< Psalms 53 >

1 [For the Chief Musician. To the tune of "Mahalath." A contemplation by David.] The fool has said in his heart, "There is no God." They are corrupt, and have done abominable iniquity. There is no one who does good.
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Potsata mayimbidwe a Mahalati. Ndakatulo ya Davide. Chitsiru chimati mu mtima mwake, “Kulibe Mulungu.” Iwo ndi oyipa ndipo njira zawo ndi zonyansa; palibe ndi mmodzi yemwe amene amachita chabwino.
2 God looks down from heaven on the descendants of Adam, to see if there are any who are wise, who seek after God.
Mulungu kumwamba amayangʼana pansi pano pa ana a anthu kuti aone ngati alipo wina wanzeru, wofunafuna Mulungu.
3 Every one of them has gone back. They have become filthy together. There is no one who does good, no, not one.
Aliyense wabwerera, iwo onse pamodzi akhala oyipa; palibe ndi mmodzi yemwe amene amachita chabwino, ngakhale mmodzi.
4 Have evildoers no knowledge, who eat up my people as they eat bread, and do not call on God?
Kodi anthu ochita zoyipawa adzaphunziradi; anthu amene amadya anthu anga monga mmene anthu amadyera buledi, ndipo sapemphera kwa Mulungu?
5 There they will be in great fear, where no fear had been, for God will scatter the bones of those who encamp against you. You will put them to shame, because God has rejected them.
Iwo anali pamenepo atathedwa nzeru ndi mantha aakulu pamene panalibe kanthu kochititsa mantha. Mulungu anamwazamwaza mafupa a anthu amene anakuthirani nkhondo; inuyo munawachititsa manyazi, pakuti Mulungu anawanyoza.
6 Oh that the salvation of Israel would come out of Zion. When God brings back his people from captivity, may Jacob rejoice, may Israel be glad.
Ndithu, chipulumutso cha Israeli nʼchochokera ku Ziyoni! Pamene Mulungu adzabwezeretsanso ulemerero wa anthu ake, lolani Yakobo akondwere ndi Israeli asangalale!

< Psalms 53 >