< Proverbs 24 >

1 Do not be envious of evil men; neither desire to be with them:
Usachitire nsanje anthu oyipa, usalakalake kuti uzikhala nawo,
2 for their hearts plot violence, and their lips talk about mischief.
pakuti mitima yawo imalingalira chiwawa, ndipo pakamwa pawo pamayankhula zoyambitsa mavuto.
3 Through wisdom a house is built; by understanding it is established;
Nyumba imamangidwa ndi anthu anzeru, ndipo imakhazikika ndi anthu odziwa zinthu;
4 by knowledge the rooms are filled with all rare and beautiful treasure.
Munthu wodziwa zinthu angathe kudzaza zipinda zake ndi chuma chamtengowapatali ndiponso chabwino.
5 A wise man has great power; and a knowledgeable man increases strength;
Munthu wodziwa zinthu ali ndi mphamvu yayikulu kuposa munthu wanyonga zambiri, ndipo munthu wachidziwitso amaposa munthu wamphamvu.
6 for by wise guidance you wage your war; and victory is in many advisors.
Pafunika malangizo kuti ukamenye nkhondo. Pakakhala aphungu ambiri kupambana kumakhalapo.
7 Wisdom is too high for a fool: he doesn't open his mouth in the gate.
Nzeru ndi chinthu chapatali kwambiri kwa chitsiru; chilibe choti chiyankhule pabwalo la milandu pa chipata.
8 One who plots to do evil will be called a schemer.
Amene amakonzekera kuchita zoyipa adzatchedwa mvundulamadzi.
9 The schemes of folly are sin. The mocker is detested by men.
Kukonzekera kuchita za uchitsiru ndi tchimo, ndipo munthu wonyoza amanyansa anthu.
10 If you falter in the time of trouble, your strength is small.
Ngati utaya mtima nthawi ya mavuto ndiye kuti mphamvu yako ndi yochepadi!
11 Rescue those who are being led away to death. Indeed, hold back those who are staggering to the slaughter.
Uwapulumutse amene akutengedwa kuti akaphedwe; uwalanditse amene akuyenda movutika kupita kokaphedwa.
12 If you say, "Look, we did not know this;" doesn't he who weighs the hearts consider it? He who keeps your soul, doesn't he know it? Shall he not render to every man according to his work?
Ukanena kuti, “Koma ife sitinadziwe kanthu za izi,” kodi Iye amene amasanthula mtima sazindikira zimenezi? Kodi Iye amene amateteza moyo wako sazidziwa zimenezi? Kodi Iye sadzalipira munthu malingana ndi ntchito zake?
13 My son, eat honey, for it is good; the droppings of the honeycomb, which are sweet to your taste.
Mwana wanga, uzidya uchi popeza ndi wabwino; uchi wochokera mʼchisa cha njuchi ndi wokoma ukawulawa.
14 Likewise, know that wisdom is such to your soul; if you have found it, then there will be a reward, and your hope will not be cut off.
Udziwe kuti nzeru ndi yoteronso pa moyo wako; ngati uyipeza nzeruyo, zinthu zidzakuyendera bwino mʼtsogolo, ndipo chiyembekezo chako sichidzapita pachabe.
15 Do not lie in wait, wicked man, against the habitation of the righteous. Do not destroy his resting place.
Usachite zachifwamba nyumba ya munthu wolungama ngati munthu woyipa. Usachite nayo nkhondo nyumba yake;
16 For the righteous may fall seven times, but gets up again, but the wicked will stumble in adversity.
paja munthu wolungama akagwa kasanu nʼkawiri amadzukiriranso. Koma woyipa adzathedwa tsoka likadzawafikira.
17 Do not rejoice when your enemy falls. Do not let your heart be glad when he is overthrown;
Usamakondwera ndi kugwa kwa mdani wako. Mtima wako usamasangalale iye akapunthwa.
18 lest YHWH see it, and it displease him, and he turn away his wrath from him.
Kuopa kuti Yehova ataziona zimenezi nayipidwa nazo, angaleke kukwiyira mdaniyo.
19 Do not fret yourself because of evildoers; neither be envious of the wicked:
Usavutike mtima chifukwa cha anthu ochita zoyipa kapena kuchitira nsanje anthu oyipa,
20 for there will be no reward to the evil man; and the lamp of the wicked shall be snuffed out.
paja munthu woyipa alibe tsogolo. Moyo wa anthu oyipa adzawuzimitsa ngati nyale.
21 My son, fear YHWH and the king. Do not join those who are rebellious:
Mwana wanga, uziopa Yehova ndi mfumu, ndipo usamagwirizana ndi anthu owachitira mwano,
22 for their calamity will rise suddenly; the destruction from them both—who knows?
awiri amenewa amagwetsa tsoka mwadzidzidzi. Ndani angadziwe mavuto amene angagwetse?
23 These also are sayings of the wise. To show partiality in judgment is not good.
Malangizo enanso a anthu anzeru ndi awa: Kukondera poweruza mlandu si chinthu chabwino:
24 He who says to the wicked, "You are righteous;" peoples shall curse him, and nations shall abhor him?
Aliyense amene amawuza munthu wolakwa kuti, “Iwe ndi munthu wosalakwa,” anthu a mitundu yonse adzamutemberera, ndi mitundu ya anthu idzayipidwa naye.
25 but it will go well with those who convict the guilty, and a rich blessing will come on them.
Koma olanga anthu oyipa zinthu zidzawayendera bwino ndipo madalitso ochuluka adzakhala pa iwo.
26 An honest answer is like a kiss on the lips.
Woyankhula mawu owona ndiye amaonetsa chibwenzi chenicheni.
27 Prepare your work outside, and get your fields ready. Afterwards, build your house.
Ugwiriretu ntchito zako zonse, makamaka za ku munda ndipo pambuyo pake uyambe kumanga nyumba.
28 Do not be a witness against your neighbor without cause. Do not deceive with your lips.
Usakhale mboni yotsutsa mnzako popanda chifukwa, kapena kugwiritsa ntchito pakamwa pako kunena zachinyengo.
29 Do not say, "I will do to him as he has done to me; I will render to the man according to his work."
Usanene kuti, “Ine ndidzamuchitira iye monga momwe wandichitira ine; ndidzamubwezera munthu ameneyo zimene anandichitira.”
30 I went by the field of the sluggard, by the vineyard of the man void of understanding;
Ndinkayenda mʼmbali mwa munda wa munthu waulesi ndinadutsa munda wamphesa wa munthu wopanda nzeru.
31 Look, it was all grown over with thorns. Its surface was covered with nettles, and its stone wall was broken down.
Ndinapeza kuti paliponse mʼmundamo munali mutamera minga, mʼnthaka imeneyo munali mutamera khwisa, ndipo mpanda wake wamiyala unali utawonongeka.
32 Then I saw, and considered well. I saw, and received instruction:
Tsono nditaona ndinayamba kuganizira mu mtima mwanga ndipo ndinatolapo phunziro ili:
33 a little sleep, a little slumber, a little folding of the hands to sleep;
Ukati, “Bwanji ndigone pangʼono,” kapena “Ndiwodzereko pangʼono,” kapenanso “Ndipinde manja pangʼono kuti ndipumule,”
34 so your poverty will come as a robber, and your want as an armed man.
umphawi udzafika pa iwe ngati mbala ndipo usiwa udzakupeza ngati munthu wachifwamba.

< Proverbs 24 >