< Judges 7 >

1 Then Jerubbaal, who is Gideon, and all the people who were with him, rose up early, and camped beside the spring of Harod. And the camp of Midian was on the north side of them, by the hill of Moreh, in the valley.
Yeru-Baala (Gideoni) ndi anthu ake onse anadzuka mʼmamawa nakamanga misasa pambali pa kasupe ku Harodi. Misasa ya Amidiyani inali mʼchigwa kumpoto kwa phiri la More.
2 YHWH said to Gideon, "The people who are with you are too many for me to give the Midianites into their hand, lest Israel vaunt themselves against me, saying, 'My own hand has saved me.'
Yehova anati kwa Gideoni, “Anthu uli nawowa andichulukira kwambiri kuti ndigonjetse Amidiyani chifukwa Aisraeli angamadzitukumule pamaso panga ndi kumanena kuti, ‘Tadzipulumutsa ndi mphamvu zathu.’
3 Now therefore proclaim in the ears of the people, saying, 'Whoever is fearful and trembling, let him return and depart from Mount Gilead.' There returned of the people twenty-two thousand; but ten thousand remained.
Tsono lengeza kwa anthu kuti, ‘Aliyense amene akuchita mantha ndi kunjenjemera abwerere kwawo, ndipo achoke kuno ku phiri la Giliyadi.’” Choncho anthu 22,000 anachoka, ndipo anatsalira anthu 10,000.
4 YHWH said to Gideon, "The people are yet too many; bring them down to the water, and I will try them for you there: and it shall be, that of whom I tell you, This shall go with you, the same shall go with you; and of whoever I tell you, This shall not go with you, the same shall not go.
Koma Yehova anawuza Gideoni kuti, “Anthuwa achulukabe. Uwatenge upite nawo ku mtsinje ndipo ndikawayesa kumeneko mʼmalo mwako. Ndikadzanena kuti, ‘Uyu apite nawe’ adzapita nawe; koma ndikanena kuti ‘Uyu asapite nawe,’ sadzapita nawe.”
5 So he brought down the people to the water. And YHWH said to Gideon, "Everyone who laps of the water with his tongue, as a dog laps, you shall put to one side; and everyone who gets down on his knees to drink with hand to mouth shall be on the other side."
Choncho Gideoni anatenga anthuwo ndi kupita nawo ku madzi. Kumeneko Yehova anamuwuza kuti, “Amene amwe madzi mokhathira ndi manja ngati galu uwayike pawokha, ndipo amene amwe atagwada pansi uwayikenso pawokha.”
6 The number of those who lapped with their tongues was three hundred men, but all the rest of the people got down on their knees to drink water.
Ndipo anthu 300 anamwa mokhathira, pamene ena onse anagwada pansi pakumwa.
7 YHWH said to Gideon, "By the three hundred men who lapped will I save you, and deliver the Midianites into your hand; and let all the people go every man to his home."
Yehova anati kwa Gideoni, “Ndi anthu 300 amene anamwa madzi mokhathira ndi manja awo ndidzakupulumutsani ndipo ndidzapereka Amidiyani mʼmanja mwanu. Koma anthu ena onse apite ku nyumba kwawo.”
8 So the people took food in their hand, and their trumpets; and he sent all the men of Israel every man to his tent, but retained the three hundred men. And the camp of Midian was beneath him in the valley.
Choncho analola anthu ena onse kuti apite ku nyumba zawo kupatula anthu 300 osankhika aja. Iwowa anatenga zakudya ndi malipenga a anthuwo. Ndipo misasa ya ankhondo Amidiyani inali kumunsi kwa chigwa.
9 It happened the same night, that YHWH said to him, "Arise, get down into the camp; for I have delivered it into your hand.
Usiku umenewo Yehova anati kwa Gideoni, “Dzuka, pita kachite nkhondo ku misasayo, chifukwa ndayipereka mʼmanja mwako.
10 But if you fear to go down, go with Purah your servant down to the camp:
Ngati ukuopa, upite ku msasako ndi Pura wantchito wako,
11 and you shall hear what they say; and afterward will your hands be strengthened to go down into the camp." Then he went down with Purah his servant to the outermost part of the armed men who were in the camp.
ndipo ukamvere zimene akunena ndipo pambuyo pake udzalimba mtima ndi kupita kukayithira nkhondo misasayo.” Choncho iye ndi wantchito wake Pura anapita kumbali ina ya msasawo kumene kunali ankhondo.
12 And Midian, Amalek, and all the Kedemites lay along in the valley as numerous as locusts; and their camels were without number, as numerous as the sand which is on the seashore.
Amidiyani, Aamaleki ndi anthu ena onse akummawa anadzaza chigwa chonse ngati dzombe. Ngamira zawo zinali zambiri zosawerengeka ngati mchenga wa mʼmbali mwa nyanja.
13 When Gideon had come, look, there was a man telling a dream to his friend; and he said, "Look, I had a dream, and look, a cake of barley bread tumbled into the camp of Midian, and came to the tent, and struck it so that it fell, and turned it upside down, so that the tent collapsed."
Gideoni atafika anangomva munthu wina akuwuza mnzake maloto ake kuti, “Ine ndinalota nditaona dengu la buledi wa barele likugubuduzika kupita ku misasa ya Amidiyani. Litafika linawomba tenti moti inagwa ndi kuphwasukaphwasuka.”
