< Proverbs 13 >

1 A wise son listens to his father's instruction, but a scoffer doesn't listen to rebuke.
Mwana wanzeru amamvera malangizo a abambo ake, koma mwana wonyoza samamvetsera chidzudzulo.
2 By the fruit of his lips, a man enjoys good things; but the unfaithful crave violence.
Munthu amapeza zinthu zabwino chifukwa cha mawu ake, koma anthu osakhulupirika amalakalaka zachiwawa basi.
3 He who guards his mouth guards his soul. One who opens wide his lips comes to ruin.
Iye amene amagwira pakamwa pake amateteza moyo wake, koma amene amayankhula zopanda pake adzawonongeka.
4 The soul of the sluggard desires, and has nothing, but the desire of the diligent shall be fully satisfied.
Munthu waulesi amakhumbira zinthu koma sapeza kanthu, koma munthu wakhama adzalemera.
5 A righteous man hates lies, but a wicked man brings shame and disgrace.
Munthu wolungama amadana ndi zabodza, koma zochita za munthu woyipa zimanyansa ndiponso zimachititsa manyazi.
6 Righteousness guards the way of integrity, but wickedness overthrows the sinner.
Chilungamo chimateteza munthu wangwiro, koma tchimo limagwetsa munthu wochimwa.
7 There are some who pretend to be rich, yet have nothing. There are some who pretend to be poor, yet have great wealth.
Wina amadziyesa kuti ndi wolemera chonsecho alibe kanthu kalikonse; munthu wina amaoneka ngati wosauka chonsecho ali ndi chuma chambiri.
8 The ransom of a man's life is his riches, but the poor hear no threats.
Chuma cha munthu wolemera chitha kuwombola moyo wake, koma munthu wosauka amamva chidzudzulo.
9 The light of the righteous shines brightly, but the lamp of the wicked is snuffed out.
Nyale ya munthu wolungama ndi yokondweretsa, koma nyale ya munthu woyipa imazimitsidwa.
10 Pride only breeds quarrels, but with ones who take advice is wisdom.
Chipongwe chosamalabadirako za anthu ena chimadzetsa mikangano, koma womva malangizo a anzawo ndiwo ali ndi nzeru.
11 Wealth gained dishonestly dwindles away, but he who gathers by hand makes it grow.
Chuma chochipeza mofulumira chidzatha pangʼonopangʼono koma chuma chosonkhanitsidwa pangʼonopangʼono chidzachulukirachulukira.
12 Hope deferred makes the heart sick, but when longing is fulfilled, it is a tree of life.
Chinthu chochiyembekezera chikalephereka chimalefula mtima, koma chinthu chochilakalaka chikachitikadi chimakhala ngati mtengo wamoyo.
13 Whoever despises instruction will pay for it, but he who respects a command will be rewarded.
Amene amanyoza malangizo adzawonongeka, koma amene amasamala lamulo amalandira mphotho.
14 The teaching of the wise is a spring of life, to turn from the snares of death.
Malangizo a munthu wanzeru ali ngati kasupe wamoyo; amathandiza munthu kuti asakondwe mu msampha wa imfa.
15 Good understanding brings favor; but the way of the unfaithful leads to calamity.
Munthu wa nzeru zabwino amapeza kuyanja pakati pa anthu, koma munthu wosakhulupirika adzawonongeka.
16 Every prudent man acts from knowledge, but a fool exposes folly.
Munthu wochenjera amachita zinthu mwanzeru, koma chitsiru chimaonetsa poyera uchitsiru wake.
17 A wicked messenger falls into trouble, but a trustworthy envoy gains healing.
Wamthenga woyipa amagwetsa anthu mʼmavuto, koma nthumwi yodalirika imabweretsa mtendere.
18 Poverty and shame come to him who refuses discipline, but he who heeds correction shall be honored.
Wokana mwambo adzasauka ndi kunyozedwa, koma wosamala chidzudzulo adzalemekezedwa.
19 Longing fulfilled is sweet to the soul, but fools detest turning from evil.
Chinthu chochilakalaka chikachitika chimasangalatsa mtima, koma zitsiru zimadana ndi kuleka zoyipa.
20 One who walks with wise men grows wise, but a companion of fools suffers harm.
Woyenda ndi anthu anzeru nayenso adzakhala wanzeru; koma woyenda ndi zitsiru adzapwetekeka.
21 Misfortune pursues sinners, but prosperity rewards the righteous.
Choyipa chitsata mwini, koma wochita zolungama adzalandira mphotho yabwino.
22 A good man leaves an inheritance to his children's children, but the wealth of the sinner is stored for the righteous.
Munthu wabwino amasiyira zidzukulu zake cholowa, koma chuma cha munthu wochimwa amachilandira ndi olungama.
23 An abundance of food is in poor people's fields, but injustice sweeps it away.
Tsala la munthu wosauka limalola chakudya chambiri, koma anthu opanda chilungamo amachilanda.
24 One who spares the rod hates his son, but one who loves him is careful to discipline him.
Amene sakwapula mwana wake, ndiye kuti amamuda, koma wokonda mwana wake sazengereza kumulanga.
25 The righteous one eats to the satisfying of his soul, but the belly of the wicked goes hungry.
Munthu wolungama amakhala ndi zakudya zoti adye nʼkukhuta, koma mʼmimba mwa munthu woyipa mumakhala pululu ndi njala.

< Proverbs 13 >