< Psalms 1 >

1 Blessed is the one who doesn't follow the advice of the wicked, or take the path of sinners, or join in with scoffers.
Wodala munthu amene satsatira uphungu wa anthu ochimwa, kapena kuyima mʼnjira ya anthu oyipa, kapena kukhala mʼmagulu a anthu onyoza.
2 But his delight is in the law of YHWH, and on his law he meditates day and night.
Koma chikondwerero chake chili mʼmalamulo a Yehova ndipo mʼmalamulo akewo amalingaliramo usana ndi usiku.
3 He will be like a tree planted by the streams of water, that brings forth its fruit in its season, whose leaf also does not wither, and whatever he does shall prosper.
Iye ali ngati mtengo wodzalidwa mʼmbali mwa mitsinje ya madzi, umene umabereka zipatso zake pa nyengo yake ndipo masamba ake safota. Chilichonse chimene amachita amapindula nacho.
4 Not so with the wicked; instead, they are like the chaff which the wind drives away.
Sizitero ndi anthu oyipa! Iwo ali ngati mungu umene umawuluzidwa ndi mphepo.
5 Therefore the wicked shall not stand in the judgment, nor sinners in the congregation of the righteous.
Kotero anthu oyipa sadzatha kuyima pa chiweruzo, kapena anthu ochimwa mu msonkhano wa anthu olungama.
6 For YHWH knows the way of the righteous, but the way of the wicked shall perish.
Pakuti Yehova amayangʼanira mayendedwe a anthu olungama, koma mayendedwe a anthu oyipa adzawonongeka.

< Psalms 1 >