14 His friend answered, "This is nothing less than the sword of Gideon the son of Joash, a man of Israel. Into his hand God has delivered Midian, and all the army."
Ndipo mnzakeyo anamuyankha kuti, “Iyi ndi nkhondo ya Gideoni mwana wa Yowasi, wa ku Israeli. Mulungu wapereka Amidiyani pamodzi ndi ankhondo ake onse mʼdzanja mwake.”
15 It was so, when Gideon heard the telling of the dream, and its interpretation, that he worshiped, and he returned into the camp of Israel, and said, "Get up, for YHWH has delivered into your hand the army of Midian."
Gideoni atamva za malotowo ndi kumasulira kwake, anapembedza Mulungu. Kenaka anabwerera ku msasa wa Israeli nawawuza kuti, “Dzukani popeza Yehova wapereka msasa wa Midiyani mʼmanja mwanu.”
16 He divided the three hundred men into three companies, and he put into the hands of all of them trumpets, and empty pitchers, with torches within the pitchers.
Anawagawa anthu 300 aja magulu atatu, nawapatsa malipenga mʼmanja mwawo ndi mbiya zimene mʼkati mwake munali nsakali zoyaka.
17 He said to them, "Look at me, and do likewise. And look, when I come to the outermost part of the camp, it shall be that, as I do, so you shall do.
Anawuza anthuwo kuti, “Muzikayangʼana ine ndi kuchita zimene ndizikachita. Ndikakafika kumalire a msasa, mukachite zomwe ndikachita ine.
18 When I blow the trumpet, I and all who are with me, then you blow the trumpets also on every side of all the camp, and say, "For YHWH and for Gideon."
Ndikadzaliza lipenga ndi onse amene ali ndi ine, inunso mukalize malipenga kumbali zonse za misasa yonse ndi kufuwula kuti, ‘Lupanga la Yehova ndi la Gideoni.’”
19 So Gideon and the hundred men who were with him came to the outermost part of the camp in the beginning of the middle watch, when they had but newly set the watch: and they blew the trumpets, and broke in pieces the pitchers that were in their hands.
Choncho Gideoni pamodzi ndi amuna 100 omwe anali nawo anafika ku malire a msasa pakati pa usiku, alonda atangosinthana kumene. Iwo analiza malipenga awo ndi kuphwanya mbiya zimene zinali mʼmanja mwawo.
20 The three companies blew the trumpets, and broke the pitchers, and held the torches in their left hands, and the trumpets in their right hands with which to blow; and they called out, "The sword of YHWH and of Gideon.'"
Magulu awiri ena aja anayimbanso malipenga ndi kuswa mbiya zawo. Aliyense ananyamula nsakali ya moto ku dzanja lamanzere ndi lipenga ku dzanja lamanja ndipo anafuwula kuti, “Lupanga la Yehova ndi la Gideoni.”
21 They each stood in his place every man around the camp; and all the army ran; and they shouted, and put them to flight.
Aliyense anayima pa malo pake kuzungulira misasa. Ankhondo a mʼmisasa muja anadzuka nayamba kuthawa akufuwula.
22 They blew the three hundred trumpets, and YHWH set every man's sword against each other throughout the camp; and the army fled as far as Beth Shittah toward Zererah, as far as the border of Abel Meholah, by Tabbath.
Anthu 300 aja ataliza malipenga, Yehova anawasokoneza ankhondo a Midiyani aja motero kuti ankamenyana okhaokha. Ankhondowo anathawira ku Beti-Sita cha ku Zerera mpaka ku malire a Abeli-Mehola pafupi ndi Tabati.
23 The men of Israel were gathered together out of Naphtali, and out of Asher, and out of all Manasseh, and pursued after Midian.
Aisraeli a fuko la Nafutali, fuko la Aseri, ndi fuko lonse la Manase anayitanidwa, ndipo iwo anathamangitsa Amidiyaniwo.
24 Gideon sent messengers throughout all the hill country of Ephraim, saying, "Come down against Midian, and capture the waters, as far as Beth Barah, even the Jordan." So all the men of Ephraim were gathered together, and seized the waters as far as Beth Barah, even the Jordan.
Gideoni anatumiza amithenga ku dziko lonse la ku mapiri la Efereimu kukanena kuti, “Tsikani mumenyane ndi Amidiyani ndipo mulande madooko awo owolokera mpaka ku Beti-Bara.” Choncho anthu onse a fuko la Efereimu anasonkhana ndipo analanda madooko awo owolokera mpaka ku Betibaala.
25 They took the two princes of Midian, Oreb and Zeeb; and they killed Oreb at the rock of Oreb, and Zeeb they killed at the winepress of Zeeb, and pursued Midian. Then they brought the heads of Oreb and Zeeb to Gideon beyond the Jordan.
Iwo anagwiranso atsogoleri awiri a nkhondo a Amidiyani, Orebu ndi Zeebu. Anapha Orebu ku thanthwe la Orebu, koma Zeebu anamuphera ku malo ofinyira mphesa ku Zeebu pothamangitsa Amidiyani. Mitu ya Orebu ndi Zeebu anabwera nayo kwa Gideoni kutsidya kwa Yorodani.

< Judges 7 >