< Psalms 106 >

1 Praise JAH. Give thanks to YHWH, for he is good, for his loving kindness endures forever.
Tamandani Yehova. Yamikani Yehova chifukwa ndi wabwino; pakuti chikondi chake ndi chosatha.
2 Who can utter the mighty acts of YHWH, or fully declare all his praise?
Ndani angathe kufotokoza za ntchito zamphamvu za Yehova kapena kumutamanda mokwanira?
3 Blessed are those who uphold justice, who practice righteousness at all times.
Odala ndi amene amasunga chilungamo, amene amachita zolungama nthawi zonse.
4 Remember me, YHWH, with the favor that you show to your people. Visit me with your salvation,
Mundikumbukire Yehova, pamene mukuonetsa kukoma mtima kwanu kwa anthu anu, bwerani mudzandithandize pamene mukuwapulumutsa iwo,
5 that I may see the prosperity of your chosen, that I may rejoice in the gladness of your nation, that I may glory with your inheritance.
kuti ndidzasangalale ndi chuma cha anthu anu osankhika, kuti ndidzakhale nacho chimwemwe cha anthu anu ndi kukhala pamodzi ndi cholowa chanu pa kukutamandani.
6 We have sinned with our fathers. We have committed iniquity. We have done wickedly.
Ife tachimwa monga momwe anachitira makolo athu; tachita zolakwa ndipo tachita moyipa.
7 Our fathers did not understand your wonders in Egypt. They did not remember the multitude of your loving kindnesses, but were rebellious at the sea, even at the Red Sea.
Pamene makolo athu anali mu Igupto, sanalingalire za zozizwitsa zanu; iwo sanakumbukire kukoma mtima kwanu kochuluka, ndipo anawukira Inu pa Nyanja Yofiira.
8 Nevertheless he saved them for his name's sake, that he might make his mighty power known.
Komabe Iye anawapulumutsa chifukwa cha dzina lake, kuti aonetse mphamvu zake zazikulu.
9 He rebuked the Red Sea also, and it was dried up; so he led them through the depths, as through a desert.
Anadzudzula Nyanja Yofiira, ndipo inawuma; anawatsogolera mʼnyanja yakuya ngati akuyenda mʼchipululu.
10 He saved them from the hand of him who hated them, and redeemed them from the hand of the enemy.
Anawapulumutsa mʼdzanja la amaliwongo; anawawombola mʼdzanja la mdani.
11 The waters covered their adversaries. There was not one of them left.
Madzi anamiza adani awo, palibe mmodzi wa iwo anapulumuka.
12 Then they believed his words. They sang his praise.
Kenaka iwo anakhulupirira malonjezo ake ndi kuyimba nyimbo zamatamando.
13 They soon forgot his works. They did not wait for his counsel,
Koma posachedwa anayiwala zimene Iye anachita, ndipo sanayembekezere uphungu wake.
14 but gave in to craving in the desert, and tested God in the wasteland.
Mʼchipululu, anadzipereka ku zilakolako zawo; mʼdziko lopanda kanthu anayesa Mulungu.
15 He gave them their request, but sent leanness into their soul.
Choncho Iye anawapatsa chimene anapempha, koma anatumiza nthenda yowondetsa.
16 They envied Moses also in the camp, and Aaron, YHWH's holy one.
Mʼmisasa, anachitira nsanje Mose ndi Aaroni, amene Yehova anadzipatulira.
17 The earth opened and swallowed up Dathan, and covered the company of Abiram.
Nthaka inatsekuka ndipo inameza Datani; inakwirira gulu la Abiramu.
18 A fire was kindled in their company. The flame burned up the wicked.
Moto unayaka pakati pa otsatira awo; lawi lamoto linapsereza anthu oyipa.
19 They made a calf in Horeb, and worshiped a molten image.
Iwo anapanga mwana wangʼombe pa Horebu ndi kulambira fano loyengedwa kuchokera ku chitsulo.
20 Thus they exchanged their glory for an image of a bull that eats grass.
Anasinthanitsa ulemerero wawo ndi fano la ngʼombe yayimuna imene imadya udzu.
21 They forgot God, their Savior, who had done great things in Egypt,
Anayiwala Mulungu amene anawapulumutsa, amene anachita zinthu zazikulu mu Igupto,
22 Wondrous works in the land of Ham, and awesome things by the Red Sea.
zozizwitsa mʼdziko la Hamu ndi machitidwe ake woopsa pa Nyanja Yofiira.
23 Therefore he said that he would destroy them, had Moses, his chosen, not stood before him in the breach, to turn away his wrath, so that he wouldn't destroy them.
Choncho Iye anawawuza kuti adzawawononga, pakanapanda Mose, mtumiki wake wosankhidwa, kuyima pamaso pake, ndi kuletsa mkwiyo wake kuti usawawononge.
24 Yes, they despised the pleasant land. They did not believe his word,
Motero iwo ananyoza dziko lokoma; sanakhulupirire malonjezo ake.
