< Psalms 116 >

1 I love YHWH, because he listens to my voice, and my cries for mercy.
Ndimakonda Yehova pakuti Iyeyo amamva mawu anga; Iye amamva kulira kwanga kopempha chifundo.
2 Because he has turned his ear to me, therefore I will call on him as long as I live.
Pakuti ananditchera khutu, ndidzayitana Iye masiku onse a moyo wanga.
3 The cords of death surrounded me, the pains of Sheol got a hold of me. I found trouble and sorrow. (Sheol h7585)
Zingwe za imfa zinandizinga, zoopsa za ku dziko la anthu akufa zinandigwera; ndinapeza mavuto ndi chisoni. (Sheol h7585)
4 Then I called on the name of YHWH: "YHWH, I beg you, deliver my soul."
Pamenepo ndinayitana dzina la Yehova: “Inu Yehova, pulumutseni!”
5 YHWH is Gracious and righteous. Yes, our God is merciful.
Yehova ndi wokoma mtima ndi wolungama Mulungu wathu ndi wodzaza ndi chifundo.
6 YHWH preserves the simple. I was brought low, and he saved me.
Yehova amateteza munthu wodzichepetsa mtima; pamene ndinali ndi chosowa chachikulu, Iye anandipulumutsa.
7 Return to your rest, my soul, for YHWH has dealt bountifully with you.
Pumula iwe moyo wanga, pakuti Yehova wakuchitira zokoma.
8 For you have delivered my soul from death, my eyes from tears, and my feet from falling.
Pakuti Inu Yehova mwapulumutsa moyo wanga ku imfa, maso anga ku misozi, mapazi anga kuti angapunthwe,
9 I will walk before YHWH in the land of the living.
kuti ine ndiyende pamaso pa Yehova mʼdziko la anthu amoyo.
10 I believed, therefore I said, "I am greatly afflicted."
Ine ndinakhulupirira; choncho ndinati, “Ndasautsidwa kwambiri.”
11 I said in my haste, "All men are liars."
Ndipo ndili mʼnkhawa yanga ndinati, “Anthu onse ndi abodza.”
12 What will I give to YHWH for all his benefits toward me?
Ndingamubwezere chiyani Yehova, chifukwa cha zokoma zake zonse zimene wandichitira?
13 I will take the cup of salvation, and call on the name of YHWH.
Ndidzakweza chikho cha chipulumutso ndipo ndidzayitana dzina la Yehova.
14 I will pay my vows to YHWH, yes, in the presence of all his people.
Ndidzakwaniritsa malonjezo anga kwa Yehova pamaso pa anthu ake onse.
15 Precious in the sight of YHWH is the death of his faithful ones.
Imfa ya anthu oyera mtima ndi yamtengowapatali pamaso pa Yehova.
16 YHWH, truly I am your servant. I am your servant, the son of your handmaid. You have freed me from my chains.
Inu Yehova, zoonadi ndine mtumiki wanu: ndine mtumiki wanu, mwana wa mdzakazi wanu; Inu mwamasula maunyolo anga.
17 I will offer to you the sacrifice of thanksgiving, and will call on the name of YHWH.
Ndidzapereka nsembe yachiyamiko kwa Inu ndipo ndidzayitanira pa dzina la Yehova.
18 I will pay my vows to YHWH, yes, in the presence of all his people,
Ndidzakwaniritsa malonjezo anga kwa Yehova pamaso pa anthu ake onse,
19 in the courts of YHWH's house, in the midst of you, Jerusalem. Praise JAH.
mʼmabwalo a nyumba ya Yehova, mʼkati mwako iwe Yerusalemu. Tamandani Yehova.

< Psalms 116 >