< Proverbs 15 >

1 A gentle answer turns away wrath, but a harsh word stirs up anger.
Kuyankha kofatsa kumathetsa mkwiyo, koma mawu ozaza amautsa ukali.
2 The tongue of the wise commends knowledge, but the mouth of fools gush out folly.
Munthu wanzeru amayankhula zinthu za nzeru, koma pakamwa pa zitsiru pamatulutsa za uchitsiru.
3 The eyes of YHWH are everywhere, keeping watch on the evil and the good.
Maso a Yehova ali ponseponse, amayangʼana pa oyipa ndi abwino omwe.
4 A gentle tongue is a tree of life, but deceit in it crushes the spirit.
Kuyankhula kodekha kuli ngati mtengo wopatsa moyo, koma kuyankhula kopotoka kumapweteka mtima.
5 A fool despises his father's correction, but he who heeds reproof shows prudence.
Chitsiru chimanyoza mwambo wa abambo ake, koma wochenjera amasamala chidzudzulo.
6 In the house of the righteous is much treasure, but the income of the wicked brings trouble.
Munthu wolungama amakhala ndi chuma chambiri, zimene woyipa amapindula nazo zimamugwetsa mʼmavuto.
7 The lips of the wise spread knowledge; not so with the heart of fools.
Pakamwa pa anthu anzeru pamafalitsa nzeru; koma mitima ya zitsiru sitero.
8 The sacrifice made by the wicked is an abomination to YHWH, but the prayer of the upright is his delight.
Nsembe za anthu oyipa zimamunyansa Yehova, koma amakondwera ndi pemphero la anthu owona mtima.
9 The way of the wicked is an abomination to YHWH, but he loves him who follows after righteousness.
Ntchito za anthu oyipa zimamunyansa Yehova koma amakonda amene amafunafuna chilungamo.
10 There is stern discipline for one who forsakes the way: whoever hates reproof shall die.
Amene amasiya njira yabwino adzalangidwa koopsa. Odana ndi chidzudzulo adzafa.
11 Sheol and Abaddon are before YHWH—how much more then the hearts of human beings. (Sheol h7585)
Manda ndi chiwonongeko ndi zosabisika pamaso pa Yehova, nanji mitima ya anthu! (Sheol h7585)
12 A scoffer doesn't love to be reproved; he will not go to the wise.
Wonyoza sakonda kudzudzulidwa; iye sapita kwa anthu anzeru.
13 A glad heart makes a cheerful face; but an aching heart breaks the spirit.
Mtima wokondwa umachititsa nkhope kukhala yachimwemwe, koma mtima wosweka umawawitsa moyo.
14 The heart of one who has understanding seeks knowledge, but the mouths of fools feed on folly.
Mtima wa munthu wozindikira zinthu umafunafuna nzeru, koma pakamwa pa zitsiru pamadya uchitsiru wawo.
15 All the days of the afflicted are wretched, but one who has a cheerful heart enjoys a continual feast.
Munthu woponderezedwa masiku ake onse amakhala oyipa, koma mtima wachimwemwe umakhala pa chisangalalo nthawi zonse.
16 Better is little, with the fear of YHWH, than great treasure with trouble.
Kuli bwino kukhala ndi zinthu pangʼono nʼkumaopa Yehova, kusiyana ndi kukhala ndi chuma chambiri uli pamavuto.
17 Better is a dinner of herbs, where love is, than a fattened calf with hatred.
Kuli bwino kudyera ndiwo zamasamba pamene pali chikondi, kusiyana ndi kudyera nyama yangʼombe yonenepa pamene pali udani.
18 A wrathful man stirs up contention, but one who is slow to anger appeases strife.
Munthu wopsa mtima msanga amayambitsa mikangano, koma munthu woleza mtima amathetsa ndewu.
19 The way of the sluggard is like a thorn patch, but the path of the upright is a highway.
Njira ya munthu waulesi ndi yowirira ndi mtengo waminga, koma njira ya munthu wolungama ili ngati msewu waukulu.
20 A wise son makes a father glad, but a foolish man despises his mother.
Mwana wanzeru amakondweretsa abambo ake, koma mwana wopusa amanyoza amayi ake.
21 Folly is joy to one who is void of wisdom, but a man of understanding keeps his way straight.
Uchitsiru umakondweretsa munthu wopanda nzeru, koma munthu womvetsa zinthu amayenda mowongoka.
22 Where there is no counsel, plans fail; but in a multitude of counselors they are established.
Popanda uphungu zolinga zako munthu zimalephereka, koma pakakhala aphungu ambiri zolinga zimatheka.
23 Joy comes to a man with the reply of his mouth. How good is a word at the right time.
Munthu amakondwera ndi kuyankha koyenera, ndipo mawu onena pa nthawi yake ndi okoma.
24 The path of life leads upward for the wise, to keep him from going downward to Sheol. (Sheol h7585)
Munthu wanzeru amatsata njira yopita ku moyo kuti apewe malo okhala anthu akufa. (Sheol h7585)
25 YHWH will uproot the house of the proud, but he will keep the widow's borders intact.
Yehova amapasula nyumba ya munthu wonyada koma amasamalira malo a mkazi wamasiye.
26 YHWH detests the thoughts of the wicked, but the thoughts of the pure are pleasing.
Maganizo a anthu oyipa amamunyansa Yehova, koma mawu a anthu oyera mtima amamusangalatsa.
27 He who is greedy for gain troubles his own house, but he who hates bribes will live.
Munthu wofuna phindu mwachinyengo amavutitsa banja lake, koma wodana ndi ziphuphu adzakhala ndi moyo.
28 The heart of the righteous weighs answers, but the mouth of the wicked gushes out evil.
Munthu wolungama amaganizira za mmene ayankhire, koma pakamwa pa munthu woyipa pamatulutsa mawu oyipa.
29 YHWH is far from the wicked, but he hears the prayer of the righteous.
Yehova amakhala kutali ndi anthu oyipa, koma amamva pemphero la anthu olungama.
30 The light of the eyes rejoices the heart. Good news gives health to the bones.
Kuwala kwa maso kumasangalatsa mtima ndipo uthenga wabwino umalimbitsa munthu.
31 The ear that listens to reproof lives, and will be at home among the wise.
Womvera mawu a chidzudzulo amene apatsa moyo adzakhala pakati pa anthu anzeru.
32 He who refuses correction despises his own soul, but he who listens to reproof gets understanding.
Amene amanyoza mwambo amadzinyoza yekha, koma womvera mawu a chidzudzulo amapeza nzeru zomvetsa zinthu.
33 The fear of YHWH teaches wisdom. Before honor is humility.
Kuopa Yehova kumaphunzitsa munthu nzeru, ndipo kudzichepetsa ndi ulemu chili patsogolo ndi kudzichepetsa.

< Proverbs 15 >