25 but murmured in their tents, and did not listen to YHWH's voice.
Anangʼungʼudza mʼmatenti mwawo ndipo sanamvere Yehova.
26 Therefore he swore to them that he would overthrow them in the wilderness,
Kotero Iye analumbira atakweza dzanja lake, kuti adzachititsa kuti iwowo afere mʼchipululu,
27 and that he would make their offspring fall among the nations, and scatter them in the lands.
kuchititsa kuti zidzukulu zawo zifere pakati pa anthu a mitundu ina ndi kuwabalalitsa mʼdziko lonse.
28 They joined themselves also to Baal Peor, and ate the sacrifices of the dead.
Iwo anayamba kupembedza Baala-Peori ndi kudya nsembe zoperekedwa kwa milungu yopanda moyo;
29 Thus they provoked him to anger with their deeds. The plague broke in on them.
anaputa mkwiyo wa Yehova pa machitidwe awo oyipa, ndipo mliri unabuka pakati pawo.
30 Then Phinehas stood up, and executed judgment, so the plague was stopped.
Koma Finehasi anayimirira ndi kulowererapo, ndipo mliri unaleka.
31 That was credited to him for righteousness, for all generations to come.
Chimenechi ndicho chinayesedwa chilungamo chake, kwa mibado yosatha imene ikubwera.
32 They angered him also at the waters of Meribah, so that Moses was troubled for their sakes;
Pa madzi a ku Meriba iwo anakwiyitsa Yehova ndipo mavuto anabwera kwa Mose chifukwa cha anthuwo,
33 because they were rebellious against his spirit, he spoke rashly with his lips.
pakuti iwowo anawukira mzimu wa Mulungu, ndipo pa milomo ya Mose panatuluka mawu osayenera.
34 They did not destroy the peoples, as YHWH commanded them,
Aisraeliwo sanawononge mitundu ya anthu monga momwe Yehova anawalamulira.
35 but mixed themselves with the nations, and learned their works.
Koma anasakanizana ndi anthu a mitundu inayo ndi kuphunzira miyambo yawo.
36 They served their idols, which became a snare to them.
Ndipo anapembedza mafano awo, amene anakhala msampha kwa iwowo.
37 Yes, they sacrificed their sons and their daughters to demons.
Anapereka nsembe ana awo aamuna ndi ana awo aakazi kwa ziwanda.
38 They shed innocent blood, even the blood of their sons and of their daughters, whom they sacrificed to the idols of Canaan. The land was polluted with blood.
Anakhetsa magazi a anthu osalakwa, magazi a ana awo aamuna ndi a ana awo aakazi, amene anawapereka nsembe kwa mafano a ku Kanaani, ndipo dziko linayipitsidwa ndi magazi awo.
39 Thus were they defiled with their works, and prostituted themselves in their deeds.
Iwo anadzidetsa okha ndi zimene anachita; ndi machitidwe awo amakhala ngati munthu wachigololo.
40 Therefore YHWH burned with anger against his people. He abhorred his inheritance.
Tsono Yehova anakwiya ndi anthu ake ndipo ananyansidwa ndi cholowa chake.
41 He gave them into the hand of the nations. Those who hated them ruled over them.
Iye anawapereka kwa anthu a mitundu ina, ndipo adani awo anawalamulira.
42 Their enemies also oppressed them. They were brought into subjection under their hand.
Adani awo anawazunza ndi kuwakhazika pansi pa mphamvu yawo.
43 Many times he delivered them, but they were rebellious in their counsel, and were brought low in their iniquity.
Iye ankawapulumutsa nthawi zambiri, koma iwo ankatsimikiza za kuwukira ndipo anawonongeka mʼmachimo awo.
44 Nevertheless he regarded their distress, when he heard their cry.
Koma Iye anaona kuzunzika kwawo pamene anamva kulira kwawo;
45 He remembered for them his covenant, and repented according to the multitude of his loving kindnesses.
Chifukwa cha iwo Iye anakumbukira pangano lake ndipo anawalezera mtima chifukwa cha kukula kwa chikondi chake.
46 He made them also to be pitied by all those who carried them captive.
Iye anachititsa kuti amene anawagwira iwo ukapolo awamvere chisoni.
47 Save us, YHWH, our God, gather us from among the nations, to give thanks to your holy name, to triumph in your praise.
Tipulumutseni Inu Yehova Mulungu wathu, ndipo mutisonkhanitse kuchoka kwa anthu a mitundu ina kuti tithe kuyamika dzina lanu loyera ndi kunyadira mʼmatamando anu.
48 Blessed be YHWH, the God of Israel, from everlasting to everlasting. And let all the people say, "Amen." Praise JAH.
Atamandike Yehova, Mulungu wa Israeli, Kuyambira muyaya mpaka muyaya. Anthu onse anene kuti, “Ameni!” Tamandani Yehova.

< Psalms 106 >