< Job 12 >

1 Then Job answered,
Pamenepo Yobu anayankha kuti,
2 "No doubt, but you are the people, and wisdom shall die with you.
“Ndithudi inuyo ndinu anthu ndipo nzeru zanu zidzafera nanu pamodzi!
3 But I have understanding as well as you; I am not inferior to you. Yes, who doesn't know such things as these?
Koma inenso ndili nazo nzeru ngati inu; ineyo sindine munthu wamba kwa inu. Ndani amene sadziwa zonse zimene mwanenazi?
4 I am like one who is a joke to his neighbor, I, who called on God, and he answered. The just, the blameless man is a joke.
“Ndasanduka chinthu choseketsa kwa abwenzi anga, ngakhale ndinkapemphera kwa Mulungu ndipo Iye ankandiyankha. Ine ndasanduka chinthu chongoseketsa, ngakhale ndili wolungama ndi wosalakwa!
5 In the thought of him who is at ease there is contempt for misfortune. It is ready for them whose foot slips.
Anthu amene ali pabwino amanyoza anzawo amene ali pa tsoka. Tsokalo limagwa pa amene wayamba kale kugwa.
6 The tents of robbers prosper. Those who provoke God are secure, who carry their god in their hands.
Nyumba za anthu achifwamba zimakhala pa mtendere, ndipo anthu amene amaputa Mulungu amakhala pabwino, amene amanyamula milungu yawo mʼmanja.
7 "But ask the animals, now, and they shall teach you; the birds of the sky, and they shall tell you.
“Koma funsa nyama zakuthengo ndipo zidzakuphunzitsa, kapena mbalame zamumlengalenga ndipo zidzakuwuza;
8 Or speak to the earth, and it shall teach you. The fish of the sea shall declare to you.
kapena uyankhule ndi dziko lapansi ndipo lidzakuphunzitsa, kapena ulole nsomba zamʼnyanja kuti zikufotokozere.
9 Who doesn't know that in all these, the hand of YHWH has done this,
Kodi mwa zonsezi ndi chiti chimene sichidziwa kuti lachita zimenezi ndi dzanja la Yehova?
10 in whose hand is the life of every living thing, and the breath of all humankind?
Mʼmanja mwake ndi mʼmene muli moyo wa cholengedwa chilichonse, ndiponso moyo wa anthu a mitundu yonse.
11 Doesn't the ear try words, even as the palate tastes its food?
Kodi khutu sindiye limene limamva mawu monga mmene lilime limalawira chakudya?
12 With aged men is wisdom, in length of days understanding.
Kodi nzeru sipezeka pakati pa anthu okalamba? Kodi moyo wautali sumabweretsa nzeru zomvetsa zinthu?
13 "With him is wisdom and might. He has counsel and understanding.
“Kwa Mulungu ndiye kuli nzeru ndi mphamvu; uphungu ndi kumvetsa zinthu ndi zake.
14 Look, he breaks down, and it can't be built again. He imprisons a man, and there can be no release.
Chimene Iye wapasula palibe angachimangenso. Akatsekera munthu mʼndende palibe angamutulutse.
15 Look, he withholds the waters, and they dry up. Again, he sends them out, and they overturn the earth.
Iyeyo akamanga mvula dziko limawuma; akamasula mvulayo, madzi amasefukira pa dziko.
16 With him is strength and wisdom. The deceived and the deceiver are his.
Kwa Iye kuli mphamvu ndi kupambana; munthu wopusitsidwa ndiponso wopusitsa onse ali mu ulamuliro wake.
17 He leads counselors away stripped. He makes judges fools.
Iye amalanda aphungu nzeru zawo ndipo amapusitsa oweruza.
18 He loosens the bond of kings. He binds their waist with a belt.
Iye amachotsa zingwe zimene mafumu anawamanga nazo ndipo amawamanga lamba mʼchiwuno mwawo.
19 He leads priests away stripped, and overthrows the mighty.
Iye amasocheretsa ansembe atawalanda nzeru zawo ndipo amagonjetsa anthu amphamvu amene ndi okhazikika.
20 He removes the speech of those who are trusted, and takes away the understanding of the elders.
Iye amakhalitsa chete aphungu odalirika ndipo amalanda chidziwitso cha anthu akuluakulu.
21 He pours contempt on princes, and loosens the belt of the strong.
Iye amanyoza anthu otchuka ndipo anthu anyonga amawatha mphamvu.
22 He uncovers deep things out of darkness, and brings out to light the shadow of death.
Iye amatulutsira poyera zinthu zozama za mu mdima ndipo mdima wandiweyaniwo amawusandutsa kuwala.
23 He increases the nations, and he destroys them. He enlarges the nations, and he leads them captive.
Iye amakuza mitundu ya anthu ndipo amayiwononganso; amachulukitsa mitundu ya anthu ndipo amayimwazanso.
24 He takes away understanding from the chiefs of the people of the earth, and causes them to wander in a wilderness where there is no way.
Iye amalanda nzeru za atsogoleri a dziko lapansi; amawayendetsa mʼthengo mopanda njira.
25 They grope in the dark without light. He makes them stagger like a drunken man.
Iwo amafufuzafufuza njira mu mdima wopanda chowunikira; Iye amawayendetsa dzandidzandi ngati oledzera.

< Job 12 >