< Psalms 54 >

1 [For the Chief Musician. On stringed instruments. A contemplation by David, when the Ziphites came and said to Saul, "Isn't David hiding himself among us?"] Save me, God, by your name. Vindicate me in your might.
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Pa zoyimbira za zingwe. Ndakatulo ya Davide. Pamene anthu a ku Zifi anapita kwa Sauli ndipo anati, “Kodi Davide sakubisala pakati pathu.” Pulumutseni Inu Mulungu, mwa dzina lanu; onetsani kuti ndine wosalakwa mwamphamvu yanu.
2 Hear my prayer, God. Listen to the words of my mouth.
Imvani pemphero langa, Inu Mulungu mvetserani mawu a pakamwa panga.
3 For strangers have risen up against me. Violent men have sought after my soul. They haven't set God before them. (Selah)
Alendo akundithira nkhondo; anthu ankhanza akufunafuna moyo wanga, anthu amene salabadira za Mulungu.
4 Look, God is my helper. YHWH is the one who sustains my soul.
Zoonadi Mulungu ndi thandizo langa; Ambuye ndiye amene amandichirikiza ine.
5 He will repay the evil to my enemies. Destroy them in your truth.
Lolani kuti choyipa chifike pa iwo amene amandichita chipongwe; mwa kukhulupirika kwanu awonongeni.
6 With a free will offering, I will sacrifice to you. I will give thanks to your name, YHWH, for it is good.
Ine ndidzapereka nsembe yaufulu kwa Inu; ndidzatamanda dzina lanu, Inu Yehova, pakuti ndi labwino.
7 For he has delivered me out of all trouble. My eye has seen triumph over my enemies.
Pakuti Iyeyo wandipulumutsa ku masautso anga onse, ndipo maso anga apenya kupambana kwa pa adani anga.

< Psalms 54 >