< Psalms 56 >

1 [For the Chief Musician. To the tune of "Silent Dove in Distant Lands." A poem by David, when the Philistines seized him in Gath.] Be merciful to me, God, for man wants to swallow me up. All day long, he attacks and oppresses me.
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Potsata mayimbidwe a “Njiwa pa Mtengo wa Thundu wa Kutali.” Mikitamu ya Davide, pamene Afilisti anamugwira ku Gati. Mundichitire chifundo Inu Mulungu, pakuti anthu akundithamangitsa kwambiri; tsiku lonse akundithira nkhondo.
2 My enemies want to swallow me up all day long, for they are many who fight proudly against me.
Ondinyoza akundithamangitsa tsiku lonse, ambiri akumenyana nane monyada.
3 When I am afraid, I will put my trust in you.
Ndikachita mantha ndimadalira Inu.
4 In God, I praise his word. In God, I put my trust. I will not be afraid. What can flesh do to me?
Mwa Mulungu, amene mawu ake ine ndimatamanda, mwa Mulungu ine ndimadaliramo; sindidzachita mantha. Kodi munthu amene amafa angandichite chiyani?
5 All day long they twist my words. All their thoughts are against me for evil.
Tsiku lonse amatembenuza mawu anga; nthawi zonse amakonza zondivulaza.
6 They conspire and lurk, watching my steps, they are eager to take my life.
Iwo amakambirana, amandibisalira, amayangʼanitsitsa mayendedwe anga ndipo amakhala ndi chidwi chofuna kuchotsa moyo wanga.
7 Shall they escape by iniquity? In anger cast down the peoples, God.
Musalole konse kuti athawe; mu mkwiyo wanu Mulungu mugwetse mitundu ya anthu.
8 You number my wanderings. You put my tears into your bottle. Aren't they in your book?
Mulembe za kulira kwanga, mulembe chiwerengero cha misozi yanga mʼbuku lanu. Kodi zimenezi sizinalembedwe mʼbuku lanulo?
9 Then my enemies shall turn back in the day that I call. I know this, that God is for me.
Adani anga adzabwerera mʼmbuyo pamene ndidzalirira kwa Inu. Pamenepo ndidzadziwa kuti Mulungu ali ku mbali yanga.
10 In God, I will praise his word. In YHWH, I will praise his word.
Mwa Mulungu amene mawu ake ndimawatamanda, mwa Yehova amene mawu ake ndimawatamanda,
11 I have put my trust in God. I will not be afraid. What can man do to me?
mwa Mulungu ine ndimadalira ndipo sindidzachita mantha. Kodi munthu angandichite chiyani?
12 Your vows are on me, God. I will give thank offerings to you.
Ndiyenera kuchita zomwe ndinalumbira kwa Mulungu; ndidzapereka nsembe zanga zachiyamiko kwa inu.
13 For you have delivered my soul from death, and prevented my feet from falling, that I may walk before God in the light of the living.
Pakuti mwawombola moyo wanga ku imfa ndi mapazi anga kuti ndingagwe, kuti ndiyende pamaso pa Mulungu mʼkuwala kwa moyo.

< Psalms 56 >