondwe.
16 Cover their faces with shame, so that they might seek your name, YHWH.
Muphimbe nkhope zawo ndi manyazi kuti adzafunefune dzina lanu Yehova.
17 Let them be put to shame and terrified forever; let them perish in disgrace,
Achite manyazi ndi mantha nthawi zonse; awonongeke mwa manyazi.
18 that they will know that you alone, whose name is YHWH, are the Most High over all the earth.
Adziwe kuti Inu amene dzina lanu ndi Yehova, ndinu nokha Wammwambamwamba pa dziko lonse lapansi.

< Psalms 83 >