< Psalms 139 >

1 [For the Chief Musician. A Psalm by David.] YHWH, you have searched me, and you know me.
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la Davide. Inu Yehova, mwandisanthula ndipo mukundidziwa.
2 You know my sitting down and my rising up. You perceive my thoughts from afar.
Inu mumadziwa pamene ndikhala pansi ndi pamene ndidzuka; mumazindikira maganizo anga muli kutali.
3 You search out my path and my lying down, and are acquainted with all my ways.
Mumapenyetsetsa pamene ndikutuluka ndi kugona kwanga; mumadziwa njira zanga zonse.
4 For there is not a word on my tongue, but, look, YHWH, you know it altogether.
Mawu asanatuluke pa lilime langa mumawadziwa bwinobwino, Inu Yehova.
5 You encircle me behind and in front, and you place your hand upon me.
Mumandizinga kumbuyo ndi kutsogolo komwe; mwasanjika dzanja lanu pa ine.
6 This knowledge is beyond me. It's lofty. I can't attain it.
Nzeru zimenezi ndi zopitirira nzeru zanga, ndi zapamwamba kuti ine ndizipeze.
7 Where could I go from your Spirit? Or where could I flee from your presence?
Kodi ndingapite kuti kufuna kuzemba Mzimu wanu? Kodi ndingathawire kuti kuchoka pamaso panu?
8 If I ascend up into heaven, you are there. If I make my bed in Sheol, look, you are there. (Sheol h7585)
Ndikakwera kumwamba, Inu muli komweko; ndikakagona ku malo a anthu akufa, Inu muli komweko. (Sheol h7585)
9 If I take the wings of the dawn, and settle in the uttermost parts of the sea;
Ngati ndiwulukira kotulukira dzuwa, ngati ndikakhala ku malekezero a nyanja,
10 Even there your hand will lead me, and your right hand will hold me.
kumenekonso dzanja lanu lidzanditsogolera, dzanja lanu lamanja lidzandigwiriziza.
11 If I say, "Surely the darkness will overwhelm me; the light around me will be night;"
Ndikanena kuti, “Zoonadi, mdima udzandibisa ndithu ndipo kuwunika kukhale mdima mondizungulira,”
12 even the darkness doesn't hide from you, but the night shines as the day. The darkness is like light to you.
komabe mdimawo sudzakhala mdima kwa Inu; usiku udzawala ngati masana, pakuti mdima uli ngati kuwunika kwa Inu.
13 For you formed my inmost being. You knit me together in my mother's womb.
Pakuti Inu munalenga za mʼkati mwanga; munandiwumba pamodzi mʼmimba mwa amayi anga.
14 I will give thanks to you, for I am awesomely and wonderfully made. Your works are wonderful, and my soul knows that very well.
Ndimakuyamikani chifukwa ndinapangidwa mochititsa mantha ndi modabwitsa; ntchito zanu ndi zodabwitsa, zimenezi ndimazidziwa bwino lomwe.
15 My frame wasn't hidden from you, when I was made in secret, woven together in the depths of the earth.
Mapangidwe anga sanabisike pamaso panu pamene ndimapangidwa mʼmalo achinsinsi, pamene ndinkawumbidwa mwaluso mʼmimba ya amayi anga.
16 Your eyes saw my body. In your book they were all written, the days that were ordained for me, when as yet there were none of them.
Maso anu anaona thupi langa lisanawumbidwe. Masiku onse amene anapatsidwa kwa ine, analembedwa mʼbuku lanu asanayambe nʼkuwerengedwa komwe.
17 How precious to me are your thoughts, God. How vast is the sum of them.
Zolingalira zanu pa ine ndi zamtengowapatali, Inu Mulungu, ndi zosawerengeka ndithu!
18 If I would count them, they are more in number than the sand. When I wake up, I am still with you.
Ndikanaziwerenga, zikanakhala zochuluka kuposa mchenga; pamene ndadzuka, ndili nanube.
19 If only you, God, would kill the wicked. Get away from me, you bloodthirsty men.
Ndi bwino mukanangopha anthu oyipa, Inu Mulungu! Chokereni inu anthu owononga anzanu!
20 For they speak against you wickedly. Your enemies take your name in vain.
Amayankhula za Inu ndi zolinga zoyipa; adani anu amagwiritsa ntchito dzina lanu molakwika.
21 YHWH, do I not hate those who hate you? Am I not grieved with those who rise up against you?
Kodi ine sindidana nawo amene amakudani, Inu Yehova? Kodi sindinyansidwa nawo amene amakuwukirani?
22 I hate them with perfect hatred. They have become my enemies.
Ndimadana nawo kwathunthu; ndi adani anga.
23 Search me, God, and know my heart. Try me, and know my thoughts.
Santhuleni, Inu Mulungu ndipo mudziwe mtima wanga; Yeseni ndipo mudziwe zolingalira zanga.
24 See if there is any wicked way in me, and lead me in the everlasting way.
Onani ngati muli mayendedwe aliwonse oyipa mwa ine, ndipo munditsogolere mʼnjira yanu yamuyaya.

< Psalms 139 >