< Psalms 23 >

1 [A Psalm by David.] YHWH is my shepherd; I will not lack.
Salimo la Davide. Yehova ndiye mʼbusa wanga, sindidzasowa kanthu.
2 He makes me lie down in green pastures. He leads me beside still waters.
Amandigoneka pa msipu wobiriwira, amanditsogolera ku madzi akumwa abwino,
3 He restores my soul. He guides me in the paths of righteousness for his name's sake.
amatsitsimutsa moyo wanga. Amanditsogolera mʼnjira zachilungamo chifukwa cha dzina lake.
4 Even though I walk through the valley of the shadow of death, I will fear no evil, for you are with me. Your rod and your staff, they comfort me.
Ngakhale ndiyende mʼchigwa cha mdima wakuda bii, sindidzaopa choyipa, pakuti Inu muli ndi ine; chibonga chanu ndi ndodo yanu zimanditonthoza.
5 You prepare a table before me in the presence of my enemies. You anoint my head with oil. My cup overflows.
Mumandikonzera chakudya adani anga akuona. Mumadzoza mutu wanga ndi mafuta; chikho changa chimasefukira.
6 Surely goodness and loving kindness shall follow me all the days of my life, and I will dwell in YHWH's house forever.
Zoonadi, zokoma ndi chikondi chosasinthika zidzanditsata masiku onse a moyo wanga, ndipo ndidzakhala mʼNyumba ya Yehova kwamuyaya.

< Psalms 23 >