< Job 33 >

1 "However, Job, Please hear my speech, and listen to all my words.
“Koma tsopano, inu abambo Yobu chonde mverani mawu anga; mutcherere khutu zonse zimene ndinene.
2 See now, I have opened my mouth. My tongue has spoken in my mouth.
Tsopano ndiyamba kuyankhula; mawu anga ali pa msonga ya lilime langa.
3 My words shall utter the uprightness of my heart. That which my lips know they shall speak sincerely.
Mawu anga akuchokera mu mtima wolungama; pakamwa panga pakuyankhula zoonadi zimene ndikuzidziwa.
4 The Spirit of God has made me, and the breath of Shaddai gives me life.
Mzimu wa Mulungu wandiwumba, mpweya wa Wamphamvuzonse umandipatsa moyo.
5 If you can, answer me. Set your words in order before me, and stand forth.
Mundiyankhe ngati mungathe; konzekani tsopano kuti munditsutse.
6 Look, I am toward God even as you are. I am also formed out of the clay.
Ine ndili monga inu pamaso pa Mulungu; nanenso ndinachokera ku dothi.
7 Look, my terror shall not make you afraid, neither shall my pressure be heavy on you.
Musachite mantha ndipo musandiope ayi, Ine sindikupanikizani kwambiri ayi.
8 "Surely you have spoken in my hearing, I have heard the voice of your words, saying,
“Koma inu mwayankhula ine ndikumva, ndamva mawu anuwo onena kuti,
9 'I am clean, without disobedience. I am innocent, neither is there iniquity in me.
‘Ndine wolungama mtima ndi wopanda tchimo; ndine woyera mtima ndipo ndilibe cholakwa.
10 Look, he finds occasions against me. He counts me for his enemy.
Komatu Mulungu wapeza zifukwa zoti anditsutsire nazo; Iye akundiyesa ngati mdani wake.
11 He puts my feet in the stocks. He marks all my paths.'
Iyeyo wamanga mapazi anga mʼzigologolo, akulonda mayendedwe anga onse.’
12 "Look, I will answer you. In this you are not just, for God is greater than man.
“Koma ine ndi kuti kwa inu, inuyo simukukhoza pa zimenezi, pakuti Mulungu ndi wamkulu kupambana munthu.
13 Why do you strive against him, because he doesn't give account of any of his matters?
Chifukwa chiyani mukudandaula kwa Iye kuti sayankha mawu ena aliwonse a munthu?
14 For God speaks once, yes twice, though man pays no attention.
Pajatu Mulungu amayankhula mwa njira zosiyanasiyana, ngakhale munthu sazindikira zimenezi.
15 In a dream, in a vision of the night, when deep sleep falls on men, in slumbering on the bed;
Mʼmaloto, mʼmasomphenya usiku, pamene anthu ali mʼtulo tofa nato pamene akungosinza chabe pa bedi,
16 Then he opens the ears of men, and seals their instruction,
amawanongʼoneza mʼmakutu ndi kuwaopseza ndi machenjezo ake,
17 That he may withdraw man from his purpose, and hide pride from man.
kumuchotsa munthu ku zoyipa, ndi kuthetseratu kunyada kwake,
18 He keeps back his soul from the pit, and his life from perishing by the sword.
kumulanditsa munthu ku manda, kuti moyo wake usawonongeke ndi lupanga.
19 He is chastened also with pain on his bed, with continual strife in his bones;
“Mwina Mulungu amalanga munthu ndi matenda ndi ululu ali pa bedi pake, nthawiyo thupi lake lonse limangophwanya,
20 So that his life abhors bread, and his soul choicest food.
kuti asakhalenso ndi chilakolako cha chakudya, ndipo amanyansidwa ndi chakudya chabwino chomwe.
21 His flesh is so consumed away, that it can't be seen. His bones that were not seen stick out.
Thupi lake limawonda ndipo mafupa ake, omwe anali obisika, tsopano amaonekera poyera.
22 Yes, his soul draws near to the pit, and his life to the destroyers.
Munthuyo amayandikira ku manda, moyo wake umayandikira kwa amene amabweretsa imfa.
23 "If there is beside him an angel, an interpreter, one among a thousand, to show to man what is right for him;
“Koma patakhala mngelo ngati mthandizi, mmodzi mwa ambirimbiri oterewa, adzafotokoza zimene zili zoyenera,
24 then he is gracious to him, and says, 'Deliver him from going down to the pit, I have found a ransom.'
kudzamukomera mtima ndi kunena kuti, ‘Mupulumutseni kuti asapite ku manda; ine ndapeza cholowa mʼmalo mwa moyo wake,’
25 His flesh shall be fresher than a child's. He returns to the days of his youth.
pamenepo thupi lake lidzasanduka lasee ngati la mwana; ndipo adzabwezeretsedwanso kukhala ngati mʼmasiku a unyamata wake.
26 He prays to God, and he is favorable to him, so that he sees his face with joy. He restores to man his righteousness.
Akapemphera kwa Mulungu, iyeyo adzalandiridwa. Mulungu adzamulandira mwa chimwemwe ndipo adzamubwezeretsa pamalo ake oyamba.
27 He sings before men, and says, 'I have sinned, and perverted that which was right, and it did not profit me.
Ndipo adzabwera kwa anzake ndi kunena kuti, ‘Ndinachimwa ndipo sindinachite zolungama, koma sindinalangidwe koyenerana ndi kuchimwa kwanga.
28 He has redeemed my soul from going into the pit. My life shall see the light.'
Iye anapulumutsa moyo wanga kuti usapite ku manda, ndipo ndidzakhala ndi moyo ndi kuonanso kuwala kwa dzuwa.’
29 "Look, God works all these things, twice, yes three times, with a man,
“Mulungu amachita zonsezi kwa munthu kawirikawiri,
30 to bring back his soul from the pit, that he may be enlightened with the light of the living.
kupulumutsa moyo wa munthuyo ku manda, kuti athe kuonanso kuwala kwa moyo.
31 Mark well, Job, and listen to me. Hold your peace, and I will speak.
“Abambo Yobu, tcherani khutu ndipo mundimvere; khalani chete kuti ndiyankhule.
32 If you have anything to say, answer me. Speak, for I desire to justify you.
Ngati muli nʼchoti munene, ndiyankheni; yankhulani, pakuti ine ndikufuna mupezeke wolungama.
33 If not, listen to me. Hold your peace, and I will teach you wisdom."
Koma ngati sichoncho, mundimvere; khalani chete ndipo ine ndidzakuphunzitsani nzeru.”

< Job 33 >