< Psalms 2 >

1 Why do the nations rage, and the peoples plot in vain?
Nʼchifukwa chiyani anthu a mitundu ina akufuna kuchita chiwembu? Akonzekeranji zopanda pake anthu?
2 The kings of the earth take a stand, and the rulers take counsel together, against YHWH, and against his Anointed:
Mafumu a dziko lapansi akugwirizana nazo; ndipo olamulira asonkhana pamodzi kulimbana ndi Ambuye ndi wodzozedwa wakeyo.
3 "Let's tear off their shackles, and throw off their ropes from us."
Iwo akunena kuti, “Tiyeni timasule magoli awo ndipo titaye zingwe zawo.”
4 The one who sits in the heavens laughs. YHWH scoffs at them.
Wokhala mmwamba akuseka; Ambuye akuwanyoza iwowo.
5 Then he will speak to them in his anger, and terrify them in his wrath:
Ndipo iye awadzudzula mu mkwiyo wake ndi kuwaopseza mu ukali wake, kunena kuti,
6 "But I myself have installed my king on Zion, my holy mountain."
“Ine ndakhazikitsa mfumu yanga pa Ziyoni, phiri langa loyera.”
7 I will tell of the decree. YHWH said to me, "You are my son. Today I have become your father.
Ine ndidzalengeza zimene Yehova walamula: Iye anati kwa Ine, “Iwe ndiwe mwana wanga; lero Ine ndakhala Atate ako.
8 Ask of me, and I will give the nations as your inheritance, and the farthest parts of the earth for your possession.
Tandipempha, ndipo ndidzachititsa kuti mitundu ya anthu ikhale cholowa chako; malekezero a dziko lapansi kuti akhale chuma chako.
9 You shall rule them with an iron scepter. You shall dash them in pieces like a potter's vessel."
Iweyo udzawalamulira ndi ndodo yaufumu yachitsulo; udzawaphwanya zidutswazidutswa ngati zowumba zadothi.”
10 Now therefore, you kings, be wise; receive correction, you judges of the earth.
Kotero, inu mafumu, chenjerani; chenjezedwani, inu olamulira a dziko lapansi.
11 Serve YHWH with fear, and rejoice with trembling.
Tumikirani Yehova mwa mantha ndi kukondwerera ulamuliro wake monjenjemera.
12 Do homage in purity, lest he be angry, and you perish in the way, when his anger is suddenly kindled. Blessed are all those who take refuge in him.
Mpsopsoneni mwanayo kuti angakwiye; kuti mungawonongedwe mʼnjira zanu, pakuti ukali wake utha kuuka mʼkanthawi kochepa. Odala ndi onse amene amathawira kwa Iye.

< Psalms 2 >