< Luke 19 >
1 He entered and was passing through Jericho.
Yesu analowa mu Yeriko napitirira.
2 And look, there was a man named Zacchaeus. He was a chief tax collector, and he was rich.
Kunali munthu kumeneko dzina lake Zakeyu; iye anali mkulu wa wolandira msonkho ndipo anali wolemera.
3 He was trying to see who Jesus was, and could not because of the crowd, because he was short.
Iye ankafuna kuona Yesu kuti ndani, koma pokhala wamfupi sanathe chifukwa cha gulu la anthu.
4 He ran on ahead, and climbed up into a sycamore tree to see him, for he was to pass that way.
Choncho iye anathamangira patsogolo ndipo anakwera mu mtengo wamkuyu kuti amuone Iye, pakuti Yesu ankadutsa njira imeneyo.
5 And as he came to the place, looking up, Jesus saw him, and said to him, "Zacchaeus, hurry and come down, for today I must stay at your house."
Yesu atafika pa malopo, anayangʼana mmwamba ndipo anati kwa iye, “Zakeyu, tsika msangamsanga. Ine ndiyenera kukhala mʼnyumba mwako lero.”
6 He hurried, came down, and received him joyfully.
Ndipo nthawi yomweyo anatsika ndipo anamulandira mosangalala.
7 And when they saw it, they all murmured, saying, "He has gone in to lodge with a man who is a sinner."
Anthu onse ataona zimenezi anayamba kungʼungʼudza, nati, “Iye akupita kuti akakhale mlendo wa wochimwa.”
8 And Zacchaeus stood and said to the Lord, "Look, Lord, half of my goods I give to the poor. If I have wrongfully exacted anything of anyone, I restore four times as much."
Koma Zakeyu anayimirira ndipo anati kwa Ambuye, “Taonani Ambuye! Theka la chuma changa ndipereka kwa osauka ndipo ngati ndinamubera wina aliyense pa chilichonse, ndidzamubwezera mochulukitsa kanayi.”
9 Jesus said to him, "Today, salvation has come to this house, because he also is a son of Abraham.
Yesu anati kwa iye, “Lero chipulumutso chafika mʼnyumba ino, chifukwa munthu uyu nayenso ndi mwana wa Abrahamu.
10 For the Son of Man came to seek and to save that which was lost."
Pajatu Mwana wa Munthu anabwera kudzafunafuna ndi kupulumutsa chotayikacho.”
11 As they heard these things, he went on and told a parable, because he was near Jerusalem, and they supposed that the Kingdom of God would be revealed immediately.
Pamene iwo ankamvera izi, Iye anapitiriza kuwawuza fanizo, chifukwa Iye anali kufupi ndi Yerusalemu ndipo anthu ankaganiza kuti ufumu wa Mulungu ukanaoneka nthawi yomweyo.
12 He said therefore, "A certain nobleman went into a far country to receive for himself a kingdom, and to return.
Iye anati, “Munthu wa banja laufumu anapita ku dziko lakutali kukadzozedwa ufumu ndipo kenaka abwerenso kwawo.
13 He called ten servants of his, and gave them ten mina coins, and told them, 'Conduct business until I come.'
Tsono iye anayitana antchito ake khumi ndi kuwapatsa ndalama khumi. Iye anati, ‘Gwiritsani ntchito ndalama izi mpaka nditabwerera.’
14 But his citizens hated him, and sent an envoy after him, saying, 'We do not want this man to reign over us.'
“Koma anthu ake anamuda ndipo anatuma nthumwi pambuyo pake kukanena kuti, ‘Sitikufuna munthuyu kuti akhale mfumu yathu.’
15 "It happened when he had come back again, having received the kingdom, that he commanded these servants, to whom he had given the money, to be called to him, that he might know what they had gained by conducting business.
“Iye analandira ufumuwo ngakhale zinali zotero, ndipo anabwerera kwawo. Kenaka iye anatumiza uthenga kwa antchito ake amene anawapatsa ndalama aja, ndi cholinga chakuti adziwe chimene anapindula nazo.
