< Job 17 >

1 "My spirit is consumed. My days are extinct, And the grave is ready for me.
“Mtima wanga wasweka, masiku anga atha, manda akundidikira.
2 Surely there are mockers with me. My eye dwells on their provocation.
Ndithudi, anthu ondiseka andizungulira; maso anga akupenyetsetsa mdani wanga.
3 "Now give a pledge, be collateral for me with yourself. Who is there who will strike hands with me?
“Inu Mulungu, patseni chikole chimene mukufuna. Ndani wina amene adzandiperekera ine chikole?
4 For you have hidden their heart from understanding, Therefore you shall not exalt them.
Inu mwatseka maganizo awo kuti asamvetse zinthu; choncho simudzawalola kuti apambane.
5 He who denounces his friends for a prey, Even the eyes of his children shall fail.
Ngati munthu apereka mnzake chifukwa cha chuma, ana ake sadzaona mwayi.
6 "But he has made me a byword of the people. They spit in my face.
“Mulungu wandisandutsa chisudzo chochiseka aliyense, munthu amene anthu amalavulira malovu nkhope yake.
7 My eye also is dim by reason of sorrow. All my members are as a shadow.
Mʼmaso mwanga mwada ndi chisoni; ndawonda ndi mutu womwe.
8 Upright men shall be astonished at this. The innocent shall stir up himself against the godless.
Anthu olungama akudabwa nazo zimenezi; anthu osachimwa akupsera mtima anthu osapembedza Mulungu.
9 Yet shall the righteous hold on his way. He who has clean hands shall grow stronger and stronger.
Komabe anthu olungama adzasunga njira zawo, ndipo anthu a makhalidwe abwino mphamvu zawo zidzanka zikuchuluka.
10 But as for you all, come on now again; I shall not find a wise man among you.
“Tsono bwerani nonsenu, bwerezaninso mawu anuwo, sindidzapezapo munthu wanzeru pakati panupo.
11 My days are past, my plans are broken off, as are the thoughts of my heart.
Masiku anga atha, zimene ndinakonza zalephereka, pamodzinso ndi zokhumba za mtima wanga.
12 They change the night into day, saying 'The light is near' in the presence of darkness.
Anthu awa amasandutsa usiku kukhala usana, nthawi ya usiku iwo amati ‘kwatsala pangʼono kucha.’
13 If I look for Sheol as my house, if I have spread my couch in the darkness, (Sheol h7585)
Ngati nyumba imene ndikuyiyembekezera ndi manda, ngati ndiyala bedi langa mu mdima, (Sheol h7585)
14 If I have said to corruption, 'You are my father;' to the worm, 'My mother,' and 'my sister;'
ngati ndinena kwa dzenje la manda ‘ndinu abambo anga,’ ndiponso kwa mphutsi kuti, ‘ndinu amayi anga’ kapena ‘mlongo wanga,’
15 where then is my hope? As for my hope, who shall see it?
tsono chiyembekezo changa chili kuti? Ndani angaone populumukira panga?
16 Shall it go down with me to the gates of Sheol, or descend together into the dust?" (Sheol h7585)
Ndithu sindidzakhalanso ndi chiyembekezo chilichonse, polowa mʼmanda, pamene ndidzatsikira ku fumbi.” (Sheol h7585)

< Job 17 >