< Psalms 120 >

1 [A Song of Ascents.] In my distress, I cried to YHWH. He answered me.
Nyimbo yoyimba pokwera ku Yerusalemu. Ndimafuwulira kwa Yehova mʼmasautso anga, ndipo Iye amandiyankha.
2 Deliver my soul, YHWH, from lying lips, from a deceitful tongue.
Pulumutseni Yehova ku milomo yabodza, ndi kwa anthu achinyengo.
3 What will be given to you, and what will be done more to you, you deceitful tongue?
Kodi adzakuchitani chiyani, ndipo adzawonjezerapo zotani, inu anthu achinyengo?
4 Sharp arrows of the mighty, with coals of juniper.
Adzakulangani ndi mivi yakuthwa ya munthu wankhondo, ndi makala oyaka a mtengo wa tsanya.
5 Woe is me, that I live in Meshech, that I dwell among the tents of Kedar.
Tsoka ine kuti ndimakhala ku Mesaki, kuti ndimakhala pakati pa matenti a ku Kedara!
6 My soul has had her dwelling too long with him who hates peace.
Kwa nthawi yayitali ndakhala pakati pa iwo amene amadana ndi mtendere.
7 I am for peace, but when I speak, they are for war.
Ine ndine munthu wamtendere; koma ndikamayankhula, iwo amafuna nkhondo.

< Psalms 120 >