< Psalms 125 >

1 [A Song of Ascents.] Those who trust in YHWH are as Mount Zion, which cannot be moved, but remains forever.
Nyimbo yoyimba pokwera ku Yerusalemu. Amene amadalira Yehova ali ngati phiri la Ziyoni, limene silingagwedezeke koma ndi lokhala mpaka muyaya.
2 As the mountains surround Jerusalem, so YHWH surrounds his people from this time forth and forevermore.
Monga mapiri azungulira Yerusalemu, momwemonso Yehova azungulira anthu ake kuyambira tsopano mpaka muyaya.
3 For the scepter of wickedness won't remain over the allotment of the righteous; so that the righteous won't use their hands to do evil.
Ndodo yaufumu ya anthu oyipa sidzakhala pa dziko limene lapatsidwa kwa anthu olungama, kuti anthu olungamawo angachite nawonso zoyipa.
4 Do good, YHWH, to those who are good, to those who are upright in their hearts.
Yehova chitirani zabwino amene ndi abwino, amene ndi olungama mtima
5 But as for those who turn aside to their crooked ways, YHWH will lead them away with evildoers. Peace be on Israel.
Koma amene amatembenukira ku njira zokhotakhota, Yehova adzawachotsa pamodzi ndi anthu ochita zoyipa. Mtendere ukhale pa Israeli.

< Psalms 125 >