< Job 32 >

1 So these three men ceased to answer Job, because he was righteous in his own eyes.
Tsono anthu atatuwa analeka kumuyankha Yobu, chifukwa chakuti iyeyo ankadziona kuti ndi wolungama.
2 Then the wrath of Elihu the son of Barakel, the Buzite, of the family of Ram, was kindled against Job. His wrath was kindled because he justified himself rather than God.
Koma Elihu, mwana wa Barakeli, wa fuko la Buzi, wa banja la Ramu, anapsera mtima kwambiri Yobu chifukwa choti Yobuyo anakana kuvomera kuti anachimwa ndi kuti Mulungu anakhoza pomulanga.
3 Also his wrath was kindled against his three friends, because they had found no answer, and yet had condemned Job.
Anapseranso mtima abwenzi ake atatu aja chifukwa sanapeze njira yomutsutsira Yobu, ngakhale iwo anamupeza kuti anali wolakwa.
4 Now Elihu had waited to speak to Job, because they were elder than he.
Tsono Elihu anadikira kuti ayankhule ndi Yobu chifukwa choti abwenziwo anali akuluakulu kupambana iyeyo.
5 When Elihu saw that there was no answer in the mouth of these three men, his wrath was kindled.
Koma Elihu ataona kuti anthu atatuwo analibe mawu oti ayankhulenso, iye anapsa mtima.
6 Elihu the son of Barakel the Buzite answered, "I am young, and you are very old; Therefore I held back, and did not dare show you my opinion.
Choncho Elihu mwana wa Barakeli wa fuko la Buzi anati: “Ine ndine wamngʼono, inuyo ndinu akuluakulu, nʼchifukwa chake ndimaopa, ndimachita mantha kuti ndikuwuzeni zimene ndimadziwa.
7 I said, 'Days should speak, and multitude of years should teach wisdom.'
Ndimaganiza kuti, ‘Ayambe ndi akuluakulu kuyankhula; anthu amvulazakale ndiwo amaphunzitsa nzeru.’
8 But there is a spirit in man, and the breath of Shaddai gives them understanding.
Koma mzimu wa Mulungu mwa munthu, mpweya wa Wamphamvuzonse, ndi umene umapereka nzeru zomvetsa zinthu.
9 It is not the great who are wise, nor the aged who understand justice.
Si okalamba amene ali ndi nzeru, si amvulazakale okha amene ali ndi nzeru zomvetsa zinthu zimene zili zoyenera.
10 Therefore I said, 'Listen to me; I also will show my opinion.'
“Nʼchifukwa chake ndikuti, ‘Mvereni; inenso ndikukuwuzani zimene ndikuzidziwa.’
11 "Look, I waited for your words, and I listened for your reasoning, while you searched out what to say.
Ndadikira nthawi yonseyi, ndimamvetsera mwachidwi zimene mumayankhula, pamene mumafunafuna mawu oti muyankhule,
12 Yes, I gave you my full attention, but there was no one who convinced Job, or who answered his words, among you.
ineyo ndinakumvetseranidi. Koma palibe ndi mmodzi yemwe wa inu amene anatsutsa Yobu; palibe aliyense wa inu amene anamuyankha mawu ake.
13 Beware lest you say, 'We have found wisdom, God may refute him, not man;'
Musanene kuti, ‘Ife tapeza nzeru; Mulungu ndiye amutsutse, osati munthu.’
14 for he has not directed his words against me; neither will I answer him with your speeches.
Koma Yobu sanayankhule motsutsana ndi ine, ndipo ine sindimuyankha monga mmene inu mwamuyankhira.
15 "They are amazed. They answer no more. They do not have a word to say.
“Iwo asokonezeka ndipo alibe choti ayankhulenso; mawu awathera.
16 Shall I wait, because they do not speak, because they stand still, and answer no more?
Kodi ine ndidikire chifukwa iwo sakuyankhula tsopano, pakuti angoyima phee wopanda yankho?
17 I also will answer my part, and I also will show my opinion.
Inenso ndiyankhulapo tsopano; nanenso ndinena zimene ndikudziwa.
18 For I am full of words. The spirit within me constrains me.
Pakuti ndili nawo mawu ambiri, ndipo mtima wanga ukundikakamiza;
19 Look, my breast is as wine which has no vent; like new wineskins it is ready to burst.
mʼkati mwanga ndili ngati botolo lodzaza ndi vinyo, ngati matumba a vinyo watsopano amene ali pafupi kuphulika.
20 I will speak, that I may be refreshed. I will open my lips and answer.
Ndiyenera kuyankhula kuti mtima utsike; ndiyenera kutsekula pakamwa panga ndi kuyankha.
21 Please do not let me respect any man's person, neither will I give flattering titles to any man.
Sindidzakondera munthu wina aliyense, kapena kuyankhula zoshashalika,
22 For I do not know how to give flattering titles; or else my Maker would soon take me away.
pakuti ndikanakhala wa luso loyankhula moshashalika, Mlengi wanga akanandilanga msanga.”

< Job 32 >