16 The first came before him, saying, 'Lord, your mina has made ten more minas.'
“Woyamba anabwera ndipo anati, ‘Bwana ndalama zanu zapindula khumi zina.’
17 "And he said to him, 'Well done, good servant. Because you were faithful with very little, you will have authority over ten cities.'
“Bwana wakeyo anayankha kuti, Wachita bwino wantchito wabwino. ‘Chifukwa wakhulupirika pa zinthu zazingʼono, lamulira mizinda khumi.’
18 "The second came, saying, 'Your mina, Lord, has made five minas.'
“Wachiwiri anabwera ndipo anati, ‘Bwana, ndalama zanu zapindula zisanu zina.’
19 "So he said to him, 'And you are to be over five cities.'
“Bwana anayankha kuti, ‘Iwe lamulira mizinda isanu.’
20 Another came, saying, 'Lord, look, your mina, which I kept laid away in a handkerchief,
“Kenaka wantchito wina anabwera ndipo anati, ‘Bwana, ndalama yanu nayi; ine ndinayibisa ndi kuyisunga mʼkansalu.
21 for I feared you, because you are an exacting man. You take up that which you did not lay down, and reap that which you did not sow.'
Ine ndimakuopani, chifukwa ndinu munthu wowuma mtima. Inu mumatenga chimene simunachiyike ndi kukolola chimene simunadzale.’
22 "He said to him, 'Out of your own mouth will I judge you, you wicked servant. You knew that I am an exacting man, taking up that which I did not lay down, and reaping that which I did not sow.
“Bwana wake anayankha kuti, ‘Ine ndikukuweruza iwe ndi mawu ako omwewo. Ndiwe wantchito woyipa. Kani umadziwa kuti ndine munthu wowuma mtima ndi wotenga chimene sindinasungitse, ndi kukolola chimene sindinadzale?
23 Then why did you not deposit my money in the bank, and at my coming, I might have earned interest on it?'
Nanga nʼchifukwa chiyani sunasungitse ndalama yanga, kuti ine pobwera, ndidzayitenge ndi chiwongoladzanja?’
24 He said to those who stood by, 'Take the mina away from him, and give it to him who has the ten minas.'
“Ndipo iye anawuza amene anayimirira pafupi kuti, ‘Tengani ndalama yake ndi kumupatsa amene ali ndi ndalama khumiyo!’”
25 "They said to him, 'Lord, he has ten minas.'
Iwo anati, “Bwana iyeyu ali nazo kale khumi!”
26 'For I tell you that to everyone who has, will more be given; but from him who does not have, even that which he has will be taken away.
Iye anayankha kuti, “Ndikukuwuzani kuti, aliyense amene ali nazo, adzapatsidwa zambiri, koma amene alibe, adzalandidwa ngakhale chimene ali nacho.
27 But bring those enemies of mine who did not want me to reign over them here, and kill them before me.'"
Tsono adani anga aja amene sankafuna kuti ndikhale mfumu yawo, abweretseni pano ndi kuwapha ine ndikuona.”
28 Having said these things, he went on ahead, going up to Jerusalem.
Yesu atatha kunena izi, anayendabe kupita ku Yerusalemu.
29 It happened, when he drew near to Bethphage and Bethany, at the mountain that is called Olivet, he sent two of the disciples,
Iye atayandikira ku Betifage ndi Betaniya pa phiri lotchedwa Olivi, Iye anatuma awiri a ophunzira nati kwa iwo,
30 saying, "Go your way into the village on the other side, in which, as you enter, you will find a colt tied, whereon no one ever yet sat. Untie it, and bring it.
“Pitani mʼmudzi uli patsogolo panu, mukakalowa mʼmudzimo, mukapeza mwana wabulu womangiriridwa amene wina aliyense sanakwerepo. Mukamumasule ndi kubwera naye kuno.
31 If anyone asks you, 'Why are you untying it?' say to him: 'Because the Lord needs it.'"
Ngati wina aliyense akakufunsani kuti, ‘Nʼchifukwa chiyani mukumumasula mwana buluyo?’ Mukamuwuze kuti, ‘Ambuye akumufuna.’”
