< Job 35 >

1 Moreover Elihu answered,
Ndipo Elihu anawonjeza kunena kuti,
2 "Do you think this to be your right, or do you say, 'My righteousness is more than God's,'
“Kodi mukuganiza kuti mukukhoza? Mukunena kuti, ‘Ndine wolungama pamaso pa Mulungu.’
3 That you ask, 'What advantage will it be to you? What profit shall I have, more than if I had sinned?'
Komanso inu mukufunsa kuti, ‘Kodi phindu langa nʼchiyani, ndipo ndimapeza chiyani ndikapanda kuchimwa?’
4 I will answer you, and your companions with you.
“Ine ndikufuna ndikuyankheni inu pamodzi ndi abwenzi anu omwe.
5 Look to the heavens, and see. See the skies, which are higher than you.
Yangʼanani kumwamba ndipo muone mitambo imene ili kutali ndi inuyo.
6 If you have sinned, what effect do you have against him? If your transgressions are multiplied, what do you do to him?
Inuyo mukachimwa, Iye zimamukhudza motani? Ngati machimo anu ndi ochuluka, zimenezo zimachita chiyani kwa Iye?
7 If you are righteous, what do you give him? Or what does he receive from your hand?
Ngati inu ndinu wolungama, mumamupatsa Iyeyo chiyani? Kapena Iye amalandira chiyani chochokera mʼdzanja lanu?
8 Your wickedness may hurt a man as you are, and your righteousness may profit a son of man.
Kuyipa kwanu kumangokhudza anthu ngati inuyo, ndipo chilungamo chanu chimakhudza anthu anzanu.
9 "By reason of the multitude of oppressions they cry out. They cry for help by reason of the arm of the mighty.
“Anthu akufuwula chifukwa cha kuzunzidwa; akufuna chithandizo kuti achoke pansi pa ulamuliro wa anthu amphamvu.
10 But none says, 'Where is God my Maker, who gives songs in the night,
Koma palibe amene akunena kuti, ‘Kodi ali kuti Mulungu, Mlengi wanga, amene amatisangalatsa nthawi ya usiku,
11 who teaches us more than the animals of the earth, and makes us wiser than the birds of the sky?'
amene amatiphunzitsa kupambana nyama za dziko lapansi ndipo amatipatsa nzeru kupambana mbalame zowuluka?’
12 There they cry, but none gives answer, because of the pride of evil men.
Iye sayankha pamene anthu akufuwulira kwa Iye chifukwa cha kudzikuza kwa anthu oyipa.
13 Surely God will not hear an empty cry, neither will Shaddai regard it.
Ndithu, Mulungu samva kupempha kwawo kopanda pake; Wamphamvuzonse sasamalira zimenezi.
14 How much less when you say you do not see him. The cause is before him, and you wait for him.
Ndipo ndi bodza lalikulu kunena kuti Iye saona zimene zikuchitika. Iye adzaweruza molungama ngati inu mutamudikira
15 But now, because he has not visited in his anger, neither does he greatly regard arrogance.
ndiye tsono popeza kuti ukali wake sukupereka chilango, zoyipa zambiri zimene anthu amachita,
16 Therefore Job opens his mouth with empty talk, and he multiplies words without knowledge."
abambo Yobu mumangoyankhula zopandapake, mukungochulukitsa mawu opanda nzeru.”

< Job 35 >