< Psalms 114 >

1 When Israel went forth out of Egypt, the house of Jacob from a people of foreign language;
Pamene Israeli anatuluka mu Igupto, nyumba ya Yakobo kuchoka ku mtundu wa anthu a chiyankhulo chachilendo,
2 Judah became his sanctuary, Israel his dominion.
Yuda anasanduka malo opatulika a Mulungu, Israeli anasanduka ufumu wake.
3 The sea saw it, and fled. The Jordan was driven back.
Nyanja inaona ndi kuthawa, mtsinje wa Yorodani unabwerera mʼmbuyo;
4 The mountains skipped like rams, the little hills like lambs.
mapiri analumphalumpha ngati nkhosa zazimuna, timapiri ngati ana ankhosa.
5 What was it, you sea, that you fled? You Jordan, that you turned back?
Nʼchifukwa chiyani iwe unathawa? iwe mtsinje wa Yorodani unabwereranji mʼmbuyo?
6 You mountains, that you skipped like rams; you little hills, like lambs?
inu mapiri, munalumphalumphiranji ngati nkhosa zazimuna, inu timapiri, ngati ana ankhosa?
7 Tremble, you earth, at the presence of the Lord, at the presence of the God of Jacob,
Njenjemera pamaso pa Ambuye iwe dziko lapansi, pamaso pa Mulungu wa Yakobo,
8 who turned the rock into a pool of water, the flint into a spring of waters.
amene anasandutsa thanthwe kukhala chitsime, thanthwe lolimba kukhala akasupe a madzi.

< Psalms 114 >