< Proverbs 8 >

1 Doesn't wisdom cry out? Doesn't understanding raise her voice?
Kodi nzeru sikuyitana? Kodi nzeru yomvetsa zinthu sinakweze mawu ake?
2 On the top of high places by the way, where the paths meet, she stands.
Nzeru imayima pa zitunda mʼmbali mwa njira, imayima pa mphambano ya misewu.
3 Beside the gates, at the entry of the city, at the entry doors, she cries aloud:
Imafuwula pafupi ndi zipata zolowera mu mzinda, pa makomo olowera imafuwula kuti,
4 "To you men, I call. I send my voice to the sons of humankind.
Inu anthu, ndikuyitana inu; ndikuyitanatu anthu onse.
5 You simple, understand prudence. You fools, be of an understanding heart.
Inu amene simudziwa kanthunu khalani ochenjera; inu amene ndi opusa, khalani ndi mtima womvetsa zinthu.
6 Hear, for I will speak excellent things. The opening of my lips is for right things.
Mverani, pakuti ndikukuwuzani zinthu zofunika kwambiri; ndatsekula pakamwa panga ndipo payankhula zolungama.
7 For my mouth speaks truth. Wickedness is an abomination to my lips.
Pakamwa panga pamayankhula zoona ndimanyansidwa ndi kuyankhula zoyipa.
8 All the words of my mouth are in righteousness. There is nothing crooked or perverse in them.
Mawu onse a pakamwa panga ndi olungama; mʼmawu angawo mulibe zokhotakhota kapena zopotoka.
9 They are all plain to him who understands, right to those who find knowledge.
Kwa anthu ozindikira, mawu anga onse ndi woona; kwa anthu amene ali ndi nzeru zomvetsa zinthu, mawu angawo ndi okhoza.
10 Receive my instruction rather than silver; knowledge rather than choice gold.
Landirani malangizo anga mʼmalo mwa siliva, nzeru zomvetsa zinthu mʼmalo mwa golide wabwino.
11 For wisdom is better than rubies. All the things that may be desired can't be compared to it.
Paja nzeru ndi yabwino kwambiri kuposa miyala yamtengowapatali, ndipo zonse zimene ungazifune sizingafanane ndi nzeru.
12 "I, wisdom, have made prudence my dwelling. Find out knowledge and discretion.
Ine nzeru, ndimakhala pamodzi ndi kuchenjera. Ine ndimadziwa zinthu ndiponso ndimalingalira zinthu bwino.
13 The fear of YHWH is to hate evil. I hate pride, arrogance, the evil way, and the perverse mouth.
Kuopa Yehova ndiko kudana ndi zoyipa. Ine ndimadana ndi kunyada, kudzitama, kuchita zoyipa, ndiponso kuyankhula zonyenga.
14 Counsel and sound knowledge are mine. I have understanding and power.
Ndine mwini uphungu ndi maganizo abwino; ndili ndi nzeru yomvetsa zinthu ndiponso mphamvu.
15 By me kings reign, and rulers decree justice.
Ndine amene ndimathandiza mafumu kulamulira. Ndimawathandiza olamulira kukhazikitsa malamulo olungama.
16 By me princes rule; nobles, and all the righteous rulers of the earth.
Ndine amene ndimathandiza akalonga polamula. Ndinenso amene ndimathandiza akuluakulu onse kulamulira bwino dziko.
17 I love those who love me. Those who seek me diligently will find me.
Ndimakonda amene amandikonda, ndipo amene amandifunafuna amandipeza.
18 With me are riches, honor, enduring wealth, and prosperity.
Ine ndili ndi chuma ndi ulemu, chuma ndi kupindula pa ntchito kokhazikika.
19 My fruit is better than gold, yes, than fine gold; my yield than choice silver.
Chipatso changa ndi chabwino kuposa golide, ngakhale golide wosalala; zimene ine ndimabereka zimaposa siliva wabwino kwambiri.
20 I walk in the way of righteousness, in the midst of the paths of justice;
Ndimachita zinthu zolungama. Ine sindipatuka mʼnjira za chilungamo.
21 That I may give wealth to those who love me. I fill their treasuries.
Ndimapereka chuma kwa amene amandikonda ndi kudzaza nyumba zawo zosungiramo chuma.
22 "YHWH created me in the beginning of his way, before his works of old.
“Yehova anandilenga ine nzeru monga ntchito yake yoyamba. Mwa ntchito zake zakalekale yoyamba ndinali ine.
23 I was set up from everlasting, from the beginning, before the earth existed.
Ndinapangidwa kalekalelo, pachiyambi penipeni dziko lapansi lisanalengedwe.
24 When there were no depths, I was brought forth, when there were no springs abounding with water.
Nyanja, akasupe odzaza ndi madzi, zonsezi kulibe pamene ine ndinkabadwa.
25 Before the mountains were settled in place, before the hills, I was brought forth;
Mapiri asanakhazikitsidwe pa malo awo, mapiri angʼonoangʼono asanakhalepo, ine ndinali nditabadwa kale,
26 while as yet he had not made the earth, nor the fields, nor the beginning of the dust of the world.
lisanalengedwe dziko lapansi ndi minda yake; lisanalengedwe dothi loyamba la dziko lapansi.
27 When he established the heavens, I was there; when he set a circle on the surface of the deep,
Ine ndinalipo pamene Yehova ankakhazikitsa mlengalenga, pamene ankalemba malire a nyanja yozama,
28 when he established the clouds above, when the springs of the deep became strong,
pamene anakhazikitsa mitambo ya mlengalenga ndi kukhazikitsa akasupe a madzi ozama,
29 when he gave to the sea its boundary, that the waters should not violate his commandment, when he marked out the foundations of the earth;
pamene anayikira nyanja malire kuti madzi asadutse malirewo, ndiponso pamene ankayika malire a dziko lapansi.
30 then I was the craftsman by his side. I was a delight day by day, always rejoicing before him,
Tsono ine ndinali pambali pake ngati mmisiri; ndikumukondweretsa tsiku ndi tsiku, kusangalala nthawi zonse pamaso pake.
31 Rejoicing in his whole world. My delight was with the sons of men.
Ndinkasangalala ndi dziko lake lonse ndiponso kumakondwera nawo anthu onse.”
32 "Now therefore, son, listen to me, for blessed are those who keep my ways.
“Ndiye tsono ana inu, ndimvereni; odala anthu amene amasunga njira zanga.
33 Hear instruction, and be wise. Do not refuse it.
Mverani malangizo anga kuti mukhale ndi nzeru; musanyozere mawu anga.
34 Blessed is the man who hears me, watching daily at my gates, waiting at my door posts.
Wodala munthu amene amandimvera, amene amakhala pa khomo panga tsiku ndi tsiku, kudikirira pa chitseko changa.
35 For whoever finds me, finds life, and will obtain favor from YHWH.
Paja aliyense amene apeza ine wapeza moyo ndipo Yehova amamukomera mtima.
36 But he who sins against me wrongs his own soul. All those who hate me love death."
Koma amene alephera kundipeza, amadzipweteka yekha; onse amene amandida amakonda imfa.”

< Proverbs 8 >