32 Those who were sent went away, and found things just as he had told them.
Otumidwawo anapita nakamupeza mwana wabulu monga momwe Yesu anawawuzira.
33 As they were untying the colt, its owners said to them, "Why are you untying the colt?"
Pamene ankamasula mwana wabuluyo, eni ake anawafunsa kuti, “Nʼchifukwa chiyani mukumasula mwana wabuluyo?”
34 They said, "Because the Lord needs it."
Iwo anayankha kuti, “Ambuye akumufuna.”
35 They brought it to Jesus. They threw their cloaks on the colt, and set Jesus on them.
Iwo anabweretsa buluyo kwa Yesu, naponya zovala zawo pa bulupo ndi kumukwezapo Yesu.
36 As he went, they spread their cloaks in the way.
Pamene ankapita, anthu anayala zovala zawo mu msewu.
37 As he was now getting near, at the descent of the Mount of Olives, the whole crowd of the disciples began to rejoice and praise God with a loud voice for all the mighty works which they had seen,
Iye atafika pafupi ndi pamene msewu umatsikira ku phiri la Olivi, gulu lonse la ophunzira linayamba kuyamika Mulungu mwachimwemwe ndi mawu ofuwula chifukwa cha zodabwitsa zonse anaziona.
38 saying, "Blessed is the King who comes in the name of the Lord. Peace in heaven, and glory in the highest."
“Yodala mfumu imene ikubwera mʼdzina la Ambuye!” “Mtendere kumwamba ndi ulemerero mmwambamwamba!”
39 Some of the Pharisees from the crowd said to him, "Teacher, rebuke your disciples."
Ena mwa Afarisi mʼgulumo anati kwa Yesu, “Aphunzitsi, adzudzuleni ophunzira anu!”
40 He answered them, "I tell you that if these were silent, the stones would cry out."
Iye anayankha kuti, “Ine ndikukuwuzani kuti, ngati atakhala chete, miyala idzafuwula.”
41 When he drew near, he saw the city and wept over it,
Iye atayandikira ku Yerusalemu ndi kuona mzindawo, anawulirira
42 saying, "If you, even you, had known today the things that make for peace. But now, they are hidden from your eyes.
nati, “Iwe ukanadziwa lero lino zinthu zokubweretsera mtendere, koma tsopano zabisikira maso ako.
43 For the days will come on you, when your enemies will throw up a barricade against you, surround you, hem you in on every side,
Pakuti masiku adzabwera pamene adani ako adzamanga mitumbira yankhondo nakuzungulira, nadzakutsekereza mbali zonse.
44 and will dash you and your children within you to the ground. They will not leave in you one stone on another, because you did not know the time of your visitation."
Iwo adzakugwetsera pansi, iwe, ana ako onse a mʼkati mwako. Iwo sadzasiya mwa iwe mwala wina pa unzake, chifukwa sunazindikire nthawi ya kubwera kwa Mulungu.”
45 And he entered into the temple, and began to drive out those who were selling and buying in it,
Kenaka Iye analowa mʼdera la Nyumba ya Mulungu ndi kuyamba kutulutsa kunja amene amachita malonda.
46 saying to them, "It is written, 'And my house will be a house of prayer,' but you have made it a 'den of robbers'."
Iye anawawuza kuti, “Zinalembedwa kuti Nyumba yanga idzakhala nyumba ya mapemphero, koma inu mwayisadutsa phanga la achifwamba.”
47 He was teaching daily in the temple, but the chief priests and the scribes and the leaders among the people sought to destroy him.
Tsiku lililonse amaphunzitsa mʼNyumba ya Mulungu. Koma akulu a ansembe, aphunzitsi amalamulo ndi atsogoleri pakati pa anthu amayesetsa kuti amuphe.
48 They could not find what they might do, for all the people hung on to every word that he said.
Komabe iwo sanathe kupeza njira ina iliyonse kuti achite izi, chifukwa anthu onse anakhulupirira mawu ake.