< Psalms 80 >

1 [For the Chief Musician. To the tune of "The Lilies of the Covenant." A Psalm by Asaph.] Hear us, Shepherd of Israel, you who lead Joseph like a flock, you who sit above the cherubim, shine forth.
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Potsata mayimbidwe a “Kakombo wa Pangano.” Salimo la Asafu. Tcherani khutu Inu mʼbusa wa Israeli, Inu amene mumatsogolera Yosefe monga nkhosa; Inu amene mumakhala pa mpando waufumu pakati pa akerubi, walani
2 Before Ephraim and Benjamin and Manasseh, stir up your might. Come to save us.
kwa Efereimu, Benjamini ndi Manase. Utsani mphamvu yanu; bwerani ndi kutipulumutsa.
3 Restore us, God. Cause your face to shine, and we will be saved.
Tibwezereni mwakale Inu Mulungu; nkhope yanu itiwalire kuti tipulumutsidwe.
4 YHWH, the God of hosts, How long will you be angry against the prayer of your people?
Inu Mulungu Wamphamvuzonse, mpaka liti mkwiyo wanu udzanyeka kutsutsana ndi mapemphero a anthu anu?
5 You have fed them with the bread of tears, and given them tears to drink in large measure.
Mwawadyetsa buledi wa misozi; mwachitisa iwo kumwa misozi yodzaza mbale.
6 You make us a source of contention to our neighbors. Our enemies have mocked us.
Mwachititsa kuti tikhale gwero la mikangano pakati pa anansi athu, ndipo adani athu akutinyoza.
7 Restore us, God of hosts. Cause your face to shine, and we will be saved.
Tibwezereni mwakale Inu Mulungu Wamphamvuzonse, nkhope yanu itiwalire kuti tipulumutsidwe.
8 You brought a vine out of Egypt. You drove out the nations, and planted it.
Munatulutsa mpesa kuchoka ku Igupto; munathamangitsa anthu a mitundu ina ndi kuwudzala mpesawo.
9 You cleared the ground for it. It took deep root, and filled the land.
Munawulimira munda wamphesawo, ndipo unamera ndi kudzaza dziko.
10 The mountains were covered with its shadow. Its boughs were like God's cedars.
Mapiri anaphimbidwa ndi mthunzi wake, mikungudza yamphamvu ndi nthambi zake.
11 It sent out its branches to the sea, Its shoots to the River.
Unatambalitsa nthambi zake mpaka ku nyanja, mphukira zake mpaka ku mtsinje.
12 Why have you broken down its walls, so that all those who pass by the way pluck it?
Chifukwa chiyani mwagwetsa makoma ake kuti onse amene akudutsa athyole mphesa zake?
13 The boar out of the wood ravages it. The wild animals of the field feed on it.
Nguluwe zochokera mʼnkhalango zikuwononga ndipo zirombo za mthengo zimawudya.
14 Return, we beg you, God of hosts. Look down from heaven, and see, and visit this vine,
Bweraninso kwa ife Inu Mulungu Wamphamvuzonse! Yangʼanani pansi muli kumwambako ndipo muone! Uyangʼanireni mpesa umenewu,
15 the stock which your right hand planted, the branch that you made strong for yourself.
muzu umene dzanja lanu lamanja ladzala, mwana amene inu munamukuza nokha.
16 It's burned with fire. It's cut down. They perish at your rebuke.
Mpesa wanu wadulidwa ndi kutenthedwa ndi moto; pakudzudzula kwanu anthu anu awonongeka.
17 Let your hand be on the man of your right hand, on the son of man whom you made strong for yourself.
Dzanja lanu likhale pa munthu amene ali ku dzanja lanu lamanja, mwana wa munthu amene mwalera nokha.
18 So we will not turn away from you. Revive us, and we will call on your name.
Ndipo ife sitidzatembenukira kumbali kuchoka kwa Inu; titsitsimutseni ndipo tidzayitana pa dzina lanu.
19 Restore us, YHWH, the God of hosts. Cause your face to shine, and we will be saved.
Tibwezereni mwakale Inu Yehova Mulungu Wamphamvuzonse nkhope yanu itiwalire kuti tipulumutsidwe.

< Psalms 80 >