< Numbers 33 >

1 These are the journeys of the children of Israel, when they went forth out of the land of Egypt by their armies under the hand of Moses and Aaron.
Malo otsatirawa ndi omwe Aisraeli anayima pa maulendo awo atatuluka mʼdziko la Igupto mʼmagulu awo motsogozedwa ndi Mose ndi Aaroni.
2 Moses wrote their goings out according to their journeys by the commandment of YHWH: and these are their journeys according to their goings out.
Mose analemba malo amene anayambira maulendo awo molamulidwa ndi Yehova. Maulendo awo ndi malo omwe anayambira ndi awa:
3 They traveled from Rameses in the first month, on the fifteenth day of the first month; on the next day after the Passover the children of Israel went out triumphantly in the sight of all the Egyptians,
Aisraeli ananyamuka kuchokera ku Ramesesi pa tsiku la 15 la mwezi woyamba, itangotha Paska. Iwo anatuluka nayenda molimba mtima Aigupto onse akuona,
4 while the Egyptians were burying all their firstborn, whom YHWH had struck among them: on their gods also YHWH executed judgments.
pamene ankayika maliro a ana awo oyamba kubadwa, omwe Yehova anawakantha pakati pawo chifukwa Yehova anaweruza milungu yawo.
5 The children of Israel traveled from Rameses, and camped in Succoth.
Aisraeli atachoka ku Ramesesi, anamanga misasa yawo ku Sukoti.
6 They traveled from Succoth, and camped in Etham, which is in the edge of the wilderness.
Atachoka ku Sukoti anakamanga misasa yawo ku Etamu, mʼmbali mwa chipululu.
7 They traveled from Etham, and turned back to Pihahiroth, which is before Baal Zephon: and they camped before Migdol.
Ndipo atachoka ku Etamu, anabwerera ku Pihahiroti, kummawa kwa Baala-Zefoni, ndipo anamanga misasa yawo pafupi ndi Migidoli.
8 They traveled from before Hahiroth, and passed through the midst of the sea into the wilderness: and they went three days' journey in the wilderness of Etham, and camped in Marah.
Atachoka ku Pihahiroti anadutsa mʼkati mwa nyanja kupita ku chipululu ndipo atayenda masiku atatu mʼchipululu cha Etamu, anamanga misasa yawo ku Mara.
9 They traveled from Marah, and came to Elim: and in Elim were twelve springs of water, and seventy palm trees; and they camped there.
Atachoka ku Mara anafika ku Elimu, kumene kunali akasupe a madzi khumi ndi awiri ndi mitengo ya migwalangwa 70 ndipo anamanga misasa yawo kumeneko.
10 They traveled from Elim, and camped by the Red Sea.
Atachoka ku Elimu anakamanga misasa yawo mʼmbali mwa Nyanja Yofiira.
11 They traveled from the Red Sea, and camped in the wilderness of Sin.
Atachoka ku Nyanja Yofiira anakamanga misasa yawo mʼchipululu cha Sini.
12 They traveled from the wilderness of Sin, and camped in Dophkah.
Atachoka ku chipululu cha Sini anakamanga ku Dofika.
13 They traveled from Dophkah, and camped in Alush.
Atachoka ku Dofika anakamanga misasa yawo ku Alusi.
14 They traveled from Alush, and camped in Rephidim, where there was no water for the people to drink.
Atachoka ku Alusi anakamanga misasa yawo ku Refidimu, kumene kunalibe madzi woti anthu ndi kumwa.
15 They traveled from Rephidim, and camped in the wilderness of Sinai.
Atachoka ku Refidimu anakamanga ku chipululu cha Sinai
16 They traveled from the wilderness of Sinai, and camped in Kibroth Hattaavah.
Atachoka ku chipululu cha Sinai anakamanga misasa yawo ku Kiburoti-Hataava.
17 They traveled from Kibroth Hattaavah, and camped in Hazeroth.
Atachoka ku Kiburoti-Hataava anakamanga misasa yawo ku Heziroti.
18 They traveled from Hazeroth, and camped in Rithmah.
Atachoka ku Heziroti anakamanga ku Ritima.
19 They traveled from Rithmah, and camped in Rimmon Perez.
Atachoka ku Ritima anakamanga ku Rimoni-Perezi.
20 They traveled from Rimmon Perez, and camped in Libnah.
Atachoka ku Rimoni-Perezi anakamanga ku Libina.
21 They traveled from Libnah, and camped in Rissah.
Atachoka ku Libina anakamanga ku Risa.
22 They traveled from Rissah, and camped in Kehelathah.
Atachoka ku Risa anakamanga ku Kehelata.
23 They traveled from Kehelathah, and camped in Mount Shepher.
Atachoka ku Kehelata anakamanga ku phiri la Seferi.
24 They traveled from Mount Shepher, and camped in Haradah.
Atachoka ku phiri la Seferi anakamanga ku Harada.
25 They traveled from Haradah, and camped in Makheloth.
Atachoka ku Harada anakamanga ku Mekheloti.
26 They traveled from Makheloth, and camped in Tahath.
Atachoka ku Mekheloti anakamanga ku Tahati.
27 They traveled from Tahath, and camped in Terah.
Atachoka ku Tahati anakamanga ku Tera.
28 They traveled from Terah, and camped in Mithkah.
Atachoka ku Tera anakamanga ku Mitika.
29 They traveled from Mithkah, and camped in Hashmonah.
Atachoka ku Mitika anakamanga ku Hasimona.
30 They traveled from Hashmonah, and camped in Moseroth.
Atachoka ku Hasimona anakamanga ku Moseroti.
31 They traveled from Moseroth, and camped in Bene Jaakan.
Atachoka ku Moseroti anakamanga ku Beni Yaakani.
32 They traveled from Bene Jaakan, and camped in Hor Haggidgad.
Atachoka ku Beni Yaakani anakamanga ku Hori-Hagidigadi.
33 They traveled from Hor Haggidgad, and camped in Jotbathah.
Atachoka ku Hori-Hagidigadi anakamanga ku Yotibata.
34 They traveled from Jotbathah, and camped in Abronah.
Atachoka ku Yotibata anakamanga ku Abirona.
35 They traveled from Abronah, and camped in Ezion Geber.
Atachoka ku Abirona anakamanga ku Ezioni-Geberi.
36 They traveled from Ezion Geber, and camped in the wilderness of Zin (that is, Kadesh).
Atachoka ku Ezioni-Geberi anakamanga ku Kadesi, mʼchipululu cha Zini chimene ndi Kadesi.
37 They traveled from Kadesh, and camped in Mount Hor, in the edge of the land of Edom.
Anachoka ku Kadesi ndi kukamanga ku phiri la Hori, mʼmalire mwa dziko la Edomu.
38 Aaron the priest went up into Mount Hor at the commandment of YHWH, and died there, in the fortieth year after the children of Israel had come out of the land of Egypt, in the fifth month, on the first day of the month.
Molamulidwa ndi Yehova, wansembe Aaroni anakwera ku phiri la Hori kumene anakamwalirira pa tsiku loyamba la mwezi wachisanu, mʼchaka cha makumi anayi, Aisraeli atatuluka mʼdziko la Igupto.
39 Aaron was one hundred twenty-three years old when he died in Mount Hor.
Aaroni anamwalira pa phiri la Hori ali ndi zaka 123.
40 The Canaanite, the king of Arad, who lived in the Negev in the land of Canaan, heard of the coming of the children of Israel.
Mfumu ya Akanaani ya ku Aradi yomwe inkakhala ku Negevi kummwera kwa Kanaani, inamva kuti Aisraeli akubwera.
41 They traveled from Mount Hor, and camped in Zalmonah.
Atachoka ku phiri la Hori anakamanga ku Zalimoni.
42 They traveled from Zalmonah, and camped in Punon.
Atachoka ku Zalimoni anakamanga ku Punoni.
43 They traveled from Punon, and camped in Oboth.
Atachoka ku Punoni anakamanga ku Oboti.
44 They traveled from Oboth, and camped in Iye Abarim, in the border of Moab.
Atachoka ku Oboti anakamanga ku Iye-Abarimu.
45 They traveled from Iyim, and camped in Dibon Gad.
Atachoka ku Iye-Abarimu anakamanga ku Diboni Gadi.
46 They traveled from Dibon Gad, and camped in Almon Diblathaim.
Atachoka ku Diboni Gadi anakamanga ku Alimoni-Dibulataimu.
47 They traveled from Almon Diblathaim, and camped in the mountains of Abarim, before Nebo.
Atachoka ku Alimoni-Dibulataimu anakamanga mʼmapiri a Abarimu, pafupi ndi Nebo.
48 They traveled from the mountains of Abarim, and camped in the plains of Moab by the Jordan at Jericho.
Atachoka ku mapiri a Abarimu anakamanga ku zigwa za Mowabu mʼmbali mwa Yorodani moyangʼanana ndi Yeriko.
49 They camped by the Jordan, from Beth Jeshimoth even to Abel Shittim in the plains of Moab.
Ali ku zigwa za Mowabu anamanga mʼmbali mwa Yorodani kuchokera ku Beti-Yesimoti mpaka ku Abeli-Sitimu.
50 YHWH spoke to Moses in the plains of Moab by the Jordan at Jericho, saying,
Pa zigwa za Mowabu, mʼmbali mwa Yorodani moyangʼanana ndi ku Yeriko, Yehova anawuza Mose kuti,
51 Speak to the children of Israel, and tell them, "When you pass over the Jordan into the land of Canaan,
“Nena kwa Aisraeli kuti, ‘Pamene muwoloka Yorodani kulowa mʼdziko la Kanaani,
52 then you shall drive out all the inhabitants of the land from before you, destroy all their stone idols, destroy all their molten images, and demolish all their high places.
mukathamangitse nzika zonse za mʼdzikomo pamaso panu. Mukawononge mafano awo onse a miyala ndi osula ndi malo awo achipembedzo.
53 You shall take possession of the land, and dwell in it; for I have given the land to you to possess it.
Mukalande dzikolo ndi kukhalamo chifukwa ndakupatsani dziko limenelo kuti mukhalemo.
54 You shall inherit the land by lot according to your families; to the more you shall give the more inheritance, and to the fewer you shall give the less inheritance: wherever the lot falls to any man, that shall be his. You shall inherit according to the tribes of your fathers.
Mukagawane dzikolo pochita maere monga mwa mafuko anu. Kwa omwe ali ambiri, cholowa chambiri, ndipo amene ali ocheperapo, chocheperanso. Chilichonse chimene chidzawagwere iwo mwa maere chidzakhala chawo. Mukaligawane monga mwa mafuko a makolo anu.
55 "But if you do not drive out the inhabitants of the land from before you, then those you let remain of them will be as pricks in your eyes and as thorns in your sides, and they will harass you in the land in which you dwell.
“‘Koma ngati simukathamangitsa nzika zimene zili mʼdzikomo, amene mukawalole kukhalamo adzakhala ngati zisonga mʼmaso mwanu ndi ngati minga mʼmbali mwanu. Adzakubweretserani mavuto mʼdziko limene mudzakhalemolo.
56 It shall happen that as I thought to do to them, so will I do to you."
Ndipo pamenepo ndidzachitira inu zomwe ndinaganiza kuwachitira iwowo.’”

< Numbers 33 >