< Lamentations 3 >

1 I am the man that has seen affliction by the rod of his wrath.
Ine ndine munthu amene ndaona masautso ndi ndodo ya ukali wake.
2 He has led me and caused me to walk in darkness, and not in light.
Wandipititsa kutali ndipo wandiyendetsa mu mdima osati mʼkuwala;
3 Surely against me he turns his hand again and again all the day.
zoonadi anandikantha ndi dzanja lake mobwerezabwereza tsiku lonse.
4 My flesh and my skin he has made old; he has broken my bones.
Wakalambitsa khungu langa ndi mnofu wanga, ndipo waphwanya mafupa anga.
5 He has built against me, and surrounded me with bitterness and hardship.
Wandizinga ndi kundizungulira ndi zowawa ndi zolemetsa.
6 He has made me to dwell in dark places, like those that have been long dead.
Wandikhazika mu mdima ngati amene anafa kale.
7 He has walled me in, so I can't escape; he has made my chains heavy.
Wandimangira khoma kotero kuti sindingathawe, wandimanga ndi maunyolo.
8 Yes, when I cry, and call for help, he shuts out my prayer.
Ngakhale pamene ndifuwula kapena kupempha chithandizo, amakana pemphero langa.
9 He has walled up my ways with cut stone; he has made my paths crooked.
Wanditsekera njira yanga ndi miyala yosema; ndipo wakhotetsa tinjira tanga.
10 He is to me as a bear lying in wait, as a lion in hiding.
Wandidikirira ngati chimbalangondo, wandibisalira ngati mkango.
11 He has obstructed my path, and torn me in pieces; he has made me desolate.
Wandikokera pambali ndi kundingʼambangʼamba, ndipo wandisiya wopanda thandizo.
12 He has bent his bow, and set me as a mark for the arrow.
Wakoka uta wake ndipo walunjikitsa mivi yake pa ine.
13 He has caused the arrows of his quiver to pierce my inward parts.
Walasa mtima wanga ndi mivi ya mʼphodo mwake.
14 I have become a laughingstock to all peoples, and their song all the day.
Ndinakhala choseketsa cha anthu anga onse; amandinyodola mʼnyimbo zawo tsiku lonse.
15 He has filled me with bitterness, he has given me in full measure wormwood.
Wandidyetsa zowawa ndipo wandimwetsa ndulu.
16 He has also broken my teeth with gravel; he has pressed me down in the dust.
Wathyola mano anga ndi miyala; wandiviviniza mʼfumbi;
17 You have removed my soul far away from peace; I have forgotten what prosperity is.
Wandichotsera mtendere; ndayiwala kuti kupeza bwino nʼchiyani.
18 And I said, "My strength and my hope has perished from YHWH."
Choncho ndikuti, “Ulemerero wanga wachoka ndi zonse zimene ndimayembekeza kwa Yehova.”
19 Remember my affliction and my misery, the wormwood and the gall.
Kukumbukira masautso anga ndi kusowa pokhala, zili ngati zowawa ndi ndulu.
20 My soul considers them, and is depressed.
Ine ndikuzikumbukira bwino izi, ndipo moyo wanga wathedwa mʼkati mwanga.
21 But this I call to my mind; therefore I have hope:
Komabe ndimakumbukira zimenezi, nʼchifukwa chake ndili ndi chiyembekezo.
22 YHWH's faithful love does not cease; his compassion does not fail.
Ife sitinawonongekeretu chifukwa chikondi cha Yehova ndi chachikulu, ndi chifundo chake ndi chosatha.
23 They are new every morning; great is your faithfulness.
Zimaoneka zatsopano mmawa uliwonse; kukhulupirika kwanu nʼkwakukulu.
24 "YHWH is my portion," says my soul, "therefore I will hope in him."
Mu mtima mwanga ndimati, “Yehova ndiye zanga zonse; motero ndimamuyembekezera.”
25 YHWH is good to those who wait for him, to the soul that seeks him.
Yehova ndi wabwino kwa amene amayembekezera Iye, kwa munthu amene amafunafuna Iyeyo;
26 It is good that a man should hope and quietly wait for the salvation of YHWH.
nʼkwabwino kudikira chipulumutso cha Yehova modekha.
27 It is good for a man that he bear the yoke while he is young.
Nʼkwabwino kuti munthu asenze goli pamene ali wamngʼono.
28 Let him sit alone and keep silence when he is disciplining him.
Akhale chete pa yekha, chifukwa Yehova wamusenzetsa golilo.
29 Let him put his mouth to the dust, there may yet be hope.
Abise nkhope yake mʼfumbi mwina chiyembekezo nʼkukhalapobe.
30 Let him give his cheek to him who strikes him; let him be filled with insults.
Apereke tsaya lake kwa iye amene angamumenye, ndipo amuchititse manyazi.
31 For YHWH will not reject forever.
Chifukwa Ambuye satayiratu anthu nthawi zonse.
32 For though he may cause grief, yet he will have compassion according to the abundance of his loving kindness.
Ngakhale amabweretsa zowawa, Iye adzawachitira chifundo, chifukwa chikondi chake ndi chosatha.
33 For he is not predisposed to bring affliction or suffering to human beings.
Pakuti sabweretsa masautso mwadala, kapena zowawa kwa ana a anthu.
34 To crush under foot all the prisoners of the earth;
Kuphwanya ndi phazi a mʼndende onse a mʼdziko,
35 to deprive a man of justice before the face of the Most High,
kukaniza munthu ufulu wake pamaso pa Wammwambamwamba,
36 to subvert a man in his cause, YHWH does not approve.
kumana munthu chiweruzo cholungama— kodi Ambuye saona zonsezi?
37 Who can speak a thing and have it come to pass, unless YHWH has commanded it?
Kodi ndani angayankhule zinthu nʼkuchitika ngati Ambuye sanavomereze?
38 Doesn't both calamity and good come out of the mouth of the Most High?
Kodi zovuta ndi zabwino sizituluka mʼkamwa mwa Wammwambamwamba?
39 Why does a living man complain, a man for the punishment of his sins?
Kodi nʼchifukwa chiyani munthu aliyense wamoyo amadandaula akalangidwa chifukwa cha machimo ake?
40 Let us examine and search our ways, and return to YHWH.
Tiyeni tisanthule ndi kuyesa njira zathu, ndipo tiyeni tibwerere kwa Yehova.
41 Let us lift up our heart with our hands to God in the heavens.
Tiyeni tikweze mitima yathu ndi manja athu kwa Mulungu kumwamba ndipo tinene kuti:
42 We have transgressed and have rebelled, and you have not forgiven.
“Ife tachimwa ndi kuwukira ndipo inu simunakhululuke.
43 You have covered yourself with anger and pursued us; you killed without sparing.
“Mwadzikuta ndi mkwiyo ndi kutilondola ndipo mwatitha mopanda chifundo.
44 You have covered yourself with a cloud, so that no prayer can pass through.
Mwadzikuta mu mtambo kotero mapemphero athu sakukufikani.
45 You have made us rubbish and refuse in the midst of the peoples.
Mwatisandutsa zinyatsi ndi zinyalala pakati pa mitundu ya anthu.
46 All our enemies have opened their mouth wide against us.
“Adani anthu atitsekulira pakamwa.
47 Fear and the pit have come on us, devastation and destruction.
Ife tadzazidwa ndi mantha pakuti tagwa mʼdzenje, tapasuka ndi kuwonongedwa.”
48 Streams of tears run down from my eyes because of the destruction of the daughter of my people.
Misozi mʼmaso mwanga ikungoti mbwembwembwe chifukwa anthu anga akuwonongedwa.
49 My tears flow and do not cease, without respite,
Misozi idzatsika kosalekeza, ndipo sidzasiya,
50 until YHWH looks down and sees from heaven.
mpaka Yehova ayangʼane pansi kuchokera kumwamba ndi kuona.
51 My eyes bring my soul grief, because of all the daughters of my city.
Mtima wanga ukupweteka poona zimenezi chifukwa cha akazi onse a mu mzinda.
52 They have chased me relentlessly like a bird, those who are my enemies without cause.
Akundisaka ngati mbalame, amene anali adani anga, popanda chifukwa.
53 They have cut off my life in a pit, and have cast a stone on me.
Ayesa kundipha pondiponya mʼdzenje ndi kundiponya miyala;
54 Waters flowed over my head; I said, 'I am finished.'
madzi anamiza mutu wanga ndipo ndinkaganiza kuti imfa yayandikira.
55 I called on your name, YHWH, out of the depths of the pit.
Ndinayitana dzina lanu Inu Yehova, kuchokera mʼdzenje lozama.
56 You heard my voice; do not hide your ear at my sighs, to my cry.
Inu munamva kudandaula kwanga. “Mundimvere kulira kwanga kopempha thandizo.”
57 You drew near in the day that I called on you; you said, "Do not be afraid."
Munafika pafupi pamene ndinakuyitanani, ndipo munati, “Usaope.”
58 YHWH, you have taken up the case for my soul; you have redeemed my life.
Inu Ambuye munandiwombola ku mlandu wanga; munapulumutsa moyo wanga.
59 You have seen, YHWH, the wrong done to me; judge my case.
Yehova, mwaona zoyipa zimene andichitira. Mundiweruzire ndinu!
60 You have seen all their vengeance and all their plots against me.
Mwaona kuzama kwa kubwezera kwawo, chiwembu chawo chonse pa ine.
61 You have heard their insults, YHWH, and all their plots against me.
Inu Yehova mwamva kunyoza kwawo, chiwembu chawo chonse pa ine,
62 The lips of those that rose up against me, and their plots against me all day long.
manongʼonongʼo a adani anga ondiwukira ine tsiku lonse.
63 Look their sitting down, and their rising up; I am their mocking song.
Tawaonani! Kaya ali pansi kapena kuyimirira, akundinyoza mu nyimbo zawo.
64 You will render to them what they deserve, YHWH, according to the work of their hands.
Inu Yehova, muwabwezere chowayenera, chifukwa cha zimene manja awo achita.
65 You will give them hardness of heart as your curse to them.
Phimbani mitima yawo, ndipo matemberero anu akhale pa iwo!
66 You will pursue them in anger, and destroy them from under the heavens of YHWH.
Muwalondole mwaukali ndipo muwawonongeretu pa dziko lapansi.

< Lamentations 3 >