< Psalms 12 >

1 [For the Chief Musician; upon an eight-stringed lyre. A Psalm of David.] Help, YHWH; for the faithful ceases. For the loyal have vanished from among the descendants of Adam.
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Monga mwa mayimbidwe seminiti. Salimo la Davide. Thandizeni Yehova pakuti palibe munthu wokhulupirika; okhulupirika akusowa pakati pa anthu.
2 Everyone lies to his neighbor. They speak with flattering lips, and with a double heart.
Aliyense amanamiza mʼbale wake; ndi pakamwa pawo pabodza amayankhula zachinyengo.
3 May YHWH cut off all flattering lips, and the tongue that boasts,
Inu Yehova tsekani milomo yonse yachinyengo ndi pakamwa paliponse podzikuza.
4 who have said, "With our tongue we will prevail. Our lips are our own. Who is lord over us?"
Pakamwa pamene pamati, “Ife tidzapambana ndi kuyankhula kwathu; pakamwapa ndi pathupathu, tsono mbuye wathu ndani?”
5 "Because of the oppression of the weak and because of the groaning of the needy, I will now arise," says YHWH; "I will place in safety the one who longs for it."
“Chifukwa cha kuponderezedwa kwa anthu opanda mphamvu ndi kubuwula kwa anthu osowa, Ine ndidzauka tsopano,” akutero Yehova, “Ndidzawateteza kwa owazunza.”
6 The words of YHWH are flawless words, as silver refined in a clay furnace, purified seven times.
Ndipo mawu a Yehova ndi angwiro monga siliva oyengedwa mʼngʼanjo yadothi, oyengedwa kasanu nʼkawiri.
7 You, YHWH, will protect us. You will guard us from this generation forever.
Inu Yehova mudzatitchinjiriza ndipo mudzatiteteza kwa anthu otere kwamuyaya.
8 The wicked walk on every side, when what is vile is exalted among the descendants of Adam.
Oyipa amangoyendayenda ponseponse anthu akamayamikira zochita zawo.

< Psalms 12 >