< Psalms 141 >

1 [A Psalm by David.] YHWH, I have called on you. Come to me quickly. Listen to my voice when I call to you.
Salimo la Davide. Inu Yehova ndikukuyitanani; bwerani msanga kwa ine. Imvani mawu anga pamene ndiyitana Inu.
2 Let my prayer be set before you like incense; the lifting up of my hands like the evening sacrifice.
Pemphero langa lifike kwa Inu ngati lubani; kukweza manja kwanga kukhale ngati nsembe yamadzulo.
3 Set a watch, YHWH, before my mouth. Keep the door of my lips.
Yehova ikani mlonda pakamwa panga; londerani khomo la pa milomo yanga.
4 Do not incline my heart to any evil thing, to practice deeds of wickedness with men who work iniquity. Do not let me eat of their delicacies.
Musalole kuti mtima wanga ukokedwere ku zoyipa; kuchita ntchito zonyansa pamodzi ndi anthu amene amachita zoyipa; musalole kuti ndidye nawo zokoma zawo.
5 Let the righteous strike me, it is kindness; let him reprove me, it is like oil on the head; do not let my head refuse it; Yet my prayer is always against evil deeds.
Munthu wolungama andikanthe, chimenecho ndiye chifundo; andidzudzule ndiye mafuta pa mutu wanga. Mutu wanga sudzakana zimenezi. Komabe pemphero langa nthawi zonse ndi lotsutsana ndi ntchito za anthu ochita zoyipa.
6 Their judges are thrown down by the sides of the rock. They will hear my words, for they are well spoken.
Olamulira awo adzaponyedwa pansi kuchokera pa malo okwera kwambiri, ndipo anthu oyipa adzaphunzira kuti mawu anga anayankhulidwa bwino.
7 "As when one plows and breaks up the earth, our bones are scattered at the mouth of Sheol." (Sheol h7585)
Iwo adzati, “Monga momwe nkhuni zimamwazikira akaziwaza, ndi momwenso mafupa athu amwazikira pa khomo la manda.” (Sheol h7585)
8 For my eyes are on you, YHWH. In you, I take refuge. Do not leave my soul destitute.
Koma maso anga akupenyetsetsa Inu Ambuye Wamphamvuzonse; ndimathawira kwa Inu, musandipereke ku imfa.
9 Keep me from the snare which they have laid for me, from the traps of evildoers.
Mundipulumutse ku misampha imene anditchera, ku makhwekhwe amene anthu oyipa andikonzera.
10 Let the wicked fall together into their own nets, while I pass by.
Anthu oyipa akodwe mʼmaukonde awo, mpaka ine nditadutsa mwamtendere.

< Psalms